< Yoswa 21 >
1 Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
Kemudian para pemimpin suku Lewi datang kepada Imam Besar Eleazar, Yosua, dan para pemimpin suku-suku Israel lainnya di Silo, di negeri Kanaan. Kata mereka, “TUHAN sudah memerintahkan Musa untuk memberikan kota-kota kepada kami sebagai tempat tinggal, dan padang rumput untuk ternak kami.”
2 ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
Maka orang Israel memberikan kota-kota dan padang rumput dari wilayah mereka kepada suku Lewi, sesuai perintah TUHAN.
4 Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
Undian pembagian tanah pertama diberikan kepada marga Kehat dalam suku Lewi. Keturunan Imam Harun mendapat tiga belas kota dari suku Yehuda, Simeon, dan Benyamin.
5 Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
Keturunan marga Kehat lainnya mendapat sepuluh kota dari suku Efraim, suku Dan, dan separuh suku Manasye di barat.
6 Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
Marga Gerson menerima tiga belas kota dari suku Isakar, suku Asyer, suku Naftali, dan separuh suku Manasye di timur.
7 Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
Marga Merari menerima dua belas kota dari suku Ruben, Gad, dan Zebulon.
8 Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Demikianlah orang Israel memberikan kota-kota dan padang-padang rumput untuk menggembalakan ternak kepada orang-orang Lewi dengan cara undian, sesuai perintah TUHAN kepada Musa.
9 Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
Keturunan Imam Harun dari marga Kehat menerima undian yang pertama. Bangsa Israel memberikan kepada mereka tiga belas kota serta padang-padang rumput di sekitarnya untuk menggembalakan ternak: sembilan kota dari suku Yehuda dan Simeon, empat kota dari suku Benyamin. Kota-kota dari suku Yehuda dan Simeon adalah Hebron, Libna, Yatir, Estemoa, Holon, Debir, Ain, Yutah, dan Bet Semes. Kota Hebron, yang terletak di pegunungan suku Yehuda, adalah kota perlindungan bagi orang-orang yang tidak sengaja membunuh. Kota ini juga disebut Kiryat Arba. Arba adalah nenek moyang raksasa Anakim. Keturunan Imam Harun diberi padang rumput di sekeliling kota itu, tetapi tidak termasuk tanah ladang kota dan desa-desa di sekitarnya, karena daerah itu sudah diberikan kepada Kaleb. Kota-kota dari suku Benyamin adalah Gibeon, Geba, Anatot, dan Almon.
10 ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
16 Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
Keturunan marga Kehat lainnya menerima sepuluh kota serta padang rumput di sekitarnya untuk menggembalakan ternak: empat kota dari suku Efraim, empat kota dari suku Dan, dan dua kota dari separuh suku Manasye. Kota-kota dari suku Efraim adalah Sikem (kota perlindungan di pegunungan Efraim bagi orang yang tidak sengaja membunuh), Gezer, Kibzaim, dan Bet Horon. Kota-kota dari suku Dan adalah Elteke, Gibeton, Ayalon, dan Gat Rimon. Kota-kota dari separuh suku Manasye adalah Taanak dan Gat Rimon.
21 Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
Keturunan marga Gerson dalam suku Lewi menerima tiga belas kota dan padang-padang rumput untuk menggembalakan ternak: dua kota dari separuh suku Manasye, empat kota dari suku Isakar, empat kota dari suku Asyer, dan tiga kota dari suku Naftali. Kota-kota dari separuh suku Manasye adalah Golan di Basan, yang adalah kota perlindungan bagi orang yang tidak sengaja membunuh, dan Bestera. Kota-kota dari suku Isakar adalah Kison, Daberat, Yarmut, dan En Ganim. Kota-kota dari suku Asyer adalah Misal, Abdon, Helkat, dan Rehob. Kota-kota dari suku Naftali adalah Kedes di Galilea, yaitu kota perlindungan bagi orang yang tidak sengaja membunuh, Hamot Dor, dan Kartan.
28 Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
Keturunan marga Merari dalam suku Lewi menerima dua belas kota serta padang rumput di sekitarnya untuk menggembalakan ternak: empat kota dari suku Zebulon, empat kota dari suku Ruben, dan empat kota dari suku Gad. Kota-kota dari suku Zebulon adalah Yoknam, Karta, Dimna, dan Nahalal. Kota-kota dari suku Ruben adalah Bezer, Yahas, Kedemot, dan Mefaat. Kota-kota dari suku Gad adalah Ramot di Gilead, yaitu kota perlindungan untuk orang yang tidak segaja membunuh, Mahanaim, Hesbon, dan Yazer.
35 Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
Jadi, suku Lewi menerima empat puluh delapan kota di tengah-tengah suku-suku Israel lainnya. Setiap kota dikelilingi oleh padang-padang rumput untuk menggembalakan ternak. Padang-padang rumput itu juga diberikan kepada orang-orang Lewi.
42 Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
Dengan demikian, TUHAN memberikan kepada bangsa Israel seluruh negeri, seperti yang sudah Dia janjikan dengan sumpah kepada nenek moyang mereka. Bangsa Israel menguasai negeri itu serta menetap di sana.
44 Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
TUHAN memberi mereka ketenangan, sesuai dengan sumpah-Nya kepada nenek moyang mereka. Tidak ada satu pun musuh yang bisa melawan mereka. TUHAN menyerahkan semua musuh ke dalam tangan mereka.
45 Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
Tiada satu pun janji TUHAN yang tidak digenapi kepada bangsa Israel. Dia menepati semua janji-Nya.