< Yoswa 18 >

1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
Toute la communauté des enfants d’Israël s’assembla à Silo et y installa la Tente d’assignation; le pays était conquis et à leur disposition.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Mais il restait, parmi les enfants d’Israël, sept tribus à qui on n’avait pas encore départi leur patrimoine.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
Josué dit à ces Israélites: "Combien de temps encore négligerez-vous de prendre possession du pays que vous a donné l’Eternel, le Dieu de vos pères?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Désignez vous-mêmes trois hommes par tribu, afin que je leur donne mission de parcourir le pays et d’en faire le plan selon les possessions à attribuer; après quoi, ils viendront me trouver.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
Ils le diviseront en sept parts, Juda devant conserver sa frontière au midi, et la maison de Joseph devant garder la sienne au nord.
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Vous ferez donc délimiter le pays en sept parts et m’apporterez le plan ici, où je les tirerai pour vous au sort devant l’Eternel, notre Dieu.
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
Car, pour ce qui est des Lévites, ils n’ont point de part au milieu de vous, le ministère de l’Eternel étant leur apanage; quant à Gad, à Ruben et à la demi-tribu de Manassé, ils ont reçu leur patrimoine sur la rive orientale du Jourdain, telle que Moïse, serviteur de l’Eternel, le leur a attribué."
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Les délégués se disposant à partir pour lever le plan du pays, Josué leur donna cet ordre: "Allez, parcourez le pays, faites-en le plan et revenez auprès de moi, afin qu’ici, à Silo, je vous le répartisse au sort, en présence de l’Eternel."
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
Les hommes partirent, traversèrent le pays, en dressèrent le plan par villes, en sept parties, sur un registre, et vinrent trouver Josué au camp, à Silo.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
Et Josué jeta le sort à Silo, devant l’Eternel, et il y répartit le pays entre les enfants d’Israël, selon leurs groupements.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
Le premier lot échut à la tribu des enfants de Benjamin, selon leurs familles; les confins que leur attribua le sort se trouvaient entre les enfants de Juda et ceux de Joseph.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
Leur limite, du côté du nord, partait du Jourdain, montait au côté nord de Jéricho, passait à l’ouest de la montagne, et aboutissait au désert de Beth-Avén.
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
De là, elle gagnait le côté méridional de Louz, nommée aussi Béthel, et descendait vers Atrot-Addar, sur la montagne qui est au sud de Bethorôn-le-Bas.
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
Puis elle s’infléchissait et tournait du côté de l’ouest, au midi de la montagne qui fait face à Bethorôn, et se terminait à Kiryath-Baal ou Kiryath-Yearîm, ville de la tribu de Juda: voilà pour le côté occidental.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Le côté du midi partait de l’extrémité de Kiryath-Yearîm, et continuait dans la direction de la mer et atteignait la source de Mê-Nephtoah;
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
puis la limite descendait à l’extrémité de la montagne faisant face à la vallée de Ben Hinnom, qui est au côté nord de la vallée des Rephaïm; suivait la vallée de Hinnom jusqu’au côté sud de Jébus et atteignait En-Roghel;
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
tournait au nord vers En-Chémech, de là vers Gheliloth, en face de la montée d’Adoummim, et descendait vers la Pierre de Bohân-ben-Ruben;
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
se poursuivait vers le côté nord de la Plaine, et atteignait Araba;
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
de là, elle passait au côté nord de Beth-Hogla, et aboutissait à la pointe nord de la mer Salée, à l’extrémité sud du Jourdain: telle était la frontière méridionale.
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
Et le Jourdain formait la limite du côté de l’orient. Telle fut, dans tout son circuit, la possession des enfants de Benjamin selon leurs familles.
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
Les villes de cette tribu, réparties entre ses familles, étaient: Jéricho, Beth-Hogla, Emek-Keçis;
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
Beth-Haaraba, Cemaraïm, Béthel;
23 Avimu, Para, Ofiri,
Awim, Para, Ofra;
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Kefar-Ammona, Ofni et Ghéba: douze villes, avec leurs bourgades.
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
Plus Gabaon, Rama, Beërot;
26 Mizipa, Kefira, Moza
Miçpé, Kefira, Moça;
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
Rékem, Yirpeël, Tareala;
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
Cèla, Elef, Jébus, la même que Jérusalem, Ghibeath, Kiryath: quatorze villes, avec leurs bourgades. Tel fut le patrimoine des descendants de Benjamin, selon leurs familles.

< Yoswa 18 >