< Yoswa 5 >

1 Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
Lorsque tous les rois des Amoréens, qui étaient de l'autre côté du Jourdain, à l'ouest, et tous les rois des Cananéens, qui étaient près de la mer, apprirent comment Yahvé avait mis à sec les eaux du Jourdain, depuis devant les enfants d'Israël jusqu'à ce que nous ayons traversé, leur cœur se fondit, et il n'y eut plus d'esprit en eux, à cause des enfants d'Israël.
2 Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
En ce temps-là, Yahvé dit à Josué: « Fais des couteaux de silex, et circoncis de nouveau les fils d'Israël pour la seconde fois. »
3 Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
Josué se fit des couteaux de silex, et il circoncit les fils d'Israël à la colline des prépuces.
4 Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
Voici pourquoi Josué les circoncit: tout le peuple sorti d'Égypte, les mâles, tous les hommes de guerre, moururent dans le désert, en chemin, après leur sortie d'Égypte.
5 Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
Car tous ceux qui étaient sortis d'Égypte étaient circoncis, mais tous ceux qui étaient nés dans le désert, sur le chemin de la sortie d'Égypte, n'avaient pas été circoncis.
6 Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
Les enfants d'Israël marchèrent quarante ans dans le désert, jusqu'à ce que toute la nation, même les hommes de guerre qui étaient sortis d'Égypte, aient été consumés, parce qu'ils n'avaient pas écouté la voix de Yahvé. Yahvé leur jura de ne pas leur laisser voir le pays que Yahvé avait juré à leurs pères de nous donner, un pays où coulent le lait et le miel.
7 Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
Leurs enfants, qu'il suscita à leur place, furent circoncis par Josué, car ils étaient incirconcis, faute d'avoir été circoncis en chemin.
8 Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
Lorsqu'ils eurent fini de circoncire toute la nation, ils restèrent à leur place dans le camp jusqu'à ce qu'ils soient guéris.
9 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
Yahvé dit à Josué: « Aujourd'hui, je roule loin de toi l'opprobre de l'Égypte. » C'est pourquoi le nom de ce lieu a été appelé Gilgal jusqu'à ce jour.
10 Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
Les enfants d'Israël campèrent à Guilgal. Ils célébrèrent la Pâque le quatorzième jour du mois, le soir, dans les plaines de Jéricho.
11 Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
Ils mangèrent des gâteaux sans levain et des grains desséchés provenant des produits du pays le lendemain de la Pâque, le même jour.
12 Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
La manne cessa le jour suivant, après qu'ils eurent mangé des produits du pays. Les enfants d'Israël n'eurent plus de manne, mais ils mangèrent des fruits du pays de Canaan cette année-là.
13 Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
Lorsque Josué fut près de Jéricho, il leva les yeux et regarda, et voici qu'un homme se tenait devant lui, son épée tirée à la main. Josué alla vers lui et lui dit: « Es-tu pour nous, ou pour nos ennemis? ».
14 Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
Il répondit: « Non, mais je suis venu maintenant comme commandant de l'armée de l'Éternel. » Josué tomba la face contre terre, se prosterna et lui demanda: « Que dit mon seigneur à son serviteur? »
15 Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.
Le prince de l'armée de Yahvé dit à Josué: « Enlève tes sandales, car le lieu sur lequel tu te tiens est saint. « Josué fit ainsi.

< Yoswa 5 >