< Yoswa 6 >

1 Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
Or, Jéricho était fermée et fortifiée, dans la crainte des enfants d’Israël, et nul n’osait sortir ou entrer.
2 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
Et le Seigneur dit à Josué: Voici que j’ai livré en la main Jéricho et son roi et tous ses braves guerriers.
3 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
Faites le tour de la ville, vous tous combattants, une fois par jour. Ainsi ferez-vous pendant six jours.
4 Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
Mais, au septième jour, que des prêtres portent sept trompettes dont on fait usage pendant le Jubilé, et qu’ils précèdent l’arche de l’alliance; et sept fois vous ferez le tour de la ville, et les prêtres sonneront des trompettes.
5 Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
Et lorsque le son de la trompette se fera entendre, d’abord prolongé, puis entrecoupé, et qu’il retentira à vos oreilles, tout le peuple ensemble poussera les plus grands cris, et les murailles de la ville s’écrouleront jusqu’aux fondements, et chacun entrera par l’endroit vis-à-vis duquel il se trouvera.
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
Josué, fils de Nun, appela donc les prêtres et leur dit: Portez l’arche de l’alliance, et que sept autres prêtres portent sept trompettes du jubilé, et qu’ils marchent devant l’arche du Seigneur.
7 Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
Au peuple aussi il dit: Allez, et faites le tour de la ville, armés, précédant l’arche du Seigneur.
8 Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
Or, lorsque Josué eut achevé ces paroles, et que les sept prêtres sonnaient des sept trompettes devant l’arche de l’alliance du Seigneur,
9 Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
Et que toute la troupe armée précédait, le reste du peuple suivait l’arche, et tout retentissait du son des trompettes.
10 Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
Or, Josué avait commandé au peuple, disant: Vous ne crierez point, et votre voix ne sera point entendue, et aucun mot ne sortira de votre bouche, jusqu’à ce que vienne le jour auquel je vous dirai: Criez et vociférez.
11 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
L’arche du Seigneur fit donc une fois le tour de la ville pendant le jour, et, revenue au camp, elle y demeura.
12 Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
Mais Josué s’étant levé durant la nuit, les prêtres portèrent l’arche du Seigneur,
13 Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
Et sept d’entre eux, les sept trompettes dont on fait usage dans le jubilé; et ils précédaient l’arche du Seigneur, marchant et sonnant des trompettes, et le peuple armé allait devant eux, et le reste du peuple suivait l’arche et sonnait des trompettes.
14 Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
Et le second jour ils firent le tour de la ville une fois, puis ils revinrent dans le camp. Ainsi firent-ils pendant six jours.
15 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
Mais le septième jour, se levant dès l’aurore, ils firent le tour de la ville, comme il leur avait été ordonné, sept fois.
16 Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
Et lorsqu’au septième tour, les prêtres sonnaient de la trompette, Josué dit à tout Israël: Poussez de grands cris; car le Seigneur vous a livré la ville.
17 Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
Et que cette ville soit anathème, et que tout ce qui s’y trouve, soit consacré au Seigneur; que la seule Rahab, la femme de mauvaise vie, vive avec tous ceux qui sont à elle dans sa maison; car elle a caché les messagers que nous avons envoyés.
18 Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
Mais vous, prenez garde que vous ne touchiez à aucune des choses qui vous ont été défendues, que vous ne soyez coupables de prévarication, et que tout le camp d’Israël ne soit sous le péché, et n’éprouve de la disgrâce.
19 Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
Ainsi, que tout ce qu’il y aura d’or et d’argent, et de vases d’airain et de fer, soit consacré au Seigneur et déposé dans ses trésors.
20 Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
Tout le peuple donc poussant de grands cris, et les trompettes sonnant, quand la voix et le son eurent retenti aux oreilles de la multitude, les murs soudain s’écroulèrent, chacun monta par le lieu qui était vis-à-vis de lui, et ils prirent la ville.
21 Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
Et ils tuèrent tout ce qui s’y trouvait, depuis l’homme jusqu’à la femme, depuis l’enfant jusqu’au vieillard. Les bœufs aussi, et les brebis et les ânes, ils les frappèrent du tranchant du glaive.
22 Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
Mais Josué dit aux deux hommes qui avaient été envoyés comme espions: Entrez dans la maison de la femme de mauvaise vie, et faites-la sortir, ainsi que tout ce qui est à elle, comme vous lui avez assuré par serment.
23 Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
Et les deux jeunes hommes étant entrés, firent sortir Rahab, son père et sa mère, ses frères aussi, tout ce qui leur appartenait et toute sa parenté, et les firent demeurer hors du camp d’Israël.
24 Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
Mais la ville et tout ce qui s’y trouvait, ils les brûlèrent, excepté l’or, l’argent, les vases d’airain et de fer, qu’ils consacrèrent pour le trésor du Seigneur.
25 Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
Quant à Rahab, la femme de mauvaise vie, à la maison de son père et à tout ce qu’elle avait, Josué leur conserva la vie, et ils ont habité au milieu d’Israël jusqu’au présent jour, parce qu’elle cacha les messagers qu’il avait envoyés pour explorer Jéricho. En ce temps-là, Josué fit une imprécation, disant:
26 Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
Maudit devant le Seigneur; l’homme qui relèvera et rebâtira la ville de Jéricho! Que ce soit sur son premier-né qu’il en jette les fondements, et que ce soit sur le dernier de ses enfants qu’il en pose les portes.
27 Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.
Le Seigneur fut donc avec Josué, et son nom se répandit sur toute la terre.

< Yoswa 6 >