< Yoswa 5 >
1 Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
And it came to pass, when all the kings of the Amorites who were over the Jordan westward, and all the kings of the Canaanites who were by the sea, heard how that Yahweh had dried up the waters of the Jordan, from before the sons of Israel, until they had passed over, that their heart melted, and there was no spirit in them any more, because of the sons of Israel.
2 Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
At that time, said Yahweh unto Joshua, Make thee knives of flint, —and again circumcise the sons of Israel, a second time.
3 Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
So Joshua made him knives of flint, —and circumcised the sons of Israel, at the Hill of Foreskins.
4 Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
Now, this, is the cause why Joshua did circumcise, —all the people who came forth out of Egypt, who were males, all the men of war, died in the desert, by the way, after they came forth out of Egypt.
5 Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
For, though all the people who came forth had been circumcised, yet, all the people who were born in the desert by the way, after they came forth out of Egypt, had they not circumcised.
6 Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
Because, for forty years, did the sons of Israel journey in the desert, until all the nation who were men of war, who came forth out of Egypt, were consumed, because they hearkened not unto the voice of Yahweh, —unto whom Yahweh sware that he would not let them see the land, which Yahweh sware unto their fathers, that he would give unto us, a land flowing with milk and honey.
7 Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
Their sons, therefore, whom he had raised up in their stead, them, did Joshua circumcise, —for, uncircumcised, they were, in that they had not circumcised them by the way.
8 Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
And so it came to pass, when they had made an end of circumcising all the nation, they remained in their place, in the camp, until they were healed.
9 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
Then said Yahweh unto Joshua, To-day, have I rolled away the reproach of Egypt from off you. Wherefore the name of that place is called Gilgal ["a rolling away"]unto this day.
10 Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
Thus then the sons of Israel encamped in Gilgal, —and kept the passover on the fourteenth day of the month, in the evening, in the waste plains of Jericho.
11 Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
And they did eat of the corn of the land, on the morrow of the passover, unleavened cakes and parched ears of corn, —on this selfsame day.
12 Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
And the manna ceased on the morrow, when they had eaten of the corn of the land, neither had the sons of Israel manna any more, —so they did eat of the yield of the land of Canaan throughout that year.
13 Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
And it came to pass, while Joshua was at Jericho, that he lifted up his eyes, and looked, and lo! a man standing over against him, with his sword drawn, in his hand, —so Joshua went unto him, and said to him, For us, art thou, or for our adversaries?
14 Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
And he said—Nay, but, I, as prince of the host of Yahweh, have, now, come. So Joshua fell on his face to the earth, and worshipped, and said unto him, What is my lord speaking unto his servant?
15 Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.
Then said the prince of the host of Yahweh unto Joshua—Slip off thy sandals from thy feet, for, as for the place whereon thou art standing, holy, it is. And Joshua did so.