< Yoswa 24 >
1 Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
Josué rassembla toutes les tribus d'Israël en Silo; il convoqua leurs anciens, leurs scribes, leurs juges, et il les plaça devant Dieu.
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
Et Josué dit à tout le peuple: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Nos pères, dans les premiers temps, et Tharé, père de Nachor, ont demeuré au delà du fleuve, et ils ont servi des dieux étrangers.
3 Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
Et j'ai pris votre père Abraham, au delà du fleuve, je l'ai amené en cette terre; j'ai multiplié sa race, je lui ai donne Isaac, et à Isaac, j'ai
4 ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
Donné Jacob et Esau; j'ai donné à Esau pour héritage la montagne de Seir. Or, Jacob et ses fils sont descendus en Egypte, et ils sont devenus en ce pays une nation grande, nombreuse et puissante. Les Egyptiens les ont opprimés.
5 “‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
Mais, j'ai frappé l'Egypte avec les miracles que j'ai faits au milieu d'elle;
6 Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
Et après cela, Dieu a fait sortir vos pères de l'Egypte; vous êtes entrés dans la mer Rouge; les Egyptiens y ont poursuivi vos pères avec des chars et des chevaux.
7 Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
Et nous avons crié au Seigneur, et il a placé une nuée sombre entre nous et les Egyptiens, et il a ramené sur eux les eaux de la mer, et il les en a couverts. Vos yeux ont vu tout ce que le Seigneur a fait en Egypte, et vous êtes restés bien des jours dans le désert.
8 “‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
Enfin, le Seigneur nous a conduits en la terre des Amorrhéens qui demeuraient sur l'autre rive du Jourdain, et il nous les a livres; vous avez pris possession de leur territoire, et vous les avez exterminés devant votre face.
9 Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
En ce temps-là, Balac, fils de Sephor, roi de Moab, s'est levé, et il s'est rangé en bataille contre Israël; et il a envoyé chercher Balaam pour qu'il vous maudît.
10 Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
Mais le Seigneur, qui ne voulait point vous perdre, nous a bénis, et il nous a tirés de leurs mains, et il nous les a livrés.
11 “‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
Ensuite, vous avez traversé le Jourdain et vous êtes arrivés à Jéricho; les habitants de Jéricho, l'Amorrhéen, le Chananéen, le Phérézéen, l'Hévéen, le Jébuséen, l'Hétéen et le Gergéséen, vous ont résisté; le Seigneur les a livrés à vos mains.
12 Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
Il a lancé avant vous des essaims de guêpes, et il a chassé devant vous douze rois des Amorrhéens, non par votre glaive, non par vos flèches;
13 Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
Il vous a donné une terre que vous n'aviez point labourée, et des villes que vous n'aviez point bâties, dont vous avez fait vos demeures. Il vous a donné des vignes et des oliviers que vous n'aviez point plantés, dont vous avez mangé les fruits.
14 “Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
Maintenant donc, craignez le Seigneur; servez-le en toute droiture et justice. Faites disparaître les dieux étrangers qu'ont servis vos pères au delà de l'Euphrate ou en Egypte, et servez le Seigneur.
15 Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
Si cependant il ne vous est point agréable de servir le Seigneur, choisissez-vous dès aujourd'hui quelque dieu à servir, soit parmi ceux de vos pères au delà de l'Euphrate, soit parmi ceux des Amorrhéens dont vous habitez la terre. Pour moi et ma maison, nous servirons le Seigneur, parce qu'il est saint.
16 Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
Et le peuple répondant, dit: Dieu nous préserve d'abandonner le Seigneur pour servir d'autres dieux.
17 Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
Le Seigneur notre Dieu est le seul Dieu. C'est lui qui a fait sortir d'Egypte nous et nos pères, et qui nous a gardés tout le long de la voie que nous avons suivie, et au milieu de toutes les nations que nous avons traversées.
18 Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
Et le Seigneur a chassé devant notre face l'Amorrhéen et toutes les nations qui habitaient la terre. Nous servirons donc le Seigneur, car il est notre Dieu.
19 Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
Et Josué dit au peuple: Vous ne pourrez point servir le Seigneur: car c'est un Dieu saint; c'est un Dieu jaloux, et il ne tolèrera point vos péchés ni vos iniquité.
20 Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
Dès que vous abandonnerez le Seigneur et que vous servirez d'autres dieux, il fondra sur vous pour vous punir, et il vous accablera de maux au lieu du bien qu'il vous a fait.
21 Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
Et le peuple dit à Josué: Non, non; nous servirons le Seigneur.
22 Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
Et Josué dit au peuple: Vous êtes vous-mêmes témoins entre vous que vous avez choisi le service du Seigneur.
23 Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
Et maintenant, faites disparaître les dieux étrangers que vous avez parmi vous, et dirigez vos cœurs vers le Seigneur Dieu d'Israël.
24 Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
Et le peuple dit à Josué: Nous servirons le Seigneur, et nous serons dociles à sa voix.
25 Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
Ce jour-là, Josué fit alliance avec le peuple, et il lui donna la loi et le jugement en Silo, devant le tabernacle du Dieu d'Israël.
26 Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
Et il écrivit toutes ces paroles dans le livre des lois de Dieu; il prit une grande pierre, et il la dressa, sous le térébinthe, devant le Seigneur.
27 Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
Et Josué dit au peuple. Voyez cette pierre; elle portera parmi vous témoignage; elle a entendu tout ce qui vient d'être dit ici par le Seigneur; car c'est lui qui vous a parlé aujourd'hui, et cette pierre portera parmi vous témoignage jusqu'aux derniers des jours, lorsque vous viendrez à mentir au Seigneur mon Dieu.
28 Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
Josué alors congédia le peuple, et chacun se rendit à sa demeure.
29 Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
Après ces choses, Josué, fils de Nau, serviteur de Dieu, mourut âgé de cent dix ans.
30 ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
On l'ensevelit sur les limites de son héritage, en Thamnasarach, dans les montagnes d'Ephraïm, au nord des montagnes de Galaad.
31 Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
Israël servit donc le Seigneur durant tous les jours de Josué, et durant tous les jours des anciens dont la vie s'était prolongée avec la sienne, et qui avaient vu toutes les œuvres du Seigneur en faveur d'Israël.
32 Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
Les fils d'Israël avaient rapporté de l'Egypte les ossements de Joseph, et ils les inhumèrent à Sichem dans le champ que Jacob avait acheté au prix de cent agneaux, des Amorrhéens qui habitaient Sichem, et qu'il avait donné à Joseph.
33 Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.
Ensuite, Eléazar, fils d'Aaron le grand prêtre, mourut, et il fut enseveli en Gabaar, qu'il avait donnée à Phinées, dans la montagne d'Ephraïm.