< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
The second lot came out for the clans of the tribe of Simeon: Their inheritance lay within the territory of Judah
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
and included Beersheba (or Sheba), Moladah,
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
Hazar-shual, Balah, Ezem,
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
Eltolad, Bethul, Hormah,
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
Ziklag, Beth-marcaboth, Hazar-susah,
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
Beth-lebaoth, and Sharuhen—thirteen cities, along with their villages.
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
Ain, Rimmon, Ether, and Ashan—four cities, along with their villages,
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
and all the villages surrounding these cities as far as Baalath-beer (Ramah of the Negev). This was the inheritance of the clans of the tribe of Simeon.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
The inheritance of the Simeonites was taken from the territory of Judah, because the share for Judah’s descendants was too large for them. So the Simeonites received an inheritance within Judah’s portion.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
The third lot came up for the clans of the tribe of Zebulun: The border of their inheritance stretched as far as Sarid.
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
It went up westward to Maralah, reached Dabbesheth, and met the brook east of Jokneam.
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
From Sarid it turned eastward along the border of Chisloth-tabor and went on to Daberath and up to Japhia.
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
From there it crossed eastward to Gath-hepher and to Eth-kazin; it extended to Rimmon and curved around toward Neah.
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
Then the border circled around the north side of Neah to Hannathon and ended at the Valley of Iphtah-el.
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
It also included Kattath, Nahalal, Shimron, Idalah, and Bethlehem. There were twelve cities, along with their villages.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
This was the inheritance of the clans of the tribe of Zebulun, including these cities and their villages.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
The fourth lot came out for the clans of the tribe of Issachar:
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
Their territory included Jezreel, Chesulloth, Shunem,
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
Hapharaim, Shion, Anaharath,
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
Rabbith, Kishion, Ebez,
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
Remeth, En-gannim, En-haddah, and Beth-pazzez.
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
The border reached Tabor, Shahazumah, and Beth-shemesh, and ended at the Jordan. There were sixteen cities, along with their villages.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
This was the inheritance of the clans of the tribe of Issachar, including these cities and their villages.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
The fifth lot came out for the clans of the tribe of Asher:
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
Their territory included Helkath, Hali, Beten, Achshaph,
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
Allammelech, Amad, and Mishal. On the west the border touched Carmel and Shihor-libnath,
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
then turned eastward toward Beth-dagon, touched Zebulun and the Valley of Iphtah-el, and went north to Beth-emek and Neiel, passing Cabul on the left.
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
It went on to Ebron, Rehob, Hammon, and Kanah, as far as Greater Sidon.
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
The border then turned back toward Ramah as far as the fortified city of Tyre, turned toward Hosah, and came out at the Sea in the region of Achzib,
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
Ummah, Aphek, and Rehob. There were twenty-two cities, along with their villages.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
This was the inheritance of the clans of the tribe of Asher, including these cities and their villages.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
The sixth lot came out for the clans of the tribe of Naphtali:
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
Their border started at Heleph and the great tree of Zaanannim, passing Adami-nekeb and Jabneel as far as Lakkum and ending at the Jordan.
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
Then the border turned westward to Aznoth-tabor and ran from there to Hukkok, touching Zebulun on the south side, Asher on the west, and Judah at the Jordan on the east.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
The fortified cities were Ziddim, Zer, Hammath, Rakkath, Chinnereth,
36 Adama, Rama, Hazori,
Adamah, Ramah, Hazor,
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
Kedesh, Edrei, En-hazor,
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
Iron, Migdal-el, Horem, Beth-anath, and Beth-shemesh. There were nineteen cities, along with their villages.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
This was the inheritance of the clans of the tribe of Naphtali, including these cities and their villages.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
The seventh lot came out for the clans of the tribe of Dan:
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
The territory of their inheritance included Zorah, Eshtaol, Ir-shemesh,
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
Shaalabbin, Aijalon, Ithlah,
43 Eloni, Timna, Ekroni,
Elon, Timnah, Ekron,
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
Eltekeh, Gibbethon, Baalath,
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
Jehud, Bene-berak, Gath-rimmon,
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
Me-jarkon, and Rakkon, including the territory across from Joppa.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
(Later, when the territory of the Danites was lost to them, they went up and fought against Leshem, captured it, and put it to the sword. So they took possession of Leshem, settled there, and renamed it after their father Dan.)
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
This was the inheritance of the clans of the tribe of Dan, including these cities and their villages.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
When they had finished distributing the land into its territories, the Israelites gave Joshua son of Nun an inheritance among them,
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
as the LORD had commanded. They gave him the city of Timnath-serah in the hill country of Ephraim, as he requested. He rebuilt the city and settled in it.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
These are the inheritances that Eleazar the priest, Joshua son of Nun, and the heads of the families distributed by lot to the tribes of Israel at Shiloh before the LORD at the entrance to the Tent of Meeting. So they finished dividing up the land.

< Yoswa 19 >