< Yoswa 21 >

1 Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
And the princes of meynees of Leuy neiyiden to Eleazar, preest, and to Josue, sone of Nun, and to the duykis of kynredis, bi alle the lynagis of the sones of Israel;
2 ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
and the Leuytis spaken to hem in Sylo, of the lond of Canaan, and seiden, The Lord comaundide bi the honde of Moises, that citees schulden be youun to vs to dwelle ynne, and the subarbis of tho to werk beestis to be fed.
3 Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
And the sones of Israel yauen `of her possessiouns, bi comaundement of the Lord, citees and the subarbis of tho.
4 Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
And the lot yede out in to the meynee of Caath, of the sones of Aaron, preest, of the lynages of Juda, and of Symeon, and of Beniamyn, threttene citees;
5 Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
and to the othere of the sones of Caath, that is, to dekenes that weren left, of the lynagis of Effraym, and of Dan, and of the half lynage of Manasse, ten citees.
6 Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
Sotheli lot yede out to the sones of Gerson, that thei schulden take of the lynagis of Isachar, and of Aser, and of Neptalym, and of the half lynage of Manasses `in Basan, threttene citees in noumbre;
7 Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
and to the sones of Merari, bi her meynees, of the lynagis of Ruben, and of Gad, and of Zabulon, twelue citees.
8 Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
And the sones of Israel yauen to dekenes cytees, and the subarbis `of tho, as the Lord comaundide bi the hond of Moises; and alle yauen bi lot.
9 Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
Of the lynagis of the sones of Juda, and of Symeon, Josue yaf citees;
10 ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
to the sones of Aaron, bi the meynees of Caath, of the kyn of Leuy, of whiche citees these ben the names; for the firste lot yede out to hem;
11 Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
Cariatharbe, of the fadir of Enach, which is clepid Ebron, in the hil of Juda, and the subarbis therof bi cumpas;
12 Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
sotheli he hadde youe the feeldis and townes therof to Caleph, sone of Jephone, to haue in possessioun.
13 Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
Therfor Josue yaf to the sones of Aaron, preest, Ebron, a citee of refuyt, and the subarbis `of it, and Lebnam with hise subarbis,
14 Yatiri, Esitemowa,
and Jether, and Yschymon,
15 Holoni, Debri,
and Elon, and Dabir, and Ayn, and Lethan,
16 Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
and Bethsames, with her subarbis; nyne citees, of twei lynagis, as it is seid.
17 Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
Sotheli of the lynage of the sones of Beniamyn, he yaf Gabaon, and Gabee, and Anatoth, and Almon, with her subarbis;
18 Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
`foure citees.
19 Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
Alle the citees togidere of the sones of Aaron, preest, weren threttene, with her subarbis.
20 Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
Forsothe to `the othere, bi the meynees of the sones of Caath, of the kyn of Leuy, this possessioun was youun;
21 Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
of the lynage of Effraym, the citee of refuyt, Sichen, with hise subarbis, in the hil of Effraym, and Gazer,
22 Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
and Sebsam, and Bethoron, with her subarbis;
23 Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
`foure citees; also of the lynage of Dan, Helthece, and Gebethon, and Haialon,
24 Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
and Gethremmon, with her subarbis;
25 Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
`foure citees; sotheli of the half lynage of Manasses, Thanach, and Gethremon, with her subarbis; `twei citees.
26 Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
Alle the citees ten, and the subarbis `of tho weren youun to the sones of Caath, of the lowere degree.
27 Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
Also to the sones of Gerson, of the kyn of Leuy, Josue yaf of the half lynage of Manasses, citees of refuyt, Gaulon in Basan, and Bosra, with her subarbis, `twei citees.
28 Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
Forsothe of the lynage of Isachar, he yaf Cesion, and Daberath,
29 Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
and Jerimoth, and Engannym, with her subarbis; `foure citees.
30 Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
Of the lynage of Aser, he yaf Masal, and Abdon,
31 Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
and Elecath, and Roob, with her subarbis; `foure citees.
32 Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Also of the lynage of Neptalym, `he yaf the citee of refuyt, Cedes in Galile, and Amodor, and Carthan, with her subarbis; `thre citees.
33 Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
Alle the citees of the meynees of Gerson weren threttene, with her subarbis.
34 Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
Sotheli to the sones of Merary, dekenes of the lowere degree, bi her meynees, was youun Getheran, of the linage of Zabulon, and Charcha, and Demna, and Nalol;
35 Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
`foure citees, with her subarbis.
36 Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
And of the lynage of Gad, he yaf the citee of refuyt, Ramoth in Galaad, and Manaym, and Esebon, and Jaser; `foure citees, with her subarbis.
37 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
And of the lynage of Ruben, biyende Jordan, ayens Jerico, he yaf `the citee of refuyt, Bosor in the wildirnesse of Mysor, and Jazer, and Jecson, and Maspha; `foure citees, with her subarbis.
38 Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
39 Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
Alle the citees of Merary, bi her meynees and kynredis, weren twelue.
41 Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
And so alle the citees of Leuytis, in the myddis of possessioun of the sones of Israel, weren eiyte and fourti, with her subarbis;
42 Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
and alle citees weren departid by meynees.
43 Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
And the Lord yaf to Israel al the lond which he swoor hym silf to yyue to the fadris `of hem, and thei hadden it in possessioun, and dwelliden therynne.
44 Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
And pees was youun of hym in to alle naciouns `by cumpas; and noon of enemyes was hardi to withstonde hem, but alle weren dryuen in to the lordschip `of hem.
45 Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
Forsothe nether o word, which he bihiyte him silf to yyue to hem, was voide, but alle wordis weren fillid in werkis.

< Yoswa 21 >