< Yoswa 22 >

1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
At the same time Josue called the Rubenites, and the Gadites, and the half tribe of Manasses,
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
And said to them: You have done all that Moses the servant of the Lord commanded you: you have also obeyed me in all things,
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Neither have you left your brethren this long time, until this present day, keeping the commandment of the Lord your God.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
Therefore as the Lord your God hath given your brethren rest and peace, as he promised: return, and go to your dwellings, and to the land of your possession, which Moses the servant of the Lord gave you beyond the Jordan:
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Yet so that you observe attentively, and in work fulfill the commandment and the law which Moses the servant of the Lord commanded you: that you love the Lord your God, and walk in all his ways, and keep all his commandments, and cleave to him, and serve him with all your heart, and with all your soul.
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
And Josue blessed them, and sent them away, and they returned to their dwellings.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Now to half the tribe of Manasses, Moses had given a possession in Basan: and therefore to the half that remained, Josue gave a lot among the rest of their brethren beyond the Jordan to the west. And when he sent them away to their dwellings and had blessed them,
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
He said to them: With much substance and riches, you return to your settlements, with silver and gold, brass and iron, and variety of raiment: divide the prey of your enemies with your brethren.
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
So the children of Ruben, and the children of Gad, and the half tribe of Manasses returned, and parted from the children of Israel in Silo, which is in Chanaan, to go into Galaad the land of their possession, which they had obtained according to the commandment of the Lord by the hand of Moses.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
And when they were come to the banks of the Jordan, in the land of Chanaan, they built an altar immensely great near the Jordan.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
And when the children of Israel had heard of it, and certain messengers had brought them an account that the children of Ruben, and of Cad, and the half tribe of Manasses had built an altar in the land of Chanaan, upon the banks of the Jordan, over against the children of Israel:
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
They all assembled in Silo, to go up and fight against them.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
And in the mean time they sent to them into the land of Galaad, Phinees the son of Eleazar the priest,
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
And ten princes with him, one of every tribe.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
Who came to the children of Ruben, and of Gad, and the half tribe of Manasses, into the land of Galaad, and said to them:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
Thus saith all the people of the Lord: What meaneth this transgression? Why have you forsaken the Lord the God of Israel, building a sacrilegious altar, and revolting from the worship of him?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Is it a small thing to you that you sinned with Beelphegor, and the stain of that crime remaineth in us to this day? and many of the people perished.
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
And you have forsaken the Lord today, and tomorrow his wrath will rage against all Israel.
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
But if you think the land of your possession to be unclean, pass over to the land wherein is the tabernacle of the Lord, and dwell among us: only depart not from the Lord, and from our society, by building an altar beside the altar of the Lord our God.
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Did not Achan the son of Zare transgress the commandment of the Lord, and his wrath lay upon all the people of Israel? And he was but one man, and would to God he alone had perished in his wickedness.
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
And the children of Ruben, and of Gad, and of the half tribe of Manasses answered the princes of the embassage of Israel:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
The Lord the most mighty God, the Lord the most mighty God, he knoweth, and Israel also shall understand: If with the design of transgression we have set up this altar, let him not save us, but punish us immediately:
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
And if we did it with that mind, that we might lay upon it holocausts, and sacrifice, and victims of peace offerings, let him require and judge:
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
And not rather with this thought and design, that we should say: Tomorrow your children will say to our children: What have you to do with the Lord the God of Israel?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
The Lord hath put the river Jordan for a border between us and you, O ye children of Ruben, and ye children of Gad: and therefore you have no part in the Lord. And by this occasion you children shall turn away our children from the fear of the Lord. We therefore thought, it best,
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
And said: Let us build us an altar, not for holocausts, nor to offer victims,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
But for a testimony between us and you, and our posterity and yours, that we may serve the Lord, and that we may have a right to offer both holocausts, and victims and sacrifices of peace offerings: and that your children tomorrow may not say to our children: You have no part in the Lord.
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
And if they will say so, they shall answer them: Behold the altar of the Lord, which our fathers made, not for holocausts, nor for sacrifice, but for a testimony between us and you.
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
God keep us from any such wickedness that we should revolt from the Lord, and leave off following his steps, by building an altar to offer holocausts, and sacrifices, and victims, beside the altar of the Lord our God, which is erected before his tabernacle.
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
And when Phinees the priest, and the princes of the embassage, who were with him, had heard this, they were satisfied: and they admitted most willingly the words of the children of Ruben, and Gad, and of the half tribe of Manasses.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
And Phinees the priest the son of Eleazar said to them: Now we know that the Lord is with us, because you are not guilty of this revolt, and you have delivered the children of Israel from the hand of the Lord.
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
And he returned with the princes from the children of Ruben and Gad, out of the land of Galaad, into the land of Chanaan, to the children of Israel, and brought them word again.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
And the saying pleased all that heard it. And the children of Israel praised God, and they no longer said that they would go up against them, and fight, and destroy the land of their possession.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
And the children of Ruben, and the children of Cad called the altar which they had built, Our testimony, that the Lord is God.

< Yoswa 22 >