< Yoswa 3 >
1 Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
Ainsi, Josué se levant de nuit, leva le camp; et sortant de Sétim ils vinrent au Jourdain, lui et tous les enfants d’Israël, et ils demeurèrent là trois jours.
2 Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
Et ces trois jours écoulés, les hérauts passèrent par le milieu du camp,
3 kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
Et, commencèrent à crier: Quand vous verrez l’arche de l’alliance du Seigneur votre Dieu et les prêtres de la race lévitique qui la portent, vous aussi, levez-vous, et marchez à leur suite;
4 Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
Et qu’il y ait entre vous et l’arche l’espace de deux mille coudées, afin que de loin vous puissiez voir et connaître par quelle voie vous devez aller, parce que vous n’avez pas encore passé par cette voie; et gardez-vous d’approcher de l’arche.
5 Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
Josué dit aussi au peuple: Sanctifiez-vous; car demain le Seigneur fera parmi vous des merveilles.
6 Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
Puis il dit aux prêtres: Portez l’arche du Seigneur, et précédez le peuple. Et ceux-ci accomplissant ces ordres, la portèrent, et marchèrent devant le peuple.
7 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
Alors le Seigneur dit à Josué: Aujourd’hui je commencerai à t’exalter devant tout Israël, afin qu’ils sachent que, comme j’ai été avec Moïse, ainsi je suis avec toi aussi.
8 Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
Pour toi, commande aux prêtres qui portent l’arche de l’alliance, et dis-leur: Lorsque vous serez entrés dans une partie de l’eau du Jourdain, arrêtez-vous-là.
9 Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
Et Josué dit aux enfants d’Israël: Approchez-vous ici, et écoutez la parole du Seigneur votre Dieu.
10 Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
Et de nouveau: En cela vous saurez que le Seigneur Dieu vivant est au milieu de vous, et qu’il détruira en votre présence le Chananéen, l’Hétéen, l’Hévéen, le Phérézéen, le Gergézéen, le Jébuséen et l’Amorrhéen.
11 Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
Voilà que l’arche de l’alliance du Seigneur de toute la terre marchera devant vous à travers le Jourdain.
12 Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
Préparez douze hommes des tribus d’Israël, un de chaque tribu.
13 Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
Et lorsque les prêtres qui portent l’arche du Seigneur Dieu de toute la terre auront posé la plante de leurs pieds dans les eaux du Jourdain, les eaux d’en bas s’écouleront et se dissiperont, mais celles qui viennent d’en haut se condenseront en monceau.
14 Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
Ainsi le peuple sortit de ses tabernacles pour passer le Jourdain; et les prêtres qui portaient l’arche de l’alliance marchaient devant lui.
15 Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
Mais eux étant entrés dans le Jourdain, et leurs pieds commençant à être mouillés (car le Jourdain avait couvert ses rives au temps de la moisson),
16 madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
Les eaux qui descendaient s’arrêtèrent en un seul lieu, et, s’élevant comme une montagne, elles paraissaient de loin, depuis la ville qui est appelée Adom jusqu’au lieu nommé Sarthan; mais celles qui étaient au-dessous, descendirent dans la mer du désert (qui maintenant est appelée la mer Morte), jusqu’à ce qu’elles fussent entièrement écoulées.
17 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.
Or, le peuple marchait contre Jéricho, et les prêtres qui portaient l’arche de l’alliance du Seigneur se tenaient sur la terre sèche au milieu du Jourdain tout prêts; et tout le peuple passait à travers le lit desséché du fleuve.