< Yoswa 7 >

1 Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
Hina Gode da Isala: ili dunuma ilia da liligi huluanedafa wadela: lesima: ne amola Ema ilegei liligi mae wamolama: ne sia: i dagoi. Be ilia da Ea sia: hame nabi. Dunu ea dio amo A: iga: ne da liligi wamolai dagoi. (A: iga: ne da Gami egefe amola Sa: badai ea aowa. E da Sila sosogo fi Yuda fi amo ganodini esalu.)
2 Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
Yosiua da asunasiba: le, Isala: ili desega ahoasu dunu da Yeligou fisili, A:iai moilai bai bagade (Bedele moilai ea eso mabadi la: idi diala, Beda: ifene moilai gadenei) amo ea hou hogola asi. Ba: lalu,
3 Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
ilia da Yosiuama buhagili, amane sia: i, “A: iai da moilai bai fonobahadi fawane. Dadi gagui dunu huluane amoga doagala: musa: , mae asunasima. 3000 o 2000 dunu amo fawane da amo moilai wadela: lesimu da defea.”
4 Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
Amaiba: le, Isala: ili dadi gagui dunu 3000 agoane da A: iai moilaiga doagala: musa: asi. Be ilia se nabi, amola beba: le bu hobea: i.
5 Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
A: iai dunu da moilai bai bagade gagoi logo ga: su amoga ilima gegene, ili sefasili igi lamu sogebi amoga sefasi. Isala: ili dunu da agoloba: le sa: ili hobeale, A:iai dunu da Isala: ili dunu 36amo medole legei. Amalalu, Isala: ili dunu da ilia gasa fisili bagadewane beda: i.
6 Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
Yosiua amola Isala: ili dunu da se nababeba: le, ilia abula gadelale, Hina Gode Ea Gousa: su Sema Gagili midadi osoboga diasa: i. Ilia da: i dioi olelema: ne, ilia dialuma amo osobo gulu amoga dedebole amo esoga osoboga diasa: i dialu.
7 Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
Amola Yosiua da amane sia: i, “Hinadafa Gode! Dia da abuliba: le nini Yodane Hano degema: ne oule misibala: ? Nini A: moulaide dunu amoga wadela: musa: oule misibala: ? Ninia Yodane Hano na: iyado bega: esalumu da defea galu.
8 Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
Hina Gode! Isala: ili dunu da ilima ha lai dunu amoga hobea: iba: le, na da adi sia: ma: bela: ?
9 Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
Ga: ina: ne dunu amola dunu huluane amo soge ganodini esala da amo sia: nababeba: le, nini sisiga: le, nini huluane medole legemu. Amasea, ninia da Dia Dio nodone gaga: ma: ne, Dia da adi hamoma: bela: ?”
10 Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
Be Hina Gode da Yosiuama amane sia: i, “Wa: legadoma! Di da abuliba: le osoboga udigili diahala: ?
11 Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
Isala: ili fi da wadela: le hamoi dagoi. Ilia da Na Gousa: su amo ilia noga: le bobogema: ne Na sia: i, amo wadela: lesi dagoi. Ilia da liligi mogili Nama gobele sanasimusa: ilegei, amo lai dagoi. Ilia da wamolai amola ogogoi, amola liligi wamolai amo ilia liligi ganodini sali.
12 Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
Amaiba: le, Isala: ili dunu da ilima ha lai dunuma hasalimu gogolesa. Ilia da beba: le hobeasa. Bai ilisu da wali wadela: musa: ilegei dagoi. Amo liligi wamolai dilia hame fadegale fasisia, Na da dili hame sigi masunu.
13 “Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
Wale gadoma! Dunu huluane da Nama misa: ne, ilia dodofema: ne sia: ma. Dilia da amo liligi hame fadegale fasisia, dilia da dilima ha lai ilima gegemu da hamedei agoane ba: mu.
14 “Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
Hahabe dilia fi afae afae Nama oule misa. Na da fi afae ilegemu. Amo fi ilegei da sosogo fi afae afae Nama oule misa: ne sia: ma. Amasea, na da dunu afae ilegemu.
15 Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
Amo dunu Na da wamolasu dunu ilegemu. Amo dunu amola ea sosogo fi amola ea liligi huluane, laluga gobesima. Bai e da Na Gousa: su wadela: lesi dagoi, amola gogosiasu bagade Isala: ili fi ilima i.”
16 Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
Hahabedafa, Yosiua da Isala: ili dunu huluane fi afae afae oule misini, Yuda fi da ilegei dagoi ba: i.
17 Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
E da Yuda fi amo ganodini afae afae amo oule misini, Sila ea fi ilegei dagoi ba: i. Amo da sosogo fi afae afae misini, Sa: badai ea sosogo fi ilegei dagoi ba: i.
18 Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
Amalalu, Yosiua da Sa: badai ea sosogo fi dunu afae afae oule misini, A:iga: ne (Gami egefe amola Sa: badai ea aowa) amo ilegei dagoi ba: i.
19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
Yosiua da A: iga: nema amane sia: i, “Na gofe! Isala: ili Hina Gode ba: ma: ne, dafawane sia: olelema. Dia hamoi olelema. Nama amo hou mae wamolegema.”
20 Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
A: iga: ne da bu adole i, “Dafawane! Na Isala: ili Hina Godema wadela: le hamoi. Na da agoane hamoi.
21 Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
Ninia liligi lai amo ganodini, na da Ba: balounia abula, silifa2gilogala: me agoane amola gouli 1/2 gilogala: me baligi amo ba: i dagoi. Na da amo bagade hanaiba: le, lai dagoi. Dilia da na abula diasu ganodini amo liligi uli dogoi ganodini wamolegei dagoi ba: mu. Silifa da eno liligi hagudu dialebe ba: mu.”
22 Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
Amaiba: le, Yosiua da dunu mogili asunasi. Ilia da hehenane, wamolai liligi amo A: iga: ne ea abula diasu ganodini wamolegei dagoi ba: i. Amola silifa da hagudu dialebe ba: i.
23 Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
Amo liligi huluane ilia da A: iga: ne abula diasuga gadili gaguli asili, Yosiua amola Isala: ili dunu huluane da gaguli asili, Hina Gode ba: ma: ne ligisi.
24 Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
Yosiua amola Isala: ili dunu huluane da A: iga: ne, silifa, abula, gouli amola A: iga: ne ea dunu amola uda mano huluane, ea bulamagau, ea dougi, ea sibi amola ea abula diasu amo gaguli, Bidi Hamosu Fago sogebiga hiouginana asi.
25 Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
Amola Yosiua da amane sia: i, “Dia da abuliba: le amo se nabasu ninima iaha. Hina Gode da wali dima se imunu.” Amalalu, dunu huluane da A: iga: ne igiga medole legei. Ilia da ea sosogo fi amola ea liligi huluane igiga medole lelegele, laluga gobesi.
26 Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.
Ilia da ea da: i hodo amo igi ligisisu bagade amoga dedeboi. Amo igi ligisisu da wali eso dialebe. Amaiba: le, amo fago sogebi ea dio da wali Bidi Hamosu Fago. Amalalu, Hina Gode da Ea gia: i bagade ougi fisi.

< Yoswa 7 >