< Yoswa 4 >

1 Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
Lorsque tout le peuple eut achevé de franchir le Jourdain, le Seigneur parla à Josué, disant:
2 “Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
Prends douze hommes parmi le peuple, un de chaque tribu.
3 Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
Puis, donne-leur cet ordre: Ramassez au milieu du Jourdain douze pierres convenables; transportez-les avec vous, placez-les dans le campement où vous dresserez vos tentes pour cette nuit.
4 Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
Et Josué, ayant fait venir douze hommes illustres entre les fils d'Israël; un de chaque tribu,
5 ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
Leur dit: Descendez, sous mes yeux, devant l'arche du Seigneur, au milieu du Jourdain, et, après avoir pris là chacun une pierre, apportez-la sur vos épaules, selon le nombre des tribus en Israël,
6 kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
Afin qu'elles soient pour vous un signe immuable et perpétuel; et que quand à l'avenir ton fils t'interrogera, disant: Que signifient pour vous ces pierres?
7 Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
Tu l'expliques à ton fils, et lui dises: Elles nous rappellent que le Jourdain s'est arrêté devant l'arche de l'alliance du Seigneur de toute la terre, lorsqu'elle y a passé; et ces pierres seront un mémorial pour vous, pour les fils d'Israël, jusqu'à la consommation des temps.
8 Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
Les fils d'Israël exécutèrent ce que le Seigneur avait prescrit à Josué; après avoir pris du milieu du Jourdain douze pierres, comme le Seigneur le prescrivit à Josué, après que les fils d'Israël eurent achevé le passage du fleuve, ils les emportèrent avec eux dans le camp, et les y déposèrent.
9 Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
Et Josué plaça douze autres pierres dans le lit même du fleuve, au lieu où étaient les pieds des prêtres qui transportaient l'arche de l'alliance du Seigneur; elles y sont restées jusqu'à ce jour.
10 Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
Car les prêtres qui transportaient l'arche de l'alliance se tinrent immobiles dans le Jourdain, jusqu'à ce que Josué eut exécuté tout ce qu'il avait annoncé au peuple, selon l'ordre du Seigneur; or, le peuple tout entier avait franchi le fleuve;
11 Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
Et après que le peuple eut achevé le passage, l'arche de l'alliance du Seigneur passa, précédée de ceux qui portaient les pierres.
12 Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
Les fils de Ruben, les fils de Gad et la demi-tribu de Manassé, prêts au combat, avaient passé aussi, en avant des autres fils d'Israël, comme Moïse l'avait prescrit.
13 Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
Quarante mille combattants de ces tribus traversèrent le fleuve devant le Seigneur, pour combattre sous les murs de Jéricho.
14 Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
Et ce jour-là, le Seigneur exalta Josué aux yeux de toute la race d'Israël, et ils eurent crainte de lui comme de Moïse, au temps où il vivait.
15 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
Et le Seigneur parla à Josué, disant:
16 “Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
Ordonne aux prêtres qui portent l'arche du témoignage et de l'alliance, de sortir du Jourdain.
17 Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
Et Josué commanda aux prêtres, disant: Sortez du Jourdain.
18 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
Aussitôt que les prêtres, qui portaient l'arche de l'alliance du Seigneur, eurent quitté le lit du Jourdain et posé leurs pieds sur la rive, l'eau du fleuve reprit impétueusement son cours, et coula à pleins bords, comme auparavant.
19 Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
Le passage du Jourdain eut lieu le dixième jour du premier mois, et les fils d'Israël campèrent en Galgala, à l'orient de Jéricho.
20 Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
Là, Josué plaça les douze pierres qu'il avait tirées du Jourdain,
21 Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
Et il dit: Lorsque vos fils vous interrogeront, disant: Que signifient ces pierres?
22 Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
Apprenez à vos fils qu'Israël a passé le fleuve à pied sec,
23 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
Et que le Seigneur a desséché son lit devant vous, jusqu'à ce que vous l'eussiez traversé, comme il a desséché devant nous la mer Rouge, jusqu'à ce que nous l'eussions passée.
24 Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”
Afin que toutes les nations de la terre sachent que la puissance du Seigneur est irrésistible, et qu'en toutes vos œuvres vous honoriez le Seigneur votre Dieu.

< Yoswa 4 >