< Yoswa 22 >
1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Potem je Józue poklical Rubenovce, Gádovce in polovico Manásejevega rodu
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
ter jim rekel: »Držali ste se vsega, kar vam je Gospodov služabnik Mojzes zapovedal in moj glas ste ubogali v vsem, kar sem vam zapovedal.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Te mnoge dni do tega dne niste zapustili svojih bratov, temveč ste skrbeli za zapoved Gospoda, svojega Boga.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
Sedaj je Gospod, vaš Bog, dal počitek vašim bratom, kakor jim je obljubil, zato se sedaj vrnite in se odpravite v svoje šotore in v deželo svoje posesti, ki vam jo je dal Gospodov služabnik Mojzes na drugi strani Jordana.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Toda marljivo pazite, da izpolnite zapoved in postavo, ki vam jo je zapovedal Gospodov služabnik Mojzes, da ljubite Gospoda, svojega Boga in da hodite po vseh njegovih poteh in se držite njegovih zapovedi in da se mu trdno pridružite in mu služite z vsem svojim srcem in z vso svojo dušo.«
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
Tako jih je Józue blagoslovil in jih poslal proč; in odšli so k svojim šotorom.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Torej eni polovici Manásejevega rodu je Mojzes dal posest v Bašánu, toda drugi njegovi polovici je Józue dal [posest] med njihovimi brati na tej strani Jordana proti zahodu. Ko je Józue tudi njih poslal proč, v njihove šotore, tedaj jih je blagoslovil
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
in jim govoril, rekoč: »V svoje šotore se vrnite z mnogimi bogastvi in z zelo veliko živine, s srebrom in z zlatom, z bronom in z železom in z zelo mnogimi oblačili. Plen svojih sovražnikov razdelite s svojimi brati.«
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
Rubenovi otroci in Gadovi otroci in polovica Manásejevega rodu se je vrnila in odpotovala od Izraelovih otrok iz Šila, ki je v kánaanski deželi, da gredo v deželo Gileád, k zemlji njihove posesti, ki so jo vzeli v last, glede na Gospodovo besedo, po Mojzesovi roki.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
Ko so prišli k mejam Jordana, ki so v kánaanski deželi, so Rubenovi otroci in Gadovi otroci in polovica Manásejevega rodu tam zgradili oltar pri Jordanu, na pogled velik oltar.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
Izraelovi otroci so slišali reči: »Glejte, Rubenovi otroci, Gadovi otroci in polovica Manásejevega rodu so zgradili oltar nasproti kánaanski deželi, na mejah Jordana, ob prehodu Izraelovih otrok.«
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
Ko so Izraelovi otroci slišali o tem, se je celotna skupnost Izraelovih otrok skupaj zbrala pri Šilu, da gredo gor, da se vojskujejo proti njim.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Izraelovi otroci so k Rubenovim otrokom, h Gadovim otrokom in k polovici Manásejevega rodu v deželo Gileád poslali Pinhása, sina duhovnika Eleazarja
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
in z njim deset princev, iz vsake vodilne hiše princa, po vseh Izraelovih rodovih in vsak je bil poglavar svoje očetovske hiše med tisočerimi Izraelovimi.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
Prišli so k Rubenovim otrokom, h Gadovim otrokom in k polovici Manásejevega rodu, v deželo Gileád in z njimi govorili, rekoč:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
»Tako govori celotna Gospodova skupnost: ›Kakšen prekršek je to, kar ste zagrešili zoper Izraelovega Boga, da se ta dan odvračate od sledenja Gospodu, v tem, da ste si zgradili oltar, da bi se ta dan lahko uprli zoper Gospoda?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Mar je krivičnost Peórja premajhna za nas, od katere do tega dne nismo očiščeni, čeprav je bila nadloga v Gospodovi skupnosti,
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
temveč da ste se ta dan morali odvrniti od sledenja Gospodu? Zgodilo se bo, glede na to, da ste se ta dan uprli zoper Gospoda, da bo jutri ogorčen nad celotno Izraelovo skupnostjo.
