< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Inkatho yesibili yasivela yaya kuSimeyoni, eyesizwe sabantwana bakoSimeyoni, ngokwensendo zabo. Lelifa labo laliphakathi kwelifa labantwana bakoJuda.
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
Elifeni labo-ke babeleBherishebha leShebha leMolada
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
leHazari-Shuwali leBala leEzema
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
leElitoladi leBethuli leHorma
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
leZikilagi leBeti-Marikabothi leHazari-Susa
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
leBeti-Lebawothi leSharuheni; imizi elitshumi lantathu lemizana yayo.
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
IEni, iRimoni leEtheri leAshani; imizi emine lemizana yayo.
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
Layo yonke imizana ezingelezele imizi le, kuze kufike eBahalathi-Beri, iRama yeningizimu. Leli yilifa lesizwe sabantwana bakoSimeyoni ngokwensendo zabo.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Ilifa labantwana bakoSimeyoni lavela enkathweni yabantwana bakoJuda; ngoba isigaba sabantwana bakoJuda sasisikhulu kakhulu kibo; ngakho abantwana bakoSimeyoni badla ilifa phakathi kwelifa labo.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
Inkatho yesithathu yasivela yaya kubantwana bakoZebuluni ngokwensendo zabo. Lomngcele welifa labo wafika eSaridi.
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
Umngcele wabo-ke wenyukela entshonalanga leMarala, wafinyelela eDabeshethi wafinyelela esifuleni esiphambi kweJokineyamu;
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
waphenduka uvela eSaridi usiya empumalanga lapho okuphuma khona ilanga emngceleni weKisilothi-Thabhori, waphuma waya eDaberathi, wenyukela eJafiya;
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
ususuka lapho wedlulela empumalanga, endaweni yokuphuma kwelanga, usiya eGitha-Heferi leItha-Kazini, waphumela eRimoni, uphendukela eNeya.
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
Lomngcele wayizingelezela enyakatho eHanathoni; lokuphuma kwawo kwaba sesihotsheni seJifitaheli.
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
LeKatathi leNahalali leShimironi leJidala leBhethelehema, imizi elitshumi lambili lemizana yayo.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
Leli yilifa labantwana bakoZebuluni ngokwensendo zabo: Imizi le lemizana yayo.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
Inkatho yesine yavela yaya kubantwana bakoIsakari ngokwensendo zabo.
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
Umngcele wabo-ke wawuyiJizereyeli leKesulothi leShunemi
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
leHafarayimi leShiyoni leAnaharathi
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
leRabithi leKishiyoni leAbezi
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
leRemethi leEni-Ganimi leEni-Hada leBeti-Pazezi.
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
Lomngcele wafinyelela eThabhori leShahazima leBeti-Shemeshi; lokuphuma komngcele wabo kwakuseJordani; imizi elitshumi lesithupha lemizana yayo.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
Leli yilifa lesizwe sabantwana bakoIsakari ngokwensendo zabo, imizi lemizana yayo.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
Inkatho yesihlanu yasivela yaya esizweni sabantwana bakoAsheri ngokwensendo zabo.
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
Umngcele wabo-ke wawuyiHelkathi leHali leBeteni leAkishafi
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
leAlameleki leAmadi leMishali; wasufinyelela eKharmeli entshonalanga leShihori-Libhinathi,
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
waphendukela lapho okuphuma khona ilanga usiya eBeti-Dagoni, wafinyelela eZebuluni lesihotsha seJifitaheli enyakatho waya eBeti-Emeki leNeyiyeli, waphumela eKabuli kwesokhohlo,
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
leEbroni leRehobi leHamoni leKana, kwaze kwaba seSidoni enkulu.
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
Umngcele wasuphendukela eRama, waya emzini obiyelweyo weTire; lomngcele waphendukela eHosa; lokuphuma kwawo kwakuselwandle, uvela esigabeni usiya eAkizibi
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
leUma leAfeki leRehobi; imizi engamatshumi amabili lambili lemizana yayo.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
Leli yilifa lesizwe sabantwana bakoAsheri ngokwensendo zabo, imizi le lemizana yayo.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
Inkatho yesithupha yavela yaya kubantwana bakoNafithali, eyabantwana bakoNafithali ngokwensendo zabo.
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
Umngcele wabo wasusuka eHelefi, esihlahleni se-okhi eZahananimi leAdami-Nekebi leJabineli, kwaze kwaba seLakumi; lokuphuma kwawo kwakuseJordani.
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
Umngcele wasuphendukela entshonalanga usiya eAzinothi-Thabhori, waphuma lapho waya eHukoki, wafinyelela eZebuluni ngeningizimu, leAsheri wafinyelela entshonalanga, leJuda eJordani lapho okuphuma khona ilanga.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
Njalo imizi ebiyelweyo yile: IZidimi, iZeri, leHamathi, iRakathi, leKinerethi,
36 Adama, Rama, Hazori,
leAdama, leRama, leHazori,
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
leKedeshi, leEdreyi, leEni-Hazori,
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
leYironi, leMigidali-Eli, iHorema, leBeti-Anathi, leBeti-Shemeshi; imizi elitshumi lesificamunwemunye lemizana yayo.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
Leli yilifa lesizwe sabantwana bakoNafithali ngokwensendo zabo, imizi lemizana yayo.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
Inkatho yesikhombisa yavela yaya esizweni sabantwana bakoDani ngokwensendo zabo.
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
Lomngcele welifa labo wawuyiZora leEshitawoli leIri-Shemeshi
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
leShahalabini leAjaloni leJithila
43 Eloni, Timna, Ekroni,
leEloni leTiminatha leEkhironi
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
leEliteke leGibethoni leBahalathi
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
leJehudi leBene-Beraki leGathi-Rimoni
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
leMe-Jarkoni leRakoni kanye lomngcele oqondene leJafo.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
Lomngcele wabantwana bakoDani wavela umncinyane kakhulu kubo. Ngakho abantwana bakoDani benyuka ukuyakulwa bemelene leLeshema; sebeyithumbile bayitshaya ngobukhali benkemba, badla ilifa layo, bahlala kiyo, bayibiza iLeshema ngokuthi yiDani, ngebizo likaDani uyise.
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
Leli yilifa lesizwe sabantwana bakoDani ngokwensendo zabo, imizi le lemizana yayo.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
Kwathi sebeqedile ukwaba ilizwe libe yilifa ngokwemingcele yalo, abantwana bakoIsrayeli bamnika uJoshuwa indodana kaNuni ilifa phakathi kwabo.
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
Ngokomlayo weNkosi bamnika umuzi awucelayo, iThiminathi-Sera entabeni yakoEfrayimi, wasesakha umuzi, wahlala kuwo.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
La ngamafa uEleyazare umpristi loJoshuwa indodana kaNuni lenhloko zaboyise zezizwe zabantwana bakoIsrayeli abawaba aba yilifa ngenkatho eShilo phambi kweNkosi, emnyango wethente lenhlangano. Baqeda-ke ukulaba ilizwe.

< Yoswa 19 >