< Yoswa 7 >

1 Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
Forsothe the sones of Israel braken `the comaundement, and mystoken of the halewid thing; for Achar, the son of Charmy, sone of Zabdi, sone of Zare, of the lynage of Juda, toke sum thing of the halewid thing; and the Lord was wrooth ayens the sones of Israel.
2 Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
And whanne Josue sente men fro Jerico ayens Hai, which is bisidis Bethauen, at the eest coost of the citee Bethel, he seide to hem, Stie ye, and aspie ye the lond. Whiche filliden `the comaundementis, and aspieden Hay;
3 Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
and thei turneden ayen, and seiden to hym, `Not al the puple stie, but twey ether thre thousynde of men go, and do awei the citee; whi schal al the puple be trauelid in veyn ayens feweste enemyes?
4 Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
Therfor thre thousynde of fiyteris stieden, whiche turneden the backis anoon,
5 Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
and weren smytun of the men of Hay; and sixe and thretti men of hem `felden doun; and aduersaries pursueden hem fro the yate til to Saberym; and thei felden doun fleynge bi lowe places. And the herte of the puple dredde, and was maad vnstidefast at the licnesse of watir.
6 Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
Sotheli Josue torente hise clothis, and felde lowe to the erthe bifor the arke of the Lord, `til to euentid, as wel he, as alle the elde men of Israel; and thei castiden powdir on her heedis.
7 Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
And Josue seide, Alas! alas! Lord God, what woldist thou lede this puple ouer the flood Jordan, that thou schuldist bitake vs in the hond of Ammorrey, and schulde leese vs? Y wolde, that as we bygunnen, we hadden dwellid biyondis Jordan.
8 Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
My Lord God, what schal Y seie, seynge Israel turnynge the backis to hise enemyes?
9 Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
Cananeys, and alle dwelleris of the lond schulen here, and thei schulen be gaderid togidere, and schulen cumpas vs, and schulen do awei oure name fro erthe; and what schalt thou do to thi grete name?
10 Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
And the Lord seide to Josue, Rise thou; whi liggist thou low in the erthe?
11 Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
Israel synnede, and brak my couenaunt; and thei token of the halewid thing, and thei han stole, and lieden, and hidden among her vessels.
12 Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
And Israel may not stonde bifore hise enemyes, and Israel schal fle hem, for it is defoulid with cursyng; Y schal no more be with you, til ye al to breke hym which is gilti of this trespas.
13 “Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
Rise thou, halewe the puple, and seie thou to hem, Be ye halewid ayens to morewe; for the Lord God of Israel seith these thingis, A! Israel! cursyng is in the myddis of thee; thou schalt not mowe stonde bifor thin enemyes, til he that is defoulyd bi this trespas, be doon awei fro thee.
14 “Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
And ye schulen come eerli, alle men bi youre lynagis; and whateuer lynage the lot schal fynde, it schal come bi hise meynees; and the meynee schal come bi housis, and the hous schal come bi men.
15 Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
And whoeuer schal be takun with this trespas, he schal be brent bi fier with al his catel, for he brak the couenaunt of the Lord, and dide vnleueful thing in Israel.
16 Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
Therfor Josue roos eerly, and settide in ordre Israel, bi hise lynagis; and the lynage of Juda was foundun;
17 Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
and whanne that lynage was brouyt forth bi hise meynees, the meyne of Zare was foundun. And Josue brouyte forth it bi men, ethir housis, and foond Zabdi;
18 Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
whos hows he departide in to alle men bi hemsilf; and he foond Achar, the sone of Charmy, sone of Zabdi, sone of Zare, of the lynage of Juda.
19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
And he seide to Achar, My sone, yyue thou glorie to the Lord God of Israel, and knowleche thou, and schew to me what thou hast do; hide thou not.
20 Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
And Achar answeryde to Josue, and seide to hym, Verily, Y synnede bifor the Lord God of Israel, and Y dide `so and so;
21 Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
for among the spuylis Y siy a reed mentil ful good, and two hundrid siclis of siluer, and a goldun reule of fifti siclis; and Y coueytide, and took awei, and hidde in the erthe, ayens the myddis of my tabernacle; and Y hilide the siluer with erthe doluun.
22 Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
Therfor Josue sente mynystris, whyche runnen to his tabernacle, and foundun alle thingis hid in the same place, and the siluer togidere; and thei token awei fro the tente,
23 Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
and brouyten `tho thingis to Josue, and to alle the sones of Israel; and thei castiden forth bifor the Lord.
24 Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
Therfor Josue took Achar, the sone of Zare, and the siluer, and the mentil, and the goldun reule, and hise sones, and douytris, oxun, assis, and scheep, and the tabernacle `it silf, and al the purtenaunce of household, and al Israel with Josue; and thei ledden hem to the valei of Achar;
25 Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
where Josue seide, For thou disturblidist vs, the Lord schal disturble thee in this dai. And al Israel stonyde hym; and alle thingis that weren hise, weren wastid bi fier.
26 Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.
And thei gaderiden on hym a greet heep of stoonys, whiche dwellen til in to present day. And the strong veniaunce of the Lord was turned awei fro hem; and the name of that place was clepid the valey of Achar `til to day.

< Yoswa 7 >