< Yoswa 22 >
1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Derpå lod Josua Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme kalde til sig
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
og sagde til dem: "I har holdt alt, hvad HERRENs Tjener Moses bød eder, og adlydt mig i alt, hvad jeg har påbudt eder.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
I har ikke svigtet eders Brødre i denne lange Tid; indtil denne Dag har I holdt HERREN eders Guds Bud.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
Men nu har HERREN eders Gud skaffet eders Brødre Ro, som han lovede dem; vend derfor nu tilbage til eders Telte i det Land, hvor eders Ejendom ligger, som HERRENs Tjener Moses gav eder hinsides Jordan.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Kun må I omhyggeligt agte på at holde det Bud og den Lov, HERRENs Tjener Moses pålagde eder, at elske HERREN eders Gud, vandre på alle hans Veje, holde hans Bud, holde fast ved ham og tjene ham af hele eders Hjerte og hele eders Sjæl!"
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
Og Josua velsignede dem og lod dem drage bort, og de begav sig til deres Telte.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
Den ene Halvdel af Manasses Stamme havde Moses givet Land i Basan, den anden Halvdel derimod havde Josua givet Land sammen med deres Brødre i Landet vesten for Jordan. Og da Josua lod dem drage hver til sit efter at have velsignet dem,
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
vendte de tilbage til deres Telte med store Rigdomme, med Kvæg i Mængde, med Sølv og Guld, Kobber og Jern og Klæder i stor Mængde; og det Bytte, de havde taget fra deres Fjender, delte de med deres Brødre.
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
Så forlod Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme Israeliterne i Silo i Kana'ans Land og vendte tilbage til Gilead, det Land, de havde fået i Eje, hvor de havde nedsat sig i Følge HERRENs Bud ved Moses;'
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
og da Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme kom til Gelilot ved Jordan i Kana'ans Land, byggede de et Alter der ved Jordan, et stort Alter. der sås viden om.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
Men det kom Israeliterne for Øre, at Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme havde bygget et Alter på Grænsen af Kana'ans Land, ved Gelilot ved Jordan, på Israeliternes Side.
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
Og da Israeliterne hørte det, samledes hele Israeliternes Menighed i Silo for at drage i Kamp imod dem.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Da sendte Israeliterne Pinehas, Præsten Eleazars Søn, til Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme i Gilead
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
tillige med ti Øverster, een Øverste for hver af alle Israels Stammer; hver af dem var Overhoved for sin Stamme iblandt Israels Tusinder;
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
og da de kom til Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme i Gilead, talte de således til dem:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
"Således siger hele HERRENs Menighed: Hvad er det for en Troløshed, I har begået mod Israels Gud, at I i Dag har vendt eder fra HERREN ved at bygge eder et Alter og vise Genstridighed mod HERREN?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Har vi ikke nok i Brøden med Peor, som vi endnu den Dag i Dag ikke har fået os renset for, og for hvis Skyld der kom Plage over Israels Menighed?
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
Og dog vender I eder i Dag fra HERREN! Når I i Dag er genstridige mod HERREN, vil hans Vrede i Morgen bryde løs over hele Israels Menighed.
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Hvis det Land, I har fået i Eje, er urent, så gå over til det Land, der er HERRENs Ejendom, der, hvor HERRENs Bolig står, og nedsæt eder iblandt os; men vær ikke genstridige mod HERREN, ej heller mod os ved at bygge eder et Alter til foruden HERREN vor Guds Alter!
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Dengang Akan, Zeras Søn, øvede Svig med det bandlyste, kom der da ikke Vrede over hele Israels Menighed, skønt han kun var en enkelt Mand? Måtte han ikke dø for sin Brøde?"
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
Da svarede Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme overhovederne for Israels Tusinder således:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
"Gud, Gud HERREN, Gud, Gud HERREN ved det, og Israel skal vide det: Hvis det er i Genstridighed eller Troløshed mod HERREN, i den Hensigt at vende os fra HERREN,
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
at vi har bygget os et Alter, gid han så må unddrage os sin Hjælp i Dag! Hvis det er for at bringe Brændofre og Afgrødeofre derpå eller for at bringe Takofre derpå, så straffe HERREN det!
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
Nej, vi har gjort det af Frygt for det Tilfælde, at eders Børn engang i Fremtiden skulde sige til vore: Hvad har I med HERREN, Israels Gud, at gøre?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
HERREN har jo sat Jordan som Grænse imellem os, og eder, Rubeniter og Gaditer; I har ingen Del i HERREN! Og således kunde eders Børn få vore til at høre op med at frygte HERREN.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Derfor tænkte vi: Lad os bygge dette Alter, ikke til Brændoffer eller Slagtoffer,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
men for at det kan være Vidne mellem os og eder og mellem vore Efterkommere efter os om, at vi vil forrette HERRENs Tjeneste' for hans Åsyn med vore Brændofre, Slagtofre og Takofre, for at eders Børn ikke engang i Fremtiden skal sige til vore: I har ingen Del i HERREN!
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Og vi tænkte: Hvis de i Fremtiden siger således til os og vore Efterkommere, så siger vi: Læg dog Mærke til, hvorledes det HERRENs Alter er bygget, som vore Forfædre rejste, ikke til Brændofre eller Slagtofre, men for at det kunne være Vidne mellem os og eder.
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Det være langt fra os at være genstridige mod HERREN eller vende os fra HERREN i Dag ved at bygge et Alter til Brændoffer, Afgrødeoffer og Slagtoffer foruden HERREN vor Guds Alter, som står foran hans Bolig!"
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
Da Præsten Pinehas og Menighedens Øverster og Overhovederne for Israels Tusinder, som ledsagede ham, hørte de Ord, som Rubeniterne, Gaditerne og Manassiterne talte, var de tilfredse,
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
og Pinehas, Præsten Eleazars Søn, sagde til Rubeniterne, Gaditerne og Manassiterne: "I Dag erkender vi, at HERREN er iblandt os, siden I ikke har øvet denne Svig imod HERREN; derved har I frelst Israeliterne fra HERRENs Hånd!"
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
Derpå vendte Pinehas, Præsten Eleazars Søn, og Øversteme tilbage fra Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme i Gilead til Israeliterne i Kana'ans Land og aflagde dem Beretning,
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
og Israeliterne var tilfredse ved Meddelelsen, og Israeliterne priste Gud og tænkte ikke mere på at drage i Kamp mod dem for at ødelægge det Land, Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme boede i.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
Og Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme kaldte Alteret: Vidne; "thi," sagde de, "det skal være Vidne mellem os om, at HERREN er Gud!"