< Yoswa 18 >

1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
Inhlangano yonke-ke yabantwana bakoIsrayeli yabuthana eShilo, yamisa khona ithente lenhlangano. Lelizwe lalehliselwe phansi phambi kwabo.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Kwasekusele phakathi kwabantwana bakoIsrayeli izizwe eziyisikhombisa ezazingabelwanga ilifa lazo.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
UJoshuwa wasesithi kubantwana bakoIsrayeli: Koze kube nini lidonda ukuyakudla ilifa lelizwe iNkosi uNkulunkulu waboyihlo elinike lona?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Zinikeni amadoda amathathu ngesizwe, ngiwathume, asukume ahambe adabule ilizwe, alibhale ngokwelifa lazo, abuye kimi.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
Azalehlukanisa libe yizabelo eziyisikhombisa; uJuda uzahlala emngceleni wakhe eningizimu, labendlu kaJosefa bahlale emngceleni wabo enyakatho.
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Lani lizabhala ilizwe ngezigaba eziyisikhombisa, beseliletha kimi lapha, ukuthi ngiliphosele inkatho lapha phambi kweNkosi uNkulunkulu wethu.
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
Ngoba amaLevi kawalasabelo phakathi kwenu, ngoba ubupristi beNkosi buyilifa labo. LoGadi loRubeni lengxenye yesizwe sakoManase sebethethe ilifa labo ngaphetsheya kweJordani empumalanga, uMozisi inceku yeNkosi eyabanika lona.
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Asesuka amadoda ahamba. UJoshuwa wawalaya ahambayo ukubhala ilizwe esithi: Hambani lidabule ilizwe lilibhale, libuyele kimi, ukuze ngiliphosele inkatho lapha phambi kweNkosi eShilo.
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
Ngakho amadoda ahamba adabula phakathi kwelizwe, alibhala ngemizi ngezigaba eziyisikhombisa egwalweni; asebuya kuJoshuwa enkambeni eShilo.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
UJoshuwa wasebaphosela inkatho eShilo phambi kweNkosi; uJoshuwa wasebabela lapho ilizwe abantwana bakoIsrayeli ngokwezigaba zabo.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
Inkatho yesizwe sabantwana bakoBhenjamini yavela ngokwensendo zabo. Lomngcele wenkatho yabo waphuma phakathi kwabantwana bakoJuda labantwana bakoJosefa.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
Lomngcele wabo ngenyakatho wasukela eJordani, lomngcele wenyuka ewatheni leJeriko enyakatho, wasusenyuka udabula entabeni usiya entshonalanga, lokuphuma kwawo kwaba senkangala yeBeti-Aveni.
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
Lomngcele wedlula usuka lapho waya eLuzi, ewatheni leLuzi, eyiBhetheli, ngeningizimu; lomngcele wehlela eAtarothi-Adari, eduze lentaba engeningizimu kweBhethi-Horoni engaphansi.
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
Umngcele wagoba-ke, waphenduka waya eceleni lentshonalanga ngeningizimu, kusukela entabeni emaqondana leBhethi-Horoni eningizimu; lokuphuma kwawo kwaba eKiriyathi-Bhali, eyiKiriyathi-Jeyarimi, umuzi wabantwana bakoJuda. Lolu luhlangothi lwentshonalanga.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Lohlangothi lweningizimu lusephethelweni leKiriyathi-Jeyarimi; lomngcele waphuma waya entshonalanga, waphuma waya emthonjeni wamanzi weNefitowa.
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
Umngcele wasusehla usiya ephethelweni lentaba emaqondana lesihotsha sendodana kaHinomu esisesihotsheni seziqhwaga enyakatho, wasusehlela esihotsheni seHinomu ewatheni lamaJebusi eningizimu, wehlela eEni-Rogeli;
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
wagoba usukela enyakatho waphuma eEni-Shemeshi, waphumela eGelilothi emaqondana lomqanso weAdumimi, wehlela elitsheni likaBohani indodana kaRubeni;
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
wadlulela ewatheni maqondana leAraba enyakatho, wehlela eAraba.
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
Umngcele wasusedlulela ewatheni leBeti-Hogila enyakatho, lokuphuma komngcele kwakusethekwini loLwandle lweTshwayi enyakatho, ephethelweni leJordani ngeningizimu. Lo ngumngcele weningizimu.
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
LeJordani ingumngcele walo ehlangothini lwempumalanga. Leli yilifa labantwana bakoBhenjamini ngemingcele yalo inhlangothi zonke, ngokwensendo zabo.
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
Lemizi yesizwe sabantwana bakoBhenjamini ngokwensendo zabo yile: IJeriko leBeti-Hogila leEmeki-Kezizi
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
leBeti-Araba leZemarayimi leBhetheli
23 Avimu, Para, Ofiri,
leAvimi lePara leOfira
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
leKefari-Amoni leOfini leGeba; imizi elitshumi lambili lemizana yayo.
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
IGibeyoni leRama leBeyerothi
26 Mizipa, Kefira, Moza
leMizipa leKefira leMoza
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
leRekemi leIripheyeli leTarala
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
leZela, iElefi, leJebusi, okuyiJerusalema, iGibeyathi, iKiriyathi; imizi elitshumi lane lemizana yayo. Leli yilifa labantwana bakoBhenjamini ngokwensendo zabo.

< Yoswa 18 >