< Yoswa 24 >
1 Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
And Josue gathered together all the tribes of Israel in Sichem, and called for the ancients, and the princes, and the judges, and the masters: and they stood in the sight of the Lord:
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
And he spoke thus to the people: Thus saith the Lord the God of Israel: Your fathers dwelt of old on the other side of the river, Thare the father of Abraham, and Nachor: and they served strange gods.
3 Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
And I took your father Abraham from the borders of Mesopotamia: and brought him into the land of Chanaan: and I multiplied his seed,
4 ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
And gave him Isaac: and to him again I gave Jacob and Esau. And I gave to Esau mount Seir for his possession: but Jacob and his children went down into Egypt.
5 “‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
And I sent Moses and Aaron, and I struck Egypt with many signs and wonders.
6 Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
And I brought you and your fathers out of Egypt, and you came to the sea: and the Egyptians pursued your fathers with chariots and horsemen, as far as the Red Sea.
7 Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
And the children of Israel cried to the Lord: and he put darkness between you and the Egyptians, and brought the sea upon them, and covered them. Your eyes saw all that I did in Egypt, and you dwelt in the wilderness a long time:
8 “‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
And I brought you into the land of the Amorrhite, who dwelt beyond the Jordan. And when they fought against you, I delivered them into your hands, and you possessed their land, and slew them.
9 Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
And Balac son of Sephor king of Moab arose and fought against Israel. And he sent and called for Balaam son of Beor, to curse you:
10 Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
And I would not hear him, but on the contrary I blessed you by him, and I delivered you out of his hand.
11 “‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
And you passed over the Jordan, and you came to Jericho. And the men of that city fought against you, the Amorrhite, and the Pherezite, and the Chanaanite, and the Hethite, and the Gergesite, and the Hevite, and the Jebusite: and I delivered them into your hands.
12 Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
And I sent before you hornets: and I drove them out from their places, the two kings of the Amorrhites, not with thy sword nor with thy bow.
13 Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
And I gave you a land, in which you had not laboured, and cities to dwell in which you built not, vineyards and oliveyards, which you planted not.
14 “Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
Now therefore fear the Lord, and serve him with a perfect and most sincere heart: and put away the gods which your fathers served in Mesopotamia and in Egypt, and serve the Lord.
15 Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
But if it seem evil to you to serve the Lord, you have your choice: choose this day that which pleaseth you, whom you would rather serve, whether the gods which your fathers served in Mesopotamia, or the gods of the Amorrhites, in whose land you dwell: but as for me and my house we will serve the Lord.
16 Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
And the people answered, and said: God forbid we should leave the Lord, and serve strange gods.
17 Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
The Lord our God he brought us and our fathers out of the land of Egypt, out of the house of bondage: and did very great signs in our sight, and preserved us in all the way by which we journeyed, and among all the people through whom we passed.
18 Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
And he hath cast out all the nations, the Amorrhite the inhabitant of the land into which we are come. Therefore we will serve the Lord, for he is our God.
19 Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
And Josue said to the people: You will not be able to serve the Lord: for he is a holy God, and mighty and jealous, and will not forgive your wickedness and sins.
20 Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
If you leave the Lord, and serve strange gods, he will turn, and will afflict you, and will destroy you after all the good he hath done you.
21 Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
And the people said to Josue: No, it shall not be so as thou sayest, but we will serve the Lord.
22 Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
And Josue said to the people: You are witnesses, that you yourselves have chosen you the Lord to serve him. And they answered: We are witnesses.
23 Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
Now therefore, said he, put away strange gods from among you, and incline your hearts to the Lord the God of Israel.
24 Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
And the people said to Josue: We will serve the Lord our God, and we will be obedient to his commandments.
25 Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
Josue therefore on that day made a covenant, and set before the people commandments and judgments in Sichem.
26 Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
And he wrote all these things in the volume of the law of the Lord: and he took a great stone, and set it under the oak that was in the sanctuary of the Lord.
27 Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
And he said to all the people: Behold this stone shall be a testimony unto you, that it hath heard all the words of the Lord, which he hath spoken to you: lest perhaps hereafter you will deny it, and lie to the Lord your God.
28 Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
And he sent the people away every one to their own possession.
29 Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
And after these things Josue the son of Null the servant of the Lord died, being a hundred and ten years old:
30 ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
And they buried him in the border of his possession in Thamnathsare, which is situate in mount Ephraim, on the north side of mount Gaas.
31 Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
And Israel served the Lord all the days of Josue, and of the ancients that lived a long time after Josue, and that had known all the works of the Lord which he had done in Israel.
32 Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
And the bones of Joseph which the children of Israel had taken out of Egypt, they buried in Sichem, in that part of the field which Jacob had bought of the sons of Hemor the father of Sichem, for a hundred young ewes, and it was in the possession of the sons of Joseph.
33 Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.
Eleazar also the son of Aaron died: and they buried him in Gabaath that belongeth to Phinees his son, which was given him in mount Ephraim.