< Yoswa 21 >

1 Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
Then the heads of fathers’ houses of the Levites came near to Eleazar the priest, and to Joshua the son of Nun, and to the heads of fathers’ houses of the tribes of the children of Israel.
2 ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
They spoke to them at Shiloh in the land of Canaan, saying, “Yahweh commanded through Moses to give us cities to dwell in, with their pasture lands for our livestock.”
3 Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
The children of Israel gave to the Levites out of their inheritance, according to the commandment of Yahweh, these cities with their pasture lands.
4 Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
The lot came out for the families of the Kohathites. The children of Aaron the priest, who were of the Levites, had thirteen cities by lot out of the tribe of Judah, out of the tribe of the Simeonites, and out of the tribe of Benjamin.
5 Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
The rest of the children of Kohath had ten cities by lot out of the families of the tribe of Ephraim, out of the tribe of Dan, and out of the half-tribe of Manasseh.
6 Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
The children of Gershon had thirteen cities by lot out of the families of the tribe of Issachar, out of the tribe of Asher, out of the tribe of Naphtali, and out of the half-tribe of Manasseh in Bashan.
7 Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
The children of Merari according to their families had twelve cities out of the tribe of Reuben, out of the tribe of Gad, and out of the tribe of Zebulun.
8 Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
The children of Israel gave these cities with their pasture lands by lot to the Levites, as Yahweh commanded by Moses.
9 Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
They gave out of the tribe of the children of Judah, and out of the tribe of the children of Simeon, these cities which are mentioned by name:
10 ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
and they were for the children of Aaron, of the families of the Kohathites, who were of the children of Levi; for theirs was the first lot.
11 Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
They gave them Kiriath Arba, named after the father of Anak (also called Hebron), in the hill country of Judah, with its pasture lands around it.
12 Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
But they gave the fields of the city and its villages to Caleb the son of Jephunneh for his possession.
13 Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
To the children of Aaron the priest they gave Hebron with its pasture lands, the city of refuge for the man slayer, Libnah with its pasture lands,
14 Yatiri, Esitemowa,
Jattir with its pasture lands, Eshtemoa with its pasture lands,
15 Holoni, Debri,
Holon with its pasture lands, Debir with its pasture lands,
16 Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
Ain with its pasture lands, Juttah with its pasture lands, and Beth Shemesh with its pasture lands: nine cities out of those two tribes.
17 Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
Out of the tribe of Benjamin, Gibeon with its pasture lands, Geba with its pasture lands,
18 Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Anathoth with its pasture lands, and Almon with its pasture lands: four cities.
19 Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
All the cities of the children of Aaron, the priests, were thirteen cities with their pasture lands.
20 Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
The families of the children of Kohath, the Levites, even the rest of the children of Kohath, had the cities of their lot out of the tribe of Ephraim.
21 Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
They gave them Shechem with its pasture lands in the hill country of Ephraim, the city of refuge for the man slayer, and Gezer with its pasture lands,
22 Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Kibzaim with its pasture lands, and Beth Horon with its pasture lands: four cities.
23 Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
Out of the tribe of Dan, Elteke with its pasture lands, Gibbethon with its pasture lands,
24 Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Aijalon with its pasture lands, Gath Rimmon with its pasture lands: four cities.
25 Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
Out of the half-tribe of Manasseh, Taanach with its pasture lands, and Gath Rimmon with its pasture lands: two cities.
26 Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
All the cities of the families of the rest of the children of Kohath were ten with their pasture lands.
27 Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
They gave to the children of Gershon, of the families of the Levites, out of the half-tribe of Manasseh Golan in Bashan with its pasture lands, the city of refuge for the man slayer, and Be Eshterah with its pasture lands: two cities.
28 Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
Out of the tribe of Issachar, Kishion with its pasture lands, Daberath with its pasture lands,
29 Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Jarmuth with its pasture lands, En Gannim with its pasture lands: four cities.
30 Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
Out of the tribe of Asher, Mishal with its pasture lands, Abdon with its pasture lands,
31 Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Helkath with its pasture lands, and Rehob with its pasture lands: four cities.
32 Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Out of the tribe of Naphtali, Kedesh in Galilee with its pasture lands, the city of refuge for the man slayer, Hammothdor with its pasture lands, and Kartan with its pasture lands: three cities.
33 Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
All the cities of the Gershonites according to their families were thirteen cities with their pasture lands.
34 Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
To the families of the children of Merari, the rest of the Levites, out of the tribe of Zebulun, Jokneam with its pasture lands, Kartah with its pasture lands,
35 Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Dimnah with its pasture lands, and Nahalal with its pasture lands: four cities.
36 Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
Out of the tribe of Reuben, Bezer with its pasture lands, Jahaz with its pasture lands,
37 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Kedemoth with its pasture lands, and Mephaath with its pasture lands: four cities.
38 Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
Out of the tribe of Gad, Ramoth in Gilead with its pasture lands, the city of refuge for the man slayer, and Mahanaim with its pasture lands,
39 Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
Heshbon with its pasture lands, Jazer with its pasture lands: four cities in all.
40 Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
All these were the cities of the children of Merari according to their families, even the rest of the families of the Levites. Their lot was twelve cities.
41 Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
All the cities of the Levites among the possessions of the children of Israel were forty-eight cities with their pasture lands.
42 Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
Each of these cities included their pasture lands around them. It was this way with all these cities.
43 Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
So Yahweh gave to Israel all the land which he swore to give to their fathers. They possessed it, and lived in it.
44 Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
Yahweh gave them rest all around, according to all that he swore to their fathers. Not a man of all their enemies stood before them. Yahweh delivered all their enemies into their hand.
45 Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
Nothing failed of any good thing which Yahweh had spoken to the house of Israel. All came to pass.

< Yoswa 21 >