< Yoswa 22 >

1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Alors Josué manda les Rubénites, les Gadites et la demi-tribu de Manassé,
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
et leur dit: "Vous avez observé tout ce que vous avait prescrit Moïse, serviteur de l’Eternel, et vous m’avez aussi obéi en tout ce que je vous ai enjoint.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Vous n’avez pas abandonné vos frères durant cette longue période, jusqu’à ce jour, et vous êtes restés fidèles à la volonté de l’Eternel, votre Dieu.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
Et maintenant l’Eternel, votre Dieu, a accordé du repos à vos frères, comme il le leur avait promis; partez donc, allez dans vos tentes, au pays de votre possession que vous a donné Moïse, serviteur de l’Eternel, au delà du Jourdain.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Toutefois, appliquez-vous bien à suivre la loi et la doctrine que vous imposa Moïse, serviteur de l’Eternel, c’est-à-dire à aimer l’Eternel, votre Dieu, à marcher dans toutes ses voies, à garder ses commandements et à lui demeurer attachés; à le servir enfin de tout votre coeur et de toute votre âme."
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
Et Josué, les ayant bénis, les congédia, et ils prirent le chemin de leurs tentes.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Or, la moitié de la tribu de Manassé avait reçu sa part de Moïse dans le Basan, et l’autre moitié avait été installée par Josué parmi ses frères, sur le bord occidental du Jourdain; de plus, quand Josué renvoya les premiers à leurs tentes en les bénissant,
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
il leur dit: "Retournez à vos demeures avec de grands biens, avec un bétail considérable, chargés d’argent et d’or, de cuivre et de fer, de vêtements en grande quantité; ces dépouilles de vos ennemis, partagez-les avec vos frères!"
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
Alors les enfants de Ruben, ceux de Gad et la demi-tribu de Manassé quittèrent les autres enfants d’Israël et s’en allèrent de Silo, qui est dans le pays de Canaan, pour gagner la contrée de Galaad, le pays de leur possession, dont Moïse leur avait accordé la propriété par ordre de l’Eternel.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
Arrivés aux districts du Jourdain faisant partie du pays de Canaan, les enfants de Ruben et de Gad et la demi-tribu de Manassé érigèrent là un autel près du Jourdain, un grand autel bien apparent.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
La nouvelle en vint aux enfants d’Israël: "Voici que les enfants de Ruben, ceux de Gad et la demi-tribu de Manassé ont bâti un autel devant le pays de Canaan, dans les districts du Jourdain, en face des enfants d’Israël."
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
Ce qu’ayant appris, toute la communauté des enfants d’Israël se réunit à Silo, pour marcher contre eux en guerre.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Les enfants d’Israël députèrent auprès de ceux de Ruben et de Gad, et de la demi-tribu de Manassé, Phinéas, fils du pontife Eléazar,
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
et, avec lui, dix chefs, un chef de famille pour chacune des tribus d’Israël: chacun était le principal membre de sa famille parmi les divisions d’Israël.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
Ceux-ci allèrent trouver les enfants de Ruben et de Gad et la demi-tribu de Manassé, au pays de Galaad, et leur parlèrent en ces termes:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
"Ainsi a parlé toute la communauté de l’Eternel: Qu’est-ce que cette trahison que vous avez commise à l’égard du Dieu d’Isràël, cette défection envers l’Eternel, en vous bâtissant un autel et vous révoltant ainsi contre le Seigneur?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
N’Est-ce pas assez, pour nous, du crime de Peor, dont nous ne nous sommes pas lavés jusqu’à ce jour, et qui suscita une mortalité dans l’assemblée du Seigneur?
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
Et vous, aujourd’hui, vous vous sépareriez de l’Eternel! Qu’adviendra-t-il? Vous vous révoltez aujourd’hui contre Dieu, demain son courroux éclatera contre la communauté entière d’Israël.
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Que si le pays de votre possession vous semble impur, repassez dans le pays qui est le territoire de l’Eternel, où s’élève la résidence de l’Eternel, et établissez-vous au milieu de nous; mais ne vous révoltez pas contre l’Eternel, ne vous insurgez pas contre nous, en vous construisant un autel rival de celui de l’Eternel, notre Dieu!
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Lorsque Akhan, fils de Zérah, commit une infidélité à propos de l’anathème, est-ce que toute la communauté d’Israël ne fut pas l’objet de la colère divine? Lui pourtant était seul, mais il n’a pas seul péri par son crime."
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
Les enfants de Ruben et de Gad, et la demi-tribu de Manassé, prenant la parole, répondirent aux chefs des divisions d’Israël:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
"Le Dieu des dieux est l’Eternel! Le Dieu des dieux est l’Eternel! Il le sait, lui, et Israël aussi le saura! Si nous avons agi par rébellion et forfaiture envers l’Eternel, qu’il nous prive aujourd’hui de son assistance!
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
Si nous avons bâti un autel pour nous séparer du Seigneur, soit en y offrant holocauste ou oblation, soit en y sacrifiant des victimes rémunératoires, que le Seigneur nous en demande compte!
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
Non certes; si nous avons agi ainsi, c’est que nous avons craint qu’un jour vos fils ne disent aux nôtres: "Qu’avez-vous de commun avec l’Eternel, Dieu d’Israël?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
Entre nous et vous, enfants de Ruben et de Gad, l’Eternel a posé une limite, le Jourdain: vous n’avez point de part à l’Eternel!" Et ainsi vos descendants empêcheraient les nôtres de rendre hommage à l’Eternel.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Donc, nous nous sommes dit: Agissons pour nous-mêmes en élevant un autel, non pour y offrir ni holocauste ni autre sacrifice;
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
mais ce sera un garant entre nous et vous, comme entre nos descendants respectifs, de notre droit à servir l’Eternel en sa présence, par nos holocaustes, nos rémunératoires et autres sacrifices, et que vos enfants ne puissent pas, demain, dire aux nôtres: Vous n’avez point de part à l’Eternel.
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Nous nous sommes dit: Si un jour on devait nous parler ainsi, à nous ou à nos descendants, nous répondrions: "Voyez cette image de l’autel du Seigneur, que nos pères ont établie, non en vue d’holocaustes ni de sacrifices quelconques, mais comme garantie entre nous et vous."
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Loin de nous pareille chose, de nous révolter contre l’Eternel et de l’abandonner aujourd’hui, en érigeant un autel pour y offrir holocauste, oblation ou sacrifice, à l’exclusion de l’autel de l’Eternel, notre Dieu, placé devant son tabernacle!"
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
Quand Phinéas le pontife, ainsi que les chefs de la communauté et des divisions d’Israël qui l’accompagnaient, eurent entendu les paroles prononcées par les enfants de Ruben, de Gad et de Manassé, ils les approuvèrent.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
Et Phinéas, fils du pontife Eléazar, dit aux enfants de Ruben, à ceux de Gad et de Manassé: "Maintenant nous savons que l’Eternel réside au milieu de nous, puisque vous 'n’avez pas commis cette prévarication envers lui; dès lors, vous avez préservé les enfants d’Israël de la vindicte du Seigneur."
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
Phinéas, fils du pontife Eléazar, et les chefs, quittant les enfants de Ruben et ceux de Gad, revinrent du pays de Galaad dans celui de Canaan, auprès des enfants d’Israël, et leur rendirent compte.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
La chose plut aux enfants d’Israël, qui rendirent grâce à Dieu, et ne parlèrent plus de faire contre eux une expédition, ni de ravager le pays habité par les enfants de Ruben et ceux de Gad.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
Les enfants de Ruben et ceux de Gad dénommèrent l’autel en disant: "Ce sera un témoin entre nous, attestant que l’Eternel seul est Dieu!"

< Yoswa 22 >