< Yoswa 5 >
1 Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
And it came to pass, when all the kings of the Emorites, who were on the side of the Jordan westward, and all the kings of the Canaanites, who were by the sea, heard that the Lord had dried up the waters of the Jordan from before the children of Israel, until they were passed over, that their heart melted, and there remained no more any courage in them, because of the children of Israel.
2 Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
At that time the Lord said unto Joshua, Make thee sharp knives, and circumcise again the children of Israel the second time.
3 Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
And Joshua made himself sharp knives, and circumcised the children of Israel at the hill of 'Araloth.
4 Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
And this is the cause why Joshua did circumcise: All the people that came out of Egypt, the males, all the men of war, died in the wilderness on the way, after their going forth out of Egypt.
5 Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
For all the people that came out were circumcised; but all the people that were born in the wilderness on the way at their going forth out of Egypt, they had not circumcised.
6 Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
For during forty years the children of Israel wandered in the wilderness, till there was an end of all the people, the men of war, who were come out of Egypt, who had not obeyed the voice of the Lord; unto whom the Lord had sworn that he would not let them see the land, which the Lord had sworn unto their fathers that he would give unto us, a land flowing with milk and honey.
7 Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
But their children he raised up in their stead: these did Joshua circumcise; for they were uncircumcised, because they had not circumcised them on the way.
8 Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
And it came to pass, when the whole people had all been circumcised, that they abode in their places in the camp till they were healed.
9 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
And the Lord said unto Joshua, This day have I rolled away the reproach of Egypt from off you. And he called the name of the place Gilgal unto this day.
10 Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
And the children of Israel encamped in Gilgal, and they prepared the passover-offering on the fourteenth day of the month at evening in the plains of Jericho.
11 Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
And they ate of the corn of the land on the morrow after the passover-offering, unleavened cakes and parched corn, on the selfsame day.
12 Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
And the manna ceased on the morrow after they had eaten of the corn of the land; and the children of Israel had not any more manna; but they did eat of the product of the land of Canaan during that year.
13 Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
And it came to pass, when Joshua was by Jericho, that he lifted up his eyes and looked, and, behold, a man was standing over against him with his sword drawn in his hand; and Joshua went unto him, and said to him, Art thou for us, or for our adversaries?
14 Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
And he said, No; for I am a captain of the host of the Lord: now am I come. And Joshua fell on his face to the earth, and bowed himself, and said to him, What doth my lord speak unto his servant?
15 Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.
And the captain of the Lord's host said unto Joshua, Put off thy shoe from off thy foot; for the place whereon thou standest is holy. And Joshua did so.