< Yoswa 7 >
1 Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
Mais les enfants d'Israël commirent une infidélité à l'égard des choses consacrées, car Acan, fils de Carmi, fils de Zabdi, fils de Zérach, de la tribu de Juda, prit des choses consacrées. C'est pourquoi la colère de Yahvé s'enflamma contre les enfants d'Israël.
2 Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
Josué envoya des hommes de Jéricho à Aï, qui est à côté de Beth Aven, à l'est de Béthel, et leur parla ainsi: « Montez et explorez le pays. » Les hommes montèrent et découvrirent Aï.
3 Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
Ils revinrent vers Josué et lui dirent: « Que tout le peuple ne monte pas, mais que deux ou trois mille hommes environ montent et frappent Aï. Ne fais pas travailler tout le peuple, car il n'y en a qu'un petit nombre. »
4 Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
Environ trois mille hommes du peuple montèrent et s'enfuirent devant les hommes d'Aï.
5 Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
Les gens d'Aï frappèrent environ trente-six hommes d'entre eux. Ils les poursuivirent depuis devant la porte jusqu'à Shebarim, et les frappèrent à la descente. Le cœur du peuple se fondit, et devint comme de l'eau.
6 Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
Josué déchira ses vêtements et tomba par terre, sur sa face, devant l'arche de Yahvé, jusqu'au soir, lui et les anciens d'Israël, et ils se mirent de la poussière sur la tête.
7 Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
Josué dit: « Hélas, Seigneur Yahvé, pourquoi as-tu fait passer le Jourdain à ce peuple, pour nous livrer entre les mains des Amoréens et nous faire périr? J'aurais voulu que nous soyons satisfaits et que nous vivions au-delà du Jourdain!
8 Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
Oh, Seigneur, que dirai-je, après qu'Israël aura tourné le dos devant ses ennemis?
9 Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
Car les Cananéens et tous les habitants du pays l'apprendront, ils nous entoureront et retrancheront notre nom de la terre. Que feras-tu pour ton grand nom? »
10 Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
Yahvé dit à Josué: « Lève-toi! Pourquoi es-tu tombé sur ta face comme cela?
11 Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
Israël a péché. Ils ont même transgressé l'alliance que je leur avais prescrite. Ils ont même pris des choses consacrées, ils ont volé, ils ont trompé. Ils ont même mis cela parmi leurs propres affaires.
12 Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
C'est pourquoi les enfants d'Israël ne peuvent pas se tenir debout devant leurs ennemis. Ils tournent le dos devant leurs ennemis, parce qu'ils se sont dévoués pour la destruction. Je ne serai plus avec vous, à moins que vous ne détruisiez les choses consacrées du milieu de vous.
13 “Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
Levez-vous! Sanctifiez le peuple, et dites: « Sanctifiez-vous pour demain, car Yahvé, le Dieu d'Israël, dit: « Il y a parmi toi, Israël, une chose dévouée. Tu ne pourras pas tenir devant tes ennemis tant que tu n'auras pas ôté du milieu de toi cette chose dévouée. »
14 “Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
Dès le matin, on vous fera approcher par vos tribus. La tribu choisie par Yahvé s'approchera par familles. La famille choisie par l'Éternel s'approchera des ménages. Le foyer choisi par l'Éternel s'approchera de l'homme par l'homme.
15 Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
Celui qui aura pris la chose dévouée sera brûlé au feu, lui et tout ce qui lui appartient, parce qu'il a transgressé l'alliance de Yahvé et parce qu'il a commis une infamie en Israël.'"
16 Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
Josué se leva de bon matin et fit approcher Israël selon ses tribus. Il choisit la tribu de Juda.
17 Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
Il fit approcher la famille de Juda, et il choisit la famille des Zérachites. Il fit approcher la famille des Zérachites homme par homme, et Zabdi fut choisi.
18 Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
Il fit approcher sa famille homme par homme, et Akan, fils de Carmi, fils de Zabdi, fils de Zérah, de la tribu de Juda, fut choisi.
19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
Josué dit à Acan: « Mon fils, rends gloire à Yahvé, le Dieu d'Israël, et confesse-toi à lui. Dis-moi maintenant ce que tu as fait! Ne me le cache pas! »
20 Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
Acan prit la parole devant Josué et dit: « J'ai vraiment péché contre Yahvé, le Dieu d'Israël, et voici ce que j'ai fait.
21 Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
Lorsque j'ai vu parmi le butin une belle robe babylonienne, deux cents sicles d'argent, et un coin d'or pesant cinquante sicles, je les ai convoités et je les ai pris. Voici qu'ils sont cachés dans le sol, au milieu de ma tente, avec l'argent en dessous. »
22 Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
Josué envoya des messagers, et ils coururent à la tente. Et voici, il était caché dans sa tente, avec l'argent en dessous.
23 Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
Ils les prirent au milieu de la tente et les apportèrent à Josué et à tous les enfants d'Israël. Ils les déposèrent devant Yahvé.
24 Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
Josué, et tout Israël avec lui, prit Acan, fils de Zérach, l'argent, la robe, le coin d'or, ses fils, ses filles, son bétail, ses ânes, ses brebis, sa tente et tout ce qui lui appartenait, et ils les firent monter dans la vallée d'Acor.
25 Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
Josué dit: « Pourquoi nous avez-vous inquiétés? C'est Yahvé qui va te troubler aujourd'hui. » Tout Israël le lapida, et ils les brûlèrent au feu et les lapidèrent.
26 Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.
Ils élevèrent au-dessus de lui un grand monceau de pierres qui subsiste encore aujourd'hui. Yahvé se détourna de l'ardeur de sa colère. C'est pourquoi le nom de ce lieu a été appelé jusqu'à ce jour « vallée d'Acor ».