< Yoswa 23 >
1 Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
Proteklo je mnogo dana kako je Jahve dao Izraelu da otpočine od svih neprijatelja unaokolo. I Jošua bijaše ostario, zašao u godine.
2 Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
Dozva zato Jošua sve Izraelce, starješine, glavare, suce i upravitelje njihove i reče im: “Ostario sam i odmakao u godinama.
3 Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
Vi ste bili svjedoci svega što je Jahve, Bog vaš, pred vašim očima učinio svim narodima radi vas: Jahve, Bog vaš, borio se za vas.
4 Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
Vidite, razdijelio sam ždrijebom u baštinu vašim plemenima sve narode koji su ostali i sve one narode koje sam istrijebio od Jordana do Velikog mora na zapadu.
5 Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
Jahve, Bog vaš, sam će ih goniti ispred vas i otjerat će ih ispred vas i zaposjest ćete njihovu zemlju, kao što vam je obećao Jahve, Bog vaš.
6 “Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
Budite, dakle, postojani i sve čvršći u tome da čuvate i vršite sve što je napisano u Knjizi zakona Mojsijeva i da ne odstupite od toga ni desno ni lijevo.
7 Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
Ne miješajte se s tim narodima koji ostadoše među vama; i ne spominjite imena njihovih bogova niti se kunite njima; nemojte im služiti i ne klanjajte se njima.
8 Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
Nego se držite Jahve, Boga svoga, kako ste činili do danas.
9 “Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
Jahve je protjerao ispred vas velike i moćne narode i nitko se nije do danas mogao održati pred vama.
10 Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
Jedan je od vas tjerao pred sobom tisuću, jer se Jahve, Bog vaš, borio za vas, kao što vam je obećao.
11 Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
Brižno pazite da ljubite Jahvu, Boga svojega, jer se radi o vašem životu.
12 “Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
Jer ako se odmetnete i prionete uz ostatak onih naroda koji preostaše među vama i s njima se povežete tazbinom i pomiješate se s njima i oni s vama,
13 pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
znajte dobro da će Jahve, Bog vaš, prestati goniti te narode ispred vas; oni će vam postati zamka i mreža, bit će bič bokovima vašim i trnje očima vašim, sve dok se ne iselite iz ove dobre zemlje koju vam dade Jahve, Bog vaš.
14 “Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
Evo, ja krećem danas na put kojim je svima poći. Spoznajte i priznajte svim srcem svojim i svom dušom svojom: ni jedno od svih obećanja koja vam je dao Jahve, Bog vaš, nije ostalo neispunjeno.
15 Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
I kao što vam se ispunilo svako obećanje što vam ga je dao Jahve, Bog vaš, tako će Jahve ispuniti i svaku prijetnju dok vas ne izbriše s lica ove dobre zemlje koju vam je dao Jahve, Bog vaš.
16 Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”
Ako prekršite Savez koji je Jahve, Bog vaš, sklopio s vama; ako budete služili drugim bogovima i klanjali se njima, buknut će gnjev Jahvin na vas i nestat će vas ubrzo iz dobre zemlje koju vam je Jahve dao.”