< Yoswa 20 >
1 Pambuyo pake Yehova anati kwa Yoswa:
Потом рече Господ Исусу говорећи:
2 “Uza Aisraeli kuti apatule mizinda yopulumukiramo, monga ine ndinakulangizira kudzera mwa Mose,
Кажи синовима Израиљевим и реци: Одредите градове за уточишта, за које сам вам говорио преко Мојсија,
3 kuti aliyense amene wapha munthu mosazindikira osati mwadala azithawirako. Motero adzatetezedwa kwa wolipsira.
Да онамо утече крвник који убије кога нехотице, не мислећи, да вам буду уточишта од осветника.
4 Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo.
Па кад ко утече у који од тих градова, нека стане пред вратима градским и нека каже старешинама оног града ствар своју, па нека га приме к себи, и дају му место да седи код њих.
5 Ngati munthu wolipsirayo amutsatira komweko atsogoleriwo asapereke munthu wakuphayo chifukwa anapha Mwisraeli mnzakeyo mosazindikira, osati mwachiwembu.
И ако дође за њим осветник, нека му не дају крвника у руке, јер је нехотице убио ближњег нити је пре мрзео на њега.
6 Munthu wakuphayo adzakhalabe mu mzindawo mpaka atayimbidwa mlandu pamaso pa gulu lonse, ndiponso mpaka atamwalira mkulu wa ansembe amene akutumikira pa nthawiyo. Pamenepo munthuyo atha kubwereranso ku mudzi kwawo kumene anachoka mothawa kuja.”
Него нека седи у граду оном докле не стане пред збор на суд, до смрти поглавара свештеничког који буде онда, тада нека се крвник врати и иде у свој град и својој кући, у град из ког је утекао.
7 Choncho iwo anapatula Kedesi mʼdera la Galileya ku mapiri a Nafutali, Sekemu ku mapiri a Efereimu, ndi Kiriati Ariba (ndiye Hebroni) ku mapiri a Yuda.
И оделише Кедес у Галилеји у гори Нефталимовој и Сихем у гори Јефремовој и Киријат-Арву, то је Хеврон, у гори Јудиној.
8 Kummawa kwa Yorodani, mʼmapiri a chipululu a kummawa kwa Yeriko, anapatula Bezeri pakati pa dera la fuko la Rubeni. Anapatulanso Ramoti ku Giliyadi mʼdera la fuko la Gadi, ndiponso Golani ku Basani mʼdera la fuko la Manase.
А преко Јордана од Јерихона на исток одредише Восор у пустињи, у равни, од племена Рувимовог, и Рамот у Галаду од племена Гадовог, и Голан у Васану од племена Манасијиног.
9 Imeneyi ndiyo inali mizinda yopulumukiramo ya Aisraeli onse ngakhalenso mlendo wokhala pakati pawo. Munthu aliyense wopha mnzake mwangozi ankathawira ku mizinda imeneyi. Munthu wolipsira sankaloledwa kuti aphe munthu wothawayo ngati mlandu wake sunazengedwe pamaso pa gulu lonse.
То су градови одређени свим синовима Израиљевим и дошљаку који живи међу њима, да побегне код њих ко год убије кога нехотице и да не погине од руке осветникове док не стане пред збор.