< Yoswa 3 >

1 Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
Therfor Josue roos bi nyyt, and mouede tentis; and thei yeden out of Sechym, and camen to Jordan, he and alle the sones of Israel, and dwelliden there thre daies.
2 Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
And whanne tho daies weren passid, crieris yeden thorouy the myddis of tentis,
3 kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
and bigunnen to crie, Whanne ye seen the arke of boond of pees of youre Lord God, and the preestis of the generacioun of Leuy berynge it, also rise ye, and sue the biforgoeris;
4 Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
and a space of twey thousynde cubitis be bitwixe you and the arke, that ye moun se fer, and knowe bi what weie ye schulen entre, for ye `yeden not bifore bi it; and be ye war, that ye neiye not to the arke.
5 Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
And Josue seide to the puple, Be ye halewid, for to morew the Lord schal make merueilis among you.
6 Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
And Josue seide to the preestis, Take ye the arke of the boond of pees `of the Lord, and go ye bifor the puple. Whiche filliden the heestis, and tooken the arke, and yeden bifor hem.
7 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
And the Lord seide to Josue, To dai Y schal bigynne to enhaunse thee bifor al Israel, that thei wite, that as Y was with Moises, so Y am also with thee.
8 Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
Forsothe comaunde thou to preestis, that beren the arke of bond of pees, and seie thou to hem, Whanne ye han entrid in to a part of the watir of Jordan, stonde ye therynne.
9 Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
And Josue seide to the sones of Israel, Neiye ye hidur, and here ye the word of youre Lord God.
10 Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
And eft he seide, In this ye schulen wite that the Lord God lyuynge is in the myddis of you; and he schal distrye in youre siyt Cananey, Ethei, Euey, and Feresei, and Gergesei, and Jebusei, and Amorrei.
11 Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
Lo! the arke of boond of pees of the Lord of al erthe schal go bifor you thorouy Jordan.
12 Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
Make ye redi twelue men of the twelue lynagis of Israel, bi ech lynage o man.
13 Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
And whanne the preestis, that beren the arke of boond of pees of the Lord God of al erthe, han set the steppis of her feet in the watris of Jordan, the watris that ben lowere schulen renne doun, and schulen faile; forsothe the watris that comen fro aboue schulen stonde togidere in o gobet.
14 Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
Therfor the puple yede out of her tabernaclis to passe Jordan; and the preestis that baren the arke of boond of pees yeden bifor the puple.
15 Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
And whanne the preestis entriden in to Jordan, and her feet weren dippid in the part of watir; forsothe Jordan `hadde fillid the brynkis of his trow in the tyme of `ripe corn;
16 madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
the watris yeden doun, and stoden in o place, and wexiden grete at the licnesse of an hil, and apperiden fer fro the citee that was clepid Edom, `til to the place of Sarthan; sotheli the watris that weren lowere yeden doun in to the see of wildirnesse, which is now clepid the deed see, `til the watris failiden outirli.
17 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.
Forsothe the puple yede thorouy Jordan; and the preestis, that baren the arke of the boond of pees of the Lord, stoden gird on the drie erthe in the myddis of Jordan, and al the puple passide thorouy the drie trow.

< Yoswa 3 >