< Yoswa 17 >
1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
Yusuf'un büyük oğlu Manaşşe'nin oymağı için kura çekildi. –Gilat ve Başan, Manaşşe'nin ilk oğlu Makir'e verilmişti. Çünkü Gilatlılar'ın atası olan Makir büyük bir savaşçıydı.–
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
Manaşşe soyundan gelen öbürleri –Aviezer, Helek, Asriel, Şekem, Hefer ve Şemidaoğulları– bu kuranın içindeydi. Bunlar boylarına göre Yusuf oğlu Manaşşe'nin erkek çocuklarıydı.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
Bunlardan Manaşşe oğlu, Makir oğlu, Gilat oğlu, Hefer oğlu Selofhat'ın erkek çocuğu olmadı; yalnız Mahla, Noa, Hogla, Milka ve Tirsa adında kızları vardı.
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
Bunlar, Kâhin Elazar'a, Nun oğlu Yeşu'ya ve önderlere gidip şöyle dediler: “RAB, Musa'ya erkek akrabalarımızla birlikte bize de mirastan pay verilmesini buyurdu.” RAB'bin bu buyruğu üzerine Yeşu, amcalarıyla birlikte onlara da mirastan pay verdi.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
Böylece Manaşşe oymağına Şeria Irmağı'nın doğusundaki Gilat ve Başan bölgelerinden başka on pay verildi.
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
Çünkü Manaşşe'nin kız torunları da erkek torunların yanısıra mirastan pay almışlardı. Gilat bölgesi ise Manaşşe'nin öbür oğullarına verilmişti.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
Manaşşe sınırı Aşer sınırından Şekem yakınındaki Mikmetat'a uzanıyor, buradan güneye kıvrılarak Eyn-Tappuah halkının topraklarına varıyordu.
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
Tappuah Kenti'ni çevreleyen topraklar Manaşşe'nindi. Ama Manaşşe sınırındaki Tappuah Kenti Efrayimoğulları'na aitti.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
Sonra sınır Kana Vadisi'ne iniyordu. Vadinin güneyinde Manaşşe kentleri arasında Efrayim'e ait kentler de vardı. Manaşşe sınırları vadinin kuzeyi boyunca uzanarak Akdeniz'de son buluyordu.
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
Güneydeki topraklar Efrayim'in, kuzeydeki topraklarsa Manaşşe'nindi. Böylece Manaşşe bölgesi Akdeniz'le, kuzeyde Aşer'le ve doğuda İssakar'la sınırlanmıştı.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
İssakar ve Aşer'e ait topraklardaki Beytşean ve köyleri, Yivleam'la köyleri, Dor, yani Dor sırtları halkıyla köyleri, Eyn-Dor halkıyla köyleri, Taanak halkıyla köyleri, Megiddo halkıyla köyleri Manaşşe'ye aitti.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
Ne var ki, Manaşşeoğulları bu kentleri tümüyle ele geçiremediler. Çünkü Kenanlılar buralarda yaşamaya kararlıydı.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
İsrailliler güçlenince, Kenanlılar'ı sürecek yerde, onları angaryasına çalıştırmaya başladılar.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
Yusufoğulları Yeşu'ya gelip, “Mülk olarak bize neden tek kurayla tek pay verdin?” dediler, “Çok kalabalığız. Çünkü RAB bizi bugüne dek alabildiğine çoğalttı.”
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
Yeşu, “O kadar kalabalıksanız ve Efrayim'in dağlık bölgesi size dar geliyorsa, Perizliler'in ve Refalılar'ın topraklarındaki ormanlara çıkıp kendinize yer açın” diye karşılık verdi.
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
Yusufoğulları, “Dağlık bölge bize yetmiyor” dediler, “Ancak hem Beytşean ve köylerinde, hem de Yizreel Vadisi'nde oturanların, ovada yaşayan bütün Kenanlılar'ın demirden savaş arabaları var.”
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
Yeşu Yusufoğulları'na, Efrayim ve Manaşşe oymaklarına şöyle dedi: “Kalabalıksınız ve çok güçlüsünüz. Tek kuraya kalmayacaksınız.
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
Dağlık bölge de sizin olacak. Orası ormanlıktