< Yoswa 4 >
1 Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
And it came to pass, when all the people had finished passing over the Jordan, That the Lord said unto Joshua, as followeth,
2 “Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
Take yourselves twelve men out of the people, one man each out of every tribe,
3 Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
And command ye them, saying, Take yourselves hence out of the midst of the Jordan, out of the place where the priests' feet stood firmly, twelve stones, and ye shall carry them over with you, and leave them in the lodging-place, where ye will lodge this night.
4 Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
Then did Joshua call the twelve men, whom he had appointed out of the children of Israel, one man each out of every tribe:
5 ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
And Joshua said unto them, Pass over before the ark of the Lord your God into the midst of the Jordan, and take yourselves up every man one stone upon his shoulder, according unto the number of the tribes of the children of Israel;
6 kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
In order that this may be a sign among you, when your children ask in time to come, saying, What mean ye by these stones?
7 Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
That ye shall answer them, That the waters of the Jordan were cut off before the ark of the covenant of the Lord; when it passed over the Jordan, the waters of the Jordan were cut off; and these stones shall be for a memorial unto the children of Israel for ever.
8 Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
And the children of Israel did so as Joshua had commanded; and they took up twelve stones out of the midst of the Jordan, as the Lord had spoken unto Joshua, according to the number of the tribes of the children of Israel; and they carried them over with them unto the place where they lodged, and laid them down there.
9 Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
Twelve stones also did Joshua set up in the midst of the Jordan, on the spot where the feet of the priests who bore the ark of the covenant had stood: and they have remained there unto this day.
10 Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
But the priests who bore the ark stood in the midst of the Jordan, until every thing was finished that the Lord had commanded Joshua to speak unto the people, according to all that Moses had commanded Joshua; and the people hastened and passed over.
11 Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
And it came to pass, when all the people had finished passing over, that the ark of the Lord passed over with the priests in the presence of the people.
12 Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
And the children of Reuben, and the children of Gad, and the half tribe of Menasseh, passed over armed before the children of Israel, as Moses had spoken unto them:
13 Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
About forty thousand ready armed for war, did they pass over before the Lord unto battle, to the plains of Jericho.
14 Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
On that day the Lord made Joshua great in the eyes of all Israel; and they feared him, as they had feared Moses, all the days of his life.
15 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
And the Lord said unto Joshua, as followeth,
16 “Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
Command the priests that bear the ark of the testimony, that they come up out of the Jordan.
17 Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
And Joshua commanded the priests, saying, Come ye up out of the Jordan.
18 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
And it came to pass, when the priests that bore the ark of the covenant of the Lord were come up out of the midst of the Jordan, the soles of the feet of the priests were lifted up unto the dry land, that the waters of the Jordan returned unto their place, and flowed over all its banks, as on the preceding days.
19 Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
And the people came up out of the Jordan on the tenth day of the first month, and encamped in Gilgal, on the extreme eastern border of Jericho.
20 Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
And those twelve stones, which they had taken out of the Jordan, did Joshua set up in Gilgal.
21 Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
And he said unto the children of Israel, thus, When your children shall ask in time to come their fathers, saying, What mean these stones?
22 Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
Then shall ye let your children know, saying, On dry land did Israel pass over this Jordan;
23 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
That the Lord your God dried up the waters of the Jordan from before you, until ye were passed over, as the Lord your God did to the Red Sea, which he dried up from before us, until we were gone over;
24 Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”
In order that all the nations of the earth may know the hand of the Lord, that it is mighty; in order that ye may fear the Lord your God all the days.