< Yoswa 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
Derefter sagde HERREN til Josua: "Frygt ikke og vær ikke bange! Tag alt Krigsfolket med dig, bryd op og drag mod Aj! Se, jeg giver Kongen af Aj og hans Folk, hans By og hans Land i din Hånd!
2 Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
Og du skal gøre det samme ved Aj og dets Konge, som du gjorde ved Jeriko og dets Konge; men Godset, I røver der, må I selv beholde som Bytte, ligeledes Kvæget der. Læg Baghold vesten for Byen!"
3 Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
Derpå brød Josua op og drog med alt Krigsfolket op mod Aj; og Josua udvalgte sig 30000 tapre Mænd og sendte dem bort om Natten,
4 nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
idet han bød dem: "Se, I skal lægge eder i Baghold vesten for Byen, ikke for langt fra den, og hold eder alle rede.
5 Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
Jeg og alle de Folk, som er med mig, vil nærme os Byen, og når de gør Udfald imod os ligesom forrige Gang, flygter vi for dem.
6 Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
Når de så følger efter os så langt, at vi får dem lokket bort fra Byen, idet de tænker, at vi flygter for dem ligesom forrige Gang,
7 inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
skal I bryde frem fra Bagholdet og tage Byen, thi HERREN eders Gud vil give den i eders Hånd.
8 Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
Og når I har indtaget byen, skal I stikke den i Brand. Således skal I gøre, det er mit Bud til eder!"
9 Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
Derpå sendte Josua dem bort, og de gik hen og lagde sig i Baghold mellem Betel og Aj, vesten for Aj; men Josua blev den Nat iblandt Krigsfolket.
10 Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
Tidligt næste Morgen mønstrede Josua Folket, og sammen med Israels Ældste drog han op til Aj i Spidsen for Folket.
11 Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
Hele den Styrke, som var med ham, rykkede nærmere, til de havde Byen foran sig; og de lejrede sig norden for Aj med Dalen mellem sig og Aj.
12 Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
Derpå tog han henved 5000 Mand og lagde dem i Baghold mellem Betel og Aj, vesten for Byen;
13 Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
og Krigerne blev bragt i Stilling, hele Hæren, som var norden for Byen, og den Del, som lå i Baghold vesten for Byen; men Josua begav sig om Natten ned i Dalen.
14 Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
Da nu Kongen af Aj så det, skyndte Byens Mænd sig og rykkede tidligt om Morgenen ud til Kamp mod Israel, Kongen med hele sin Styrke, til Skråningen, hvor Lavningen begynder, uden at vide af, at der var lagt Baghold imod ham vesten for Byen;
15 Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
og da Josua og hele Israel lod sig slå på Flugt af dem og flygtede ad Ørkenen til,
16 Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
blev alt Folket i Byen stævnet sammen til at forfølge dem, og de forfulgte Josua og lod sig lokke bort fra Byen;
17 Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
ikke een Mand blev tilbage i Aj, men alle drog de ud for at forfølge Israel, og de lod Byen stå åben, medens de forfulgte Israel.
18 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
Da sagde HERREN til Josua: "Ræk Spydet i din Hånd ud mod Aj; thi jeg giver det i din Hånd!" Og Josua rakte Spydet i sin Hånd ud mod Byen.
19 Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
Og Bagholdet brød hurtigt op fra sin Plads og løb hen til Byen, da han rakte Hånden ud, indtog den og skyndte sig at stikke den i Brand.
20 Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
Da Mændene fra Aj vendte sig om og så Røgen fra Byen stige op mod Himmelen, var de ude af Stand til at flygte til nogen af Siderne, idet Folket, som var flygtet ad Ørkenen til, vendte sig om mod deres Forfølgere.
21 Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
Og da Josua og hele Israel så, at Bagholdet havde indtaget Byen, og at Røgen fra byen steg til Vejrs, vendte de om og slog Mændene fra Aj;
22 Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
og da hine rykkede ud fra Byen imod dem, kom de midt ind imellem Israeliternes to Afdelinger, som huggede dem ned uden at lade en eneste af dem undkomme eller slippe bort.
23 kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
Men Kongen af Aj fangede de levende og bragte ham til Josua.
24 Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
Da Israel nu havde hugget alle Ajs Indbyggere ned på åben Mark, på Skråningen, hvor de forfulgte dem, og de alle til sidste Mand var faldet for Sværdet, vendte hele Israel tilbage til Aj og slog det med Sværdet.
25 Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
Alle de, der faldt på den Dag, Mænd og Kvinder, udgjorde 12000, alle Indbyggerne i Aj.
26 Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
Og Josua trak ikke sin Hånd med det udrakte Spyd tilbage, før han havde lagt Band på alle Ajs Indbyggere.
27 Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
Kun Kvæget og Godset, de røvede i denne By, beholdt Israeliterne som Bytte efter den Befaling, HERREN havde givet Josua.
28 Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
Og Josua stak Aj i Brand og gjorde den til en Ruinhob for bestandig, til den Ødemark, den er den Dag i Dag.
29 Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
Men Kongen af Aj hængte han på en Pæl og lod ham hænge til Aften; og da Solen gik ned, tog man på Josuas Befaling hans Lig ned af Pælen og kastede det hen ved Indgangen til Byens Port. Og man opkastede over ham en stor Stendysse, som står der den Dag i Dag.
30 Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
Da byggede Josua HERREN, Israels Gud, et Alter på Ebals Bjerg,
31 Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
som HERRENs Tjener Moses havde pålagt Israeliterne, i Overensstemmelse med, hvad der står skrevet i Moses's Lovbog, et Alter af utilhugne Sten, hvor over der ikke var svunget Jern; og de bragte HERREN Brændofre og ofrede Takofre der.
32 Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
Og han skrev der på Stenene i Israeliternes Påsyn en Afskrift af Mose Lov, som denne havde skrevet,
33 Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
idet hele Israel og dets Ældste, Tilsynsmænd og Dommere stod på begge Sider af Arken lige over for Levitpræsterne, som bar HERRENs Pagts Ark, de fremmede såvel som de indfødte, den ene Halvdel hen imod Garizims Bjerg, den anden Halvdel hen imod Ebals Bjerg, således som HERRENs Tjener Moses forhen havde påbudt at velsigne Israels Folk.
34 Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
Så oplæste han alle Lovens Ord, Velsignelsen og Forbandelsen, alt som det var skrevet i Lovbogen;
35 Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.
ikke et Ord af alt, hvad Moses havde påbudt, undlod Josua at op læse for hele Israels Menighed, Mændene, Kvinderne og Børnene og de fremmede, som var draget med iblandt dem.

< Yoswa 8 >