< Yoswa 18 >

1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
Und es versammelte sich die ganze Gemeinde der Söhne Israels in Schiloh und richteten daselbst das Versammlungszelt auf; denn das Land war vor ihnen unterworfen.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Und es waren noch sieben Stämme unter den Söhnen Israels übrig, denen noch nicht ein Erbe verteilt war.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
Und Joschua sprach zu den Söhnen Israels: Wie lange wollt ihr lässig sein, hinzugehen und das Land einzunehmen, das Jehovah, der Gott eurer Väter, euch gegeben hat?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Gebet her für euch von je einem Stamm drei Männer, daß ich sie sende und sie sich aufmachen und im Land umhergehen und es beschreiben zum Behuf ihres Erbes und kommen zu mir.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
Und ihr sollt es in sieben Teile teilen. Judah bleibe im Mittagsland in seinen Grenzen stehen, und das Haus Joseph bleibe auf seinen Grenzen im Norden stehen!
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Und ihr sollt das Land in sieben Teile schreiben, und es zu mir hierher bringen, auf daß ich euch hier vor Jehovah, unserem Gott, das Los werfe.
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
Denn keinen Teil haben in eurer Mitte die Leviten; denn das Priestertum Jehovahs ist ihr Erbe. Und Gad und Ruben und der halbe Stamm Menaschehs haben jenseits des Jordans gegen den Aufgang ihr Erbe, das ihnen Mose, der Knecht Jehovahs, gegeben hat, genommen.
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Und die Männer machten sich auf und gingen. Und Joschua gebot denen, die gingen, das Land zu beschreiben und sprach: Gehet hin und durchwandelt das Land und beschreibt es und kommt zu mir zurück, auf daß ich hier vor Jehovah in Schiloh das Los für euch werfe.
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
Und die Männer gingen und durchzogen das Land und beschrieben es nach den Städten zu sieben Teilen in ein Buch und kamen zu Joschua in das Lager nach Schiloh.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
Und Joschua warf für sie das Los in Schiloh vor Jehovah, und Joschua verteilte allda das Land den Söhnen Israels nach ihren Teilen.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
Und herauf kam das Los des Stammes der Söhne Benjamins nach seinen Familien. Und die Grenze ihres Loses kam heraus zwischen den Söhnen Judahs und den Söhnen Josephs.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
Und ihre Grenze war an der Nordecke am Jordan, und die Grenze stieg auf hinter auf der Nordseite und ging hinauf auf den Berg gegen das Meer, und ihre Ausläufe waren nach der Wüste Beth Aven.
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
Und von dannen ging die Grenze hinüber nach Lus, an die Mittagseite von Lus, das ist Bethel, und die Grenze geht hinab nach Atroth Addar auf den Berg, der an der Mittagseite des unteren Beth-Chorons ist.
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
Und die Grenze erstreckte sich und wendete sich herum zur Westseite mittäglich von dem Berge, der gegen Mittag vor Beth-Choron liegt, und seine Ausläufe waren bis Kirjath-Baal, das ist Kirjath-Jearim, eine Stadt der Söhne Judahs. Dies ist die Westseite.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Und die Mittagsecke ist vom Ende von Kirjath-Jearim, und die Grenze ging aus meerwärts, und ging aus nach dem Brunnquell der Wasser des Nephtoach.
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
Und die Grenze ging hinab nach dem Ende des Berges, der vor der Schlucht Ben-Hinnoms, die im Talgrunde Rephaim gegen Mitternacht ist, und ging hinab in die Schlucht Hinnoms zur Mittagseite des Jebusiters und ging hinab bis En Rogel;
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
Und erstreckte sich von Mitternacht und ging hinaus nach En Schemesch und ging aus nach Geliloth, das der Steige Adummim gerade gegenüber, und geht hinab zum Stein Bohans, des Sohnes Rubens;
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
Und sie zog hinüber an die Seite der Arabah gegen Mitternacht und ging hinab nach der Arabah;
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
Und die Grenze ging hinüber nach dem Rücken von Beth-Choglah gegen Mitternacht, und waren seine Ausläufe, die Grenze nach der Zunge des Salzmeeres gegen Mitternacht an dem mittäglichen Ende des Jordans. Das ist die Grenze gegen Mittag.
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
Und der Jordan begrenzt es auf der Ostseite. Das ist das Erbe der Söhne Benjamins nach ihren Grenzen ringsum nach ihren Familien.
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
Und die Städte des Stammes der Söhne Benjamins nach ihren Familien waren Jericho und Beth-Chogla und Emik Geziz.
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
Und Beth-Arabah und Zemarajim und Bethel.
23 Avimu, Para, Ofiri,
Und Avim und Parah und Ophrah.
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Und Chephar Ammonai und Ophni und Geba, zwölf Städte und ihre Dörfer;
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
Gibeon und Ramah und Beeroth.
26 Mizipa, Kefira, Moza
Und Mizpeh und Chephirah und Mozah.
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
Und Rekem und Jirpeel und Tharalah.
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
Und Zela, Eleph und Jebusi, das ist Jerusalem, Gibath, Kirjath, vierzehn Städte und ihre Dörfer. Das ist das Erbe der Söhne Benjamins nach ihren Familien.

< Yoswa 18 >