< Yoswa 6 >

1 Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
Now Jericho was closed as well as fortified, out of fear of the sons of Israel, and no one dared to depart or to enter.
2 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
And the Lord said to Joshua: “Behold, I have given Jericho into your hand, with its king and all the strong men.
3 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
Have all the warriors circle the city once each day; you shall do so for six days.
4 Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
Then, on the seventh day, the priests shall take the seven trumpets, which are used on the jubilee, and they shall precede the ark of the covenant. And you shall circle the city seven times, and the priests shall sound the trumpets.
5 Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
And when the voice of the trumpet sounds longer and with interruptions, and it increases in your ears, then all the people shall cry out together with a very great shout, and the walls of the city shall fall to the foundation, and they shall enter it, each from a place opposite where they are standing.”
6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
Then Joshua, the son of Nun, called the priests, and he said to them, “Take the ark of the covenant, and let seven other priests take the seven trumpets of the jubilee, and advance before the ark of the Lord.”
7 Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
He also said to the people, “Go, and circle the city, armed, preceding the ark of the Lord.”
8 Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
And when Joshua had finished his words, and the seven priests sounded the seven trumpets before the ark of the covenant of the Lord,
9 Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
and all the armed soldiers went ahead, the remainder of the common people followed the ark, and the sound of the trumpets grew louder everywhere.
10 Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
But Joshua had instructed the people, saying, “You shall not cry out, nor shall your voice be heard, and no word at all shall proceed from your mouth, until the day arrives on which I will say to you, ‘Cry out, and shout.’”
11 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
Thus, the ark of the Lord circled the city once each day, and returning to the camp, it remained there.
12 Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
And so, with Joshua, arising in the night, the priests took the ark of the Lord,
13 Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
and seven of them took the seven trumpets, which are used in the jubilee, and they preceded the ark of the Lord, walking and sounding the trumpets. And the armed men went before them, and the remainder of the common people followed the ark, and they were blaring the trumpets.
14 Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
And they circled the city on the second day, once, and they returned to the camp. They did so for six days.
15 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
Then, on the seventh day, rising at first light, they circled the city, just as had been ordered, seven times.
16 Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
And at the seventh circling, when the priests sounded the trumpets, Joshua said to all of Israel: “Shout! For the Lord has delivered the city to you.
17 Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
And let this city be anathema, with all the things that are within it, before the Lord. May only Rahab the harlot live, with all who are with her in the house. For she hid the messengers whom we sent.
18 Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
But you must be careful that you do not touch any of those things, as you have been instructed, for then you would be guilty of transgression, and all the camp of Israel would be under sin and would be troubled.
19 Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
But whatever gold and silver there will be, and vessels of brass or of iron, let these be consecrated to the Lord and be stored in his treasuries.”
20 Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
Therefore, with all the people shouting, and the trumpets blaring, after the voice and the sound increased in the ears of the multitude, the walls promptly fell to ruin. And each one climbed up at the place which was opposite where he was. And they seized the city.
21 Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
And they put to death all who were in it, from man even to woman, from infant even to elder. Likewise, the oxen and sheep and donkeys, they struck down with the edge of the sword.
22 Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
But Joshua said to the two men who had been sent to explore, “Enter the house of the harlot woman, and bring her out, and all the things that are hers, just as you assured her by oath.”
23 Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
And the youths entered, and they led out Rahab, and her parents, also her brothers, and all her goods and kindred, and they caused them to dwell outside the camp.
24 Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
Then they set fire to the city and all the things that were within it, except the gold and silver, and the vessels of brass or of iron, which they consecrated into the treasury of the Lord.
25 Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
Yet truly, Joshua caused Rahab the harlot, and her father’s household, and all she had, to survive. And they lived in the midst of Israel, even to the present day. For she hid the messengers, whom he had sent to explore Jericho. At that time, Joshua made an invocation, saying:
26 Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
“Cursed before the Lord is the man who will raise up and rebuild the city of Jericho! With his firstborn, may he lay its foundation, and with the last of his children, may he set up its gates.”
27 Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.
And so the Lord was with Joshua, and his name was made known throughout all the land.

< Yoswa 6 >