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Vendar če je dežela vaše posesti nečista, potem prečkajte v deželo Gospodove posesti, v kateri prebiva Gospodovo šotorsko svetišče in vzemite posest med nami, toda ne uprite se zoper Gospoda niti se ne uprite zoper nas v tem, da si gradite oltar poleg oltarja Gospoda, našega Boga.
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Mar ni Zerahov sin Ahán zagrešil prekršek v prekleti stvari in je bes padel na vso Izraelovo skupnost? In ta mož v svoji krivičnosti ni umrl sam.‹«
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
Potem so Rubenovi otroci, Gadovi otroci in polovica Manásejevega rodu odgovorili in rekli poglavarjem tisočerih Izraelovih:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
» Gospod, Bog bogov, Gospod, Bog bogov, on ve in Izrael bo vedel. Če je to v uporu ali če je v prestopku zoper Gospoda (ta dan nas ne reši),
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
da smo si zgradili oltar, da se obrnemo od sledenja Gospodu, ali če na njem darujemo žgalno daritev ali jedilno daritev ali če na njem žrtvujejo mirovne daritve, naj sam Gospod to zahteva
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
in če nismo tega raje storili zaradi strahu pred to stvarjo, rekoč: ›V času, ki pride, bodo vaši otroci lahko govorili našim otrokom, rekoč: ›Kaj imate z Gospodom, Izraelovim Bogom?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
Kajti Gospod je naredil Jordan za mejo med nami in vami, vi Rubenovi otroci in Gadovi otroci, vi nimate deleža v Gospodu.‹‹ Tako bodo vaši otroci naredili našim otrokom, da se prenehajo bati Gospoda.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Zato smo rekli: ›Pripravimo se, da si zgradimo oltar, ne za žgalno daritev niti za klavno daritev,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
temveč, da bo ta lahko priča med nami in vami in našimi rodovi za nami, da bomo lahko pred njim opravljali Gospodovo službo s svojimi žgalnimi daritvami, svojimi klavnimi daritvami in s svojimi mirovnimi daritvami, ‹ da v času, ki pride, vaši otroci ne bodo mogli reči našim otrokom: ›Vi nimate deleža v Gospodu.‹
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Zato smo rekli, da bo tako, ko bodo tako rekli nam ali našim rodovom, v času, ki pride, da bomo lahko ponovno rekli: ›Glejte vzorec Gospodovega oltarja, ki so ga naredili naši očetje, niti za žgalne daritve, niti za klavne daritve, temveč je ta priča med vami in nami.‹
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Bog ne daj, da bi se uprli zoper Gospoda in se ta dan obrnili od sledenja Gospodu, da zgradimo oltar za žgalne daritve, za jedilne daritve ali za klavne daritve, poleg oltarja Gospoda, našega Boga, ki je pred njegovim šotorskim svetiščem.«
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
Ko so duhovnik Pinhás in princi skupnosti in poglavarji tisočerih Izraelovih, ki so bili z njim, slišali besede, ki so jih Rubenovi otroci, Gadovi otroci in Manásejevi otroci govorili, jim je to ugajalo.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
In Pinhás, sin duhovnika Eleazarja, je rekel Rubenovim otrokom, Gadovim otrokom in Manásejevim otrokom: »Ta dan smo zaznali, da je med nami Gospod, zato ker tega prekrška niste zagrešili zoper Gospoda. Sedaj ste Izraelove otroke osvobodili iz Gospodove roke.«
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
Pinhás, sin duhovnika Eleazarja in princi so se vrnili od Rubenovih otrok in od Gadovih otrok iz dežele Gileád v kánaansko deželo, k Izraelovim otrokom in jim ponovno prinesli besedo.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
Stvar je ugajala Izraelovim otrokom in Izraelovi otroci so blagoslovili Boga in niso nameravali iti gor zoper njih v bitko, da bi uničili deželo, v kateri so prebivali otroci Rubena in Gada.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
Rubenovi otroci in Gadovi otroci pa so oltar imenovali Ed, kajti ta bo priča med nami, da Gospod je Bog.