< Yoswa 6 >
1 Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
Now Jericho was straitly shut up because of the children of Israel: none went out, and none came in. —
2 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
And the LORD said unto Joshua: 'See, I have given into thy hand Jericho, and the king thereof, even the mighty men of valour.
3 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
And ye shall compass the city, all the men of war, going about the city once. Thus shalt thou do six days.
4 Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
And seven priests shall bear seven rams' horns before the ark; and the seventh day ye shall compass the city seven times, and the priests shall blow with the horns.
5 Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
And it shall be, that when they make a long blast with the ram's horn, and when ye hear the sound of the horn, all the people shall shout with a great shout; and the wall of the city shall fall down flat, and the people shall go up every man straight before him.'
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
And Joshua the son of Nun called the priests, and said unto them: 'Take up the ark of the covenant, and let seven priests bear seven rams' horns before the ark of the LORD.'
7 Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
And he said unto the people: 'Pass on, and compass the city, and let the armed body pass on before the ark of the LORD.'
8 Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
And it was so, that when Joshua had spoken unto the people, the seven priests bearing the seven rams' horns before the LORD passed on, and blew with the horns; and the ark of the covenant of the LORD followed them.
9 Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
And the armed men went before the priests that blew the horns, and the rearward went after the ark, the priests blowing with the horns continually.
10 Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
And Joshua commanded the people, saying: 'Ye shall not shout, nor let your voice be heard, neither shall any word proceed out of your mouth, until the day I bid you shout; then shall ye shout.'
11 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
So he caused the ark of the LORD to compass the city, going about it once; and they came into the camp, and lodged in the camp.
12 Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
And Joshua rose early in the morning, and the priests took up the ark of the LORD.
13 Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
And the seven priests bearing the seven rams' horns before the ark of the LORD went on continually, and blew with the horns; and the armed men went before them; and the rearward came after the ark of the LORD, the priests blowing with the horns continually.
14 Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
And the second day they compassed the city once, and returned into the camp; so they did six days.
15 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
And it came to pass on the seventh day, that they rose early at the dawning of the day, and compassed the city after the same manner seven times; only on that day they compassed the city seven times.
16 Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
And it came to pass at the seventh time, when the priests blew with the horns, that Joshua said unto the people: 'Shout; for the LORD hath given you the city.
17 Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
And the city shall be devoted, even it and all that is therein, to the LORD; only Rahab the harlot shall live, she and all that are with her in the house, because she hid the messengers that we sent.
18 Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
And ye, in any wise keep yourselves from the devoted thing, lest ye make yourselves accursed by taking of the devoted thing, so should ye make the camp of Israel accursed, and trouble it.
19 Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
But all the silver, and gold, and vessels of brass and iron, are holy unto the LORD; they shall come into the treasury of the LORD.'
20 Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
So the people shouted, and the priests blew with the horns. And it came to pass, when the people heard the sound of the horn, that the people shouted with a great shout, and the wall fell down flat, so that the people went up into the city, every man straight before him, and they took the city.
21 Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
And they utterly destroyed all that was in the city, both man and woman, both young and old, and ox, and sheep, and ass, with the edge of the sword.
22 Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
And Joshua said unto the two men that had spied out the land: 'Go into the harlot's house, and bring out thence the woman, and all that she hath, as ye swore unto her.'
23 Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
And the young men the spies went in, and brought out Rahab, and her father, and her mother, and her brethren, and all that she had, all her kindred also they brought out; and they set them without the camp of Israel.
24 Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
And they burnt the city with fire, and all that was therein; only the silver, and the gold, and the vessels of brass and of iron, they put into the treasury of the house of the LORD.
25 Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
But Rahab the harlot, and her father's household, and all that she had, did Joshua save alive; and she dwelt in the midst of Israel, unto this day; because she hid the messengers, whom Joshua sent to spy out Jericho.
26 Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
And Joshua charged the people with an oath at that time, saying: 'Cursed be the man before the LORD, that riseth up and buildeth this city, even Jericho; with the loss of his first-born shall he lay the foundation thereof, and with the loss of his youngest son shall he set up the gates of it.'
27 Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.
So the LORD was with Joshua; and his fame was in all the land.