< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
And the second lot came forth to Simeon, even for the tribe of the children of Simeon according to their families: and their inheritance was within the inheritance of the children of Judah.
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
And they had in their inheritance Beersheba, and Sheba, and Moladah,
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
And Hazarshual, and Balah, and Azem,
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
And Eltolad, and Bethul, and Hormah,
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
And Ziklag, and Bethmarcaboth, and Hazarsusah,
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
And Bethlebaoth, and Sharuhen; thirteen cities and their villages:
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
Ain, Remmon, and Ether, and Ashan; four cities and their villages:
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
And all the villages that were around these cities to Baalathbeer, Ramath of the south. This is the inheritance of the tribe of the children of Simeon according to their families.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Out of the portion of the children of Judah was the inheritance of the children of Simeon: for the part of the children of Judah was too much for them: therefore the children of Simeon had their inheritance within the inheritance of them.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
And the third lot came up for the children of Zebulun according to their families: and the border of their inheritance was to Sarid:
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
And their border went up toward the sea, and Maralah, and reached to Dabbasheth, and reached to the river that is before Jokneam;
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
And turned from Sarid eastward toward the sunrising to the border of Chislothtabor, and then goeth out to Daberath, and goeth up to Japhia,
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
And from there passeth along on the east to Gittahhepher, to Ittahkazin, and goeth out to Remmonmethoar to Neah;
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
And the border went around it on the north side to Hannathon: and the ends of it are in the valley of Jiphthahel:
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
And Kattath, and Nahallal, and Shimron, and Idalah, and Bethlehem: twelve cities with their villages.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
This is the inheritance of the children of Zebulun according to their families, these cities with their villages.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
And the fourth lot came out to Issachar, for the children of Issachar according to their families.
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
And their border was toward Jezreel, and Chesulloth, and Shunem,
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
And Hapharaim, and Shion, and Anaharath,
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
And Rabbith, and Kishion, and Abez,
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
And Remeth, and Engannim, and Enhaddah, and Bethpazzez;
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
And the border reacheth to Tabor, and Shahazimah, and Bethshemesh; and the ends of their border were at Jordan: sixteen cities with their villages.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
This is the inheritance of the tribe of the children of Issachar according to their families, the cities and their villages.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
And the fifth lot came out for the tribe of the children of Asher according to their families.
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
And their border was Helkath, and Hali, and Beten, and Achshaph,
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
And Alammelech, and Amad, and Misheal; and reacheth to Carmel westward, and to Shihorlibnath;
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
And turneth toward the sunrising to Bethdagon, and reacheth to Zebulun, and to the valley of Jiphthahel toward the north side of Bethemek, and Neiel, and goeth out to Cabul on the left hand,
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
And Hebron, and Rehob, and Hammon, and Kanah, even to great Zidon;
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
And then the border turneth to Ramah, and to the strong city Tyre; and the border turneth to Hosah; and the ends of it are at the sea from the border to Achzib:
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
Ummah also, and Aphek, and Rehob: twenty and two cities with their villages.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
This is the inheritance of the tribe of the children of Asher according to their families, these cities with their villages.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
The sixth lot came out to the children of Naphtali, even for the children of Naphtali according to their families.
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
And their land was from Heleph, from Allon to Zaanannim, and Adami, Nekeb, and Jabneel, to Lakum; and its ends were at Jordan:
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
And then the border turneth westward to Aznothtabor, and goeth out from there to Hukkok, and reacheth to Zebulun on the south side, and reacheth to Asher on the west side, and to Judah upon Jordan toward the sunrising.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
And the fortified cities are Ziddim, Zer, and Hammath, Rakkath, and Chinnereth,
36 Adama, Rama, Hazori,
And Adamah, and Ramah, and Hazor,
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
And Kedesh, and Edrei, and Enhazor,
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
And Iron, and Migdalel, Horem, and Bethanath, and Bethshemesh; nineteen cities with their villages.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
This is the inheritance of the tribe of the children of Naphtali according to their families, the cities and their villages.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
And the seventh lot came out for the tribe of the children of Dan according to their families.
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
And the land of their inheritance was Zorah, and Eshtaol, and Irshemesh,
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
And Shaalabbin, and Ajalon, and Jethlah,
43 Eloni, Timna, Ekroni,
And Elon, and Thimnathah, and Ekron,
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
And Eltekeh, and Gibbethon, and Baalath,
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
And Jehud, and Beneberak, and Gathrimmon,
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
And Mejarkon, and Rakkon, with the border opposite Japho.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
And the border of the children of Dan went out too little for them: therefore the children of Dan went up to fight against Leshem, and took it, and smote it with the edge of the sword, and possessed it, and dwelt in it, and called Leshem, Dan, after the name of Dan their father.
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
This is the inheritance of the tribe of the children of Dan according to their families, these cities with their villages.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
When they had finished dividing the land for inheritance by their borders, the children of Israel gave an inheritance to Joshua the son of Nun among them:
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
According to the word of the LORD they gave him the city which he asked, even Timnathserah in mount Ephraim: and he built the city, and dwelt in it.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
These are the inheritances, which Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun, and the heads of the fathers of the tribes of the children of Israel, divided for an inheritance by lot in Shiloh before the LORD, at the door of the tabernacle of the congregation. So they made an end of dividing the country.

< Yoswa 19 >