< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
The second lot came out for Simeon, even for the tribe of the descendants of Simeon according to their families. Their inheritance was in the midst of the inheritance of the descendants of Judah.
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
And they had for their inheritance Beersheba, and Moladah,
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
and Hazar Shual, and Balah, and Ezem,
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
and Eltolad, and Bethul, and Hormah,
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
and Ziklag, and Beth Marcaboth, and Hazar Susah,
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
and Beth Lebaoth, and Sharuhen; thirteen cities with their villages;
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
En Rimmon, and Token, and Ether, and Ashan; four cities with their villages;
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
and all the villages that were around these cities to Baalath Beer, Ramath Negev. This is the inheritance of the tribe of the descendants of Simeon according to their families.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
Out of the part of the descendants of Judah was the inheritance of the descendants of Simeon; for the portion of the descendants of Judah was too much for them. Therefore the descendants of Simeon had inheritance in the midst of their inheritance.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
And the third lot came up for the descendants of Zebulun according to their families, and the border of their inheritance was to Sadud.
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
Their border went up westward, and to Maralah, and reached to Dabbesheth, and it reached to the wadi that is before Jokneam.
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
And it turned from Sadud eastward toward the sunrise to the border of Chisloth Tabor, and it went out to Daberath, and went up to Japhia.
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
From there it passed along eastward to Gath Hepher, to Eth Kazin; and it went out to Rimmon which bends toward Neah.
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
The border turned around it on the north to Hannathon; and it ended at the Valley of Iphtah El;
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
Kattath, Nahalal, Shim'on, Idalah, and Bethlehem: twelve cities with their villages.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
This is the inheritance of the descendants of Zebulun according to their families, these cities with their villages.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
The fourth lot came out for Issachar, even for the descendants of Issachar according to their families.
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
And their border was to Jezreel, and Chesulloth, and Shunem,
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
and Hapharaim, and Shion, and Anaharath,
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
and Daberath, and Kishion, and Ebez,
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
and Remeth, and Engannim, and En Haddah, and Beth Pazzez.
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
The border reached to Tabor, and Shahazumah, and Beth Shemesh; and their border ended at the Jordan: sixteen cities with their villages.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
This is the inheritance of the tribe of the descendants of Issachar according to their families, the cities with their villages.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
The fifth lot came out for the tribe of the descendants of Asher according to their families.
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
Their border was from Helkath (and Hali, and Beten, and Achshaph,
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
and Allammelech, and Amad, and Mishal) and it reached to Carmel westward, and to Shihor Libnath.
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
And it turned eastward to Beth Dagon, and reached to Zebulun and to the Valley of Iphtah El on the north. And the border goes north to Beth Emek and Neiel, and it went out to Cabul on the north,
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
and Abdon, and Rehob, and Hammon, and Kanah, even to Greater Sidon.
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
The border turned to Ramah, to the fortified city of Tyre; and the border turned to Hosah, and it ended at the sea; Mahalab, and Achzib,
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
and Acco, and Aphek, and Rehob: twenty-two cities with their villages.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
This is the inheritance of the tribe of the descendants of Asher according to their families, these cities with their villages.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
The sixth lot came out for the descendants of Naphtali, even for the descendants of Naphtali according to their families.
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
Their border was from Heleph, from the oak in Zaanannim, Adaminekeb, and Jabneel, to Lakkum. It ended at the Jordan.
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
The border turned westward to Aznoth Tabor, and went out from there to Hukkok. It reached to Zebulun on the south, and reached to Asher on the west, and to Judah at the Jordan toward the east.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
The fortified cities were Ziddim, Zer, Hammath, Rakkath, Kinnereth,
36 Adama, Rama, Hazori,
Adamah, Ramah, Hazor,
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
Kedesh, Edrei, En Hazor,
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
Yiron, Migdal El, Horem, Beth Anath, and Beth Shemesh; nineteen cities with their villages.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
This is the inheritance of the tribe of the descendants of Naphtali according to their families, the cities with their villages.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
The seventh lot came out for the tribe of the descendants of Dan according to their families.
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
And the border of their inheritance was Zorah, and Eshtaol, and Ir Shemesh,
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
and Shaalbin, and Aijalon, and Jithlah,
43 Eloni, Timna, Ekroni,
and Elon, and Timnah, and Ekron,
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
and Eltekeh, and Gibbethon, and Baalath,
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
and Jehud, and Azzur, and Bene Berak, and Gath Rimmon,
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
and from the sea, Jarkon, and Rakkon, with the border over against Joppa.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
And the border of the descendants of Dan slipped out of their control, so the descendants of Dan went up and fought against Leshem, and after capturing it and striking it with the sword they took possession of it and dwelt in it, and called Leshem, Dan, after the name of Dan their ancestor.
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
This is the inheritance of the tribe of the descendants of Dan according to their families, these cities with their villages.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
So they made an end of distributing the land for inheritance by its borders. The children of Israel gave an inheritance among them to Joshua the son of Nun.
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
According to the commandment of the LORD, they gave him the city which he asked, even Timnath Serah in the hill country of Ephraim; and he built the city, and lived there.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
These are the inheritances, which Eleazar the priest, Joshua the son of Nun, and the heads of ancestral houses of the tribes of the children of Israel distributed by lot in Shiloh before the LORD, at the door of the Tent of Meeting. So they made an end of dividing the land.

< Yoswa 19 >