< Yoswa 23 >

1 Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
Kwasekusithi emva kwensuku ezinengi emva kokuthi iNkosi isimphumuzile uIsrayeli ezitheni zonke zabo inhlangothi zonke, loJoshuwa wayesemdala elensuku ezinengi,
2 Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
uJoshuwa wabiza uIsrayeli wonke, abadala babo, lenhloko zabo, labahluleli babo, lenduna zabo, wathi kubo: Mina sengimdala ngilensuku ezinengi.
3 Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
Lina selibonile konke iNkosi uNkulunkulu wenu ekwenzileyo kulezizizwe zonke ngenxa yenu, ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu yiyo elilweleyo.
4 Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
Bonani, ngilabele ngenkatho lezizizwe eziseleyo zibe yilifa lezizwe zenu, kusukela eJordani, lazo zonke izizwe engiziqumileyo, ngitsho kuze kube selwandle olukhulu lapho okutshona khona ilanga.
5 Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
INkosi uNkulunkulu wenu izazixotsha-ke phambi kwenu, izixotshe elifeni phambi kwenu, njalo lizakudla ilifa lelizwe, njengalokho iNkosi uNkulunkulu wenu ikhulumile kini.
6 “Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
Ngakho qinani kakhulu ukugcina lokwenza konke okubhaliweyo egwalweni lomlayo kaMozisi, ukuze lingaphambuki kuwo liye ngakwesokunene loba ngakwesokhohlo,
7 Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
ukuze lingangeni kulezi izizwe, lezi ezisele lani, lingaphathi ibizo labonkulunkulu bazo, lingafungisi ngabo, lingabakhonzi, lingakhothami kubo,
8 Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
kodwa linamathele eNkosini uNkulunkulu wenu njengoba lenzile kuze kube lamuhla.
9 “Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
Ngoba iNkosi ixotshile elifeni phambi kwenu izizwe ezinkulu lezilamandla; lina-ke kakulamuntu ome phambi kwenu kuze kube lamuhla.
10 Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
Umuntu oyedwa kini uzaxotsha inkulungwane, ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu yiyo elilwelayo, njengalokho ikhulumile kini.
11 Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
Ngakho ziqaphelisiseni ukuthanda iNkosi uNkulunkulu wenu.
12 “Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
Ngoba uba libuyela lokubuyela, linamathele kunsali yalezizizwe, lezi ezisele lani, lithathane lazo, lingene kuzo, lazo kini,
13 pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
yazini lokwazi ukuthi iNkosi uNkulunkulu wenu kayiyikuqhubeka ngokuzixotsha elifeni lezizizwe phambi kwenu; kodwa zizakuba yisifu lomjibila kini, zibe luswazi enhlangothini zenu, lameva emehlweni enu, lize libhubhe liphele kulelilizwe elihle, iNkosi uNkulunkulu wenu elinike lona.
14 “Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
Khangelani-ke, ngihamba lamuhla ngendlela yomhlaba wonke. Njalo liyazi enhliziyweni yenu yonke lemphefumulweni wenu wonke ukuthi akukho lelizwi elilodwa elehlulekayo kuwo wonke amazwi amahle iNkosi uNkulunkulu wenu ewakhulumileyo phezu kwenu; wonke ezile kini, akukho lelizwi elilodwa elehlulekayo kuwo.
15 Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
Kuzakuthi-ke, njengalokhu zonke izinto ezinhle iNkosi uNkulunkulu wenu eyazikhuluma kini sezilehlele, ngokunjalo iNkosi izalehlisela zonke izinto ezimbi, ize ilibhubhise liphele kulelilizwe elihle iNkosi uNkulunkulu wenu elinike lona.
16 Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”
Uba liseqa isivumelwano seNkosi uNkulunkulu wenu eyalilaya sona, lisuke liyekhonza abanye onkulunkulu, likhothame kibo, khona ulaka lweNkosi luzalivuthela, libhubhe masinyane liphele kulelilizwe elihle elinike lona.

< Yoswa 23 >