< Yoswa 18 >

1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
Tous les enfants d’Israël s’assemblèrent à Silo, et là ils dressèrent le tabernacle de témoignage, et la terre leur fut soumise.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Or, étaient restées sept tribus des enfants d’Israël, lesquelles n’avaient pas encore reçu leurs possessions.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
Josué leur dit: Jusqu’à quand languirez-vous dans l’inaction, et n’entrerez-vous pas, pour la posséder, dans la terre que le Seigneur Dieu de vos pères vous a donnée?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Choisissez de chaque tribu trois hommes, afin que je les envoie, et qu’ils aillent, et parcourent cette terre; qu’ensuite ils la décrivent, selon le nombre de chaque multitude, et qu’ils me rapportent ce qu’ils auront décrit.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
Divisez entre vous la terre en sept parties: que Juda soit dans ses limites du côté austral, et Joseph du côté de l’aquilon.
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Décrivez la terre qui est au milieu d’eux en sept parts; ensuite vous viendrez ici vers moi, afin que, devant le Seigneur votre Dieu, je jette pour vous ici le sort,
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
Parce qu’il n’y a point de part parmi vous pour les Lévites, mais que le sacerdoce du Seigneur est leur héritage. Quant à Gad, à Ruben et à la demi-tribu de Manassé, déjà elles avaient reçu au-delà du Jourdain, au côté oriental, leurs possessions, que leur donna Moïse, serviteur du Seigneur.
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Lorsque ces hommes se furent levés pour aller décrire la terre, Josué leur ordonna, disant: Parcourez la terre, décrivez-la, et revenez vers moi, afin qu’ici, devant le Seigneur, à Silo, je jette pour vous le sort.
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
C’est pourquoi ils allèrent; et parcourant la terre avec soin, ils la divisèrent en sept parts, écrivant dans un livre; puis ils revinrent au camp, à Silo, vers Josué.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
Qui jeta les sorts devant le Seigneur, à Silo, et divisa la terre aux enfants d’Israël en sept parts.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
Or, le premier sort tomba sur les enfants de Benjamin, selon leurs familles, pour qu’ils possédassent la terre située entre les enfants de Juda et les enfants de Joseph.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
Et leur frontière fut vers l’aquilon à partir du Jourdain; s’avançant près du côté septentrional de Jéricho, et de là montant contre l’occident vers les montagnes, et parvenant jusqu’au désert de Bethaven;
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
Puis, passant vers le midi près de Luza, qui est la même que Béthel, elle descend à Ataroth-Addar vers la montagne qui est au midi de Beth-horon la basse;
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
Et s’abaisse en tournant contre la mer, au midi de la montagne qui regarde Beth-horon contre l’Africus; enfin elle se termine à Cariath-Baal, qui est appelée aussi à Cariathiarim, ville des enfants de Juda: telle est son étendue contre la mer, à l’occident.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Mais du côté du midi, sa frontière s’avance de Cariathiarim contre la mer et parvient jusqu’à la source des eaux de Nephtoa.
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
Et elle descend vers la partie de la montagne qui regarde la vallée des enfants d’Ennom, et qui est contre le côté septentrional, à l’extrémité de la vallée des Raphaïm. Elle descend aussi à Géennom (c’est-à-dire la vallée d’Ennom), à côté du Jébuséen, au midi, et elle parvient à la fontaine de Rogel,
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
Passant devant l’aquilon, et allant à Ensemès, c’est-à-dire. Fontaine du soleil,
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
Elle passe jusqu’aux tertres, qui sont vis-à-vis de la montée d’Adommim; elle descend à Abenboen, c’est-à-dire la pierre de Boen, fils de Ruben; elle passe du côté de l’aquilon jusqu’aux campagnes, et descend dans la plaine;
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
Elle s’avance vers l’aquilon au-delà de Beth-hagla, et elle se termine à la langue de la mer très salée du côté de l’aquilon, au bout du Jourdain, vers le côté austral,
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
Qui la termine du côté de l’orient: telle est la possession des enfants de Benjamin, selon leurs frontières d’alentour et leurs familles.
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
Ses villes étaient: Jéricho, Beth-hagla, la vallée de Casis,
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
Beth-Araba, Samaraïm, Béthel,
23 Avimu, Para, Ofiri,
Avim, Aphara, Ophéra,
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Le village d’Emona, Ophni et Gabée: douze villes et leurs villages;
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
Gabaon, Rama, Béroth,
26 Mizipa, Kefira, Moza
Mesphé, Caphara, Amosa,
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
Récem, Jaréphel, Taréla,
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
Sala, Elaph, Jébus, qui est Jérusalem, Gabaath et Cariath: quatorze villes et leurs villages. Telle est la possession des enfants de Benjamin, selon leurs familles.

< Yoswa 18 >