< Yoswa 2 >

1 Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
Potem Jozue, syn Nuna, wysłał potajemnie z Szittim dwóch szpiegów, mówiąc: Idźcie, obejrzyjcie ziemię i Jerycho. Poszli więc i weszli do domu [pewnej] nierządnicy, która miała na imię Rachab, i tam odpoczęli.
2 Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
I doniesiono królowi Jerycha: Oto [jacyś] mężczyźni spośród synów Izraela przyszli tu tej nocy, aby wybadać tę ziemię.
3 Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
Król Jerycha posłał więc do Rachab, rozkazując: Wyprowadź mężczyzn, którzy przyszli do ciebie i weszli do twego domu, bo przyszli wybadać całą tę ziemię.
4 Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
Kobieta jednak wzięła tych dwóch mężczyzn, ukryła ich i powiedziała: To prawda, że przyszli do mnie mężczyźni, ale nie wiedziałam, skąd oni są.
5 Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
A gdy miano zamykać bramę o zmierzchu, mężczyźni ci wyszli i nie wiem, dokąd poszli. Ścigajcie ich prędko, to ich dogonicie.
6 Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
Ona zaś zaprowadziła ich na dach i przykryła wiązkami lnu, które rozłożyła na dachu.
7 Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
[Wysłani] mężczyźni ścigali ich w kierunku Jordanu aż do brodów; i jak tylko ścigający wyszli, zamknięto bramę.
8 Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
A zanim usnęli, ona wyszła do nich na dach;
9 ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
I powiedziała do tych mężczyzn: Wiem, że PAN dał wam tę ziemię, bo strach przed wami padł na nas i wszyscy obywatele tej ziemi truchleją przed wami.
10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
Słyszeliśmy bowiem, jak PAN wysuszył przed wami wody Morza Czerwonego, gdy wychodziliście z Egiptu, i co uczyniliście dwom królom amoryckim, którzy byli po tamtej stronie Jordanu, Sichonowi i Ogowi, których pobiliście.
11 Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
Gdy [o tym] usłyszeliśmy, nasze serca struchlały i nie było już odwagi w nikim z waszego powodu; bo PAN, wasz Bóg, jest Bogiem wysoko na niebie i nisko na ziemi.
12 Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
Dlatego teraz, proszę, przysięgnijcie mi na PANA, że jak ja okazałam wam miłosierdzie, tak i wy okażecie miłosierdzie domowi mego ojca, i dajcie mi pewny znak;
13 Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
Że zachowacie przy życiu mego ojca i moją matkę, moich braci i moje siostry, i wszystko, co do nich należy, i ocalicie nas od śmierci.
14 Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
Odpowiedzieli jej mężczyźni: Ręczymy za was naszym życiem, jeśli nie wydacie tej naszej sprawy, i gdy PAN odda nam tę ziemię, okażemy ci miłosierdzie i wierność.
15 Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
Potem spuściła ich na sznurze z okna, bo jej dom przylegał do muru i ona mieszkała w murze.
16 Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
I powiedziała im: Idźcie w góry, by nie spotkali was ścigający; ukryjcie się tam przez trzy dni, aż powrócą ścigający, a potem pójdziecie swoją drogą.
17 Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
Mężczyźni powiedzieli jej: Będziemy wolni od tej przysięgi, którą kazałaś nam złożyć;
18 tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
Gdy wejdziemy do ziemi, przywiążesz do okna czerwony sznur, po którym nas spuściłaś, i zbierzesz u siebie, w domu swego ojca, swoją matkę, swoich braci i cały dom swego ojca.
19 Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
Ktokolwiek bowiem wyjdzie poza drzwi twego domu, jego krew [spadnie] mu na głowę, a my [będziemy] bez winy. Lecz krew każdego, kto będzie z tobą w domu, [spadnie] na naszą głowę, jeśli czyjaś ręka go dotknie.
20 Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
Jeśli jednak wydasz naszą sprawę, będziemy wolni od przysięgi, którą kazałaś nam złożyć.
21 Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
I odpowiedziała: Jak powiedzieliście, niech tak będzie. Wtedy wypuściła ich i poszli. I przywiązała czerwony sznur do okna.
22 Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
Odeszli więc i przyszli na górę, i pozostali tam przez trzy dni, aż powrócili ścigający. A ścigający szukali ich po wszystkich drogach, ale nie znaleźli.
23 Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
I zawrócili ci dwaj mężczyźni, zeszli z góry, przeprawili się [przez rzekę], przyszli do Jozuego, syna Nuna, i opowiedzieli mu wszystko, co się z nimi działo;
24 Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”
I mówili do Jozuego: PAN oddał w nasze ręce całą tę ziemię, bo wszyscy obywatele tej ziemi struchleli przed nami.

< Yoswa 2 >