< Yoswa 4 >

1 Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
Cuando toda la nación había llegado al otro lado del Jordán, el Señor le dijo a Josué:
2 “Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
Toma doce hombres del pueblo, un hombre por cada tribu.
3 Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
Y diles: Toma desde el medio del Jordán, desde el lugar donde descansaban los pies de los sacerdotes, doce piedras, y llévalos contigo y colócalos en el lugar donde descansen esta noche.
4 Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
Y Josué envió a buscar a los doce hombres que él tenía preparados, uno de cada tribu de los hijos de Israel,
5 ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
Y él les dijo: Vayan delante del cofre del pacto de su Dios, en medio del Jordán, y cada uno de ustedes levanten una piedra sobre su espalda, una por cada tribu de los hijos de Israel:
6 kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
Para que esto sea señal entre ustedes; Cuando sus hijos les pregunten, ¿Cuál es la razón de estas piedras?
7 Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
Entonces les dirás: Porque las aguas del Jordán fueron cortadas delante del cofre del pacto del Señor; cuando pasó por el Jordán, se cortaron las aguas del Jordán, y estas piedras serán una señal para los hijos de Israel, que se mantendrán en su memoria para siempre.
8 Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
Entonces los hijos de Israel hicieron lo que Josué les mandó, y tomaron doce piedras del medio del Jordán, como el Señor le había dicho a Josué, una por cada tribu de los hijos de Israel; Los llevaron con ellos al lugar de descanso de la noche y los pusieron allí.
9 Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
Y Josué puso doce piedras en medio del Jordán, donde se habían colocado los pies de los sacerdotes que tomaron el cofre del pacto: y allí están hasta hoy.
10 Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
Porque los sacerdotes que tomaron el cofre del pacto permanecieron allí en el medio del Jordán hasta que todas las órdenes dadas por él Señor por medio de Josué. Todo se hizo según Moisés había mandado a Josué entonces la gente se fue rápidamente.
11 Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
Y cuando todo el pueblo llegó al otro lado, el cofre del pacto del Señor se acercó, y los sacerdotes, delante de los ojos del pueblo.
12 Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
Y los hijos de Rubén y los hijos de Gad y la media tribu de Manasés fueron armados delante de los hijos de Israel como Moisés les había dicho:
13 Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
Unos cuarenta mil armados para la guerra fueron ante el Señor a la lucha, a las tierras bajas de Jericó.
14 Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
Ese día él Señor hizo a Josué grande ante los ojos de todo Israel; y todos los días de su vida fueron a temerle a él, como habían temido a Moisés.
15 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
Entonces el SEÑOR dijo a Josué:
16 “Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
Manda a los sacerdotes que tomen el cofre del pacto, que salgan del Jordán.
17 Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
Entonces Josué dio órdenes a los sacerdotes, diciendo: Salgan ahora del Jordán.
18 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
Y cuando los sacerdotes que tomaron el cofre del pacto del Señor salieron del Jordán y sus pies salieron a tierra firme, las aguas del Jordán regresaron a su lugar, desbordando sus bordes como antes.
19 Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
El décimo día del primer mes, el pueblo salió del Jordán y puso sus tiendas en Gilgal, en el lado este de Jericó.
20 Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
Y las doce piedras que sacaron del Jordán, Josué pusieron en Gilgal.
21 Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
Y dijo a los hijos de Israel: Cuando sus hijos pregunten a sus padres en el futuro, ¿cuál es la razón de estas piedras?
22 Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
Entonces cuéntales a sus hijos y digan: Israel cruzó este río Jordán en tierra firme.
23 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
Porque el Señor su Dios hizo que las aguas del Jordán se secaran delante de ti hasta que hubieras cruzado, como lo hizo con el Mar Rojo, secándose antes de que hubiéramos cruzado:
24 Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”
Para que todos los pueblos de la tierra vean que la mano del Señor es fuerte; y para que vayan temiendo al Señor su Dios para siempre.

< Yoswa 4 >