< Yoswa 18 >
1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
Celotna skupnost Izraelovih otrok se je zbrala skupaj pri Šilu in tam postavila šotorsko svetišče skupnosti. In dežela je bila podjarmljena pred njimi.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Tam je med Izraelovimi otroki ostalo sedem rodov, ki še niso prejeli svoje dediščine.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
Józue je rekel Izraelovim otrokom: »Doklej se obirate, da greste, da vzamete v last deželo, ki vam jo je dal Gospod, Bog vaših očetov?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Dajte izmed sebe tri može za vsak rod in poslal jih bom in vstali bodo in šli skozi deželo in jo opisali glede na njihovo dediščino in ponovno bodo prišli k meni.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
To bodo razdelili na sedem delov. Juda bo ostal v svojih pokrajinah na jugu in Jožefova hiša bo ostala v svojih pokrajinah na severu.
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Vi boste torej opisali deželo v sedmih delih in opis prinesli sèm k meni, da lahko mečem žrebe za vas tukaj pred Gospodom, svojim Bogom.
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
Toda Lévijevci nimajo deleža med vami, kajti Gospodovo duhovništvo je njihova dediščina. Gad, Ruben in polovica Manásejevega rodu so prejeli svojo dediščino onkraj Jordana, na vzhodu, ki jim jo je dal Gospodov služabnik Mojzes.«
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Možje so vstali ter odšli stran in Józue jim je naročil, da gredo, da opišejo deželo, rekoč: »Pojdite in hodite skozi deželo in jo opišite in ponovno pridite k meni, da bom tukaj v Šilu za vas lahko vrgel žrebe pred Gospodom.«
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
Možje so odšli in šli skozi deželo in jo v knjigi opisali po mestih v sedmih delih in ponovno prišli k Józuetu, k vojski pri Šilu.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
Józue je zanje v Šilu metal žrebe pred Gospodom in tam je Józue Izraelovim otrokom razdelil deželo glede na njihove oddelke.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
Žreb rodu Benjaminovih otrok je prišel gor glede na njihove družine in pokrajina njihovega žreba je prišla naprej med Judovimi otroki in Jožefovimi otroki.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
Njihova meja na severni strani je bila od Jordana in meja je šla gor k strani Jerihe na severni strani in se dvigala skozi gore proti zahodu in njeni izhodi so bili pri divjini Bet Aven.
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
Meja je od tam šla preko, proti Luzu, k strani Luza, ki je Betel, proti jugu in meja se je spustila k Atrót Adárju, blizu hriba, ki leži na južni strani spodnjega Bet Horóna.
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
Meja je bila potegnjena od tam in obdala vogal morja proti jugu, od hriba, ki leži pred Bet Horónom proti jugu in njihovi izhodi so bili pri Kirját Báalu, ki je Kirját Jearím, mesto Judovih otrok. To je bila zahodna četrtina.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Južna četrtina je bila od konca Kirját Jearíma in meja se je nadaljevala na zahod in izšla pri izviru vodá Neftóaha
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
in meja se je spustila k vznožju gore, ki leži pred dolino sina Hinómovega in ki je v dolini velikanov na severu in se spustila k Hinómovi dolini, k strani Jebúsa na jugu in se spustila k En Rogelu
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
in potegnjena je bila od severa in šla naprej k En Šemešu in šla naprej proti Gelilótu, ki je nasproti vzpona k Adumímu in se spustila h kamnu Rubenovega sina Bohana
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
in šla naprej proti strani nasproti Arábi proti severu in se spustila k Arábi.
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
Meja je šla vzdolž strani Bet Hogle proti severu in izhodi meje so bili pri severnem zalivu slanega morja, pri južnem koncu Jordana. To je bila južna pokrajina.
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
Jordan je bil njegova meja na vzhodni strani. To je bila dediščina Benjaminovih otrok, po njihovih pokrajinah naokoli, glede na njihove družine.
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
Torej mesta rodov Benjaminovih otrok glede na njihove družine so bila Jeriha, Bet Hogla, dolina Kecíc,
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
Bet Arába, Cemarájim, Betel,
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Kefár Amoní, Ofní in Gaba, dvanajst mest z njihovimi vasmi.
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
Gibeón, Rama, Beerót,
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
Rekem, Jirpeél, Tarála,
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
Cela, Elef, Jebús, kar je Jeruzalem, Gíbea in Kirját, štirinajst mest z njihovimi vasmi. To je dediščina Benjaminovih otrok glede na njihove družine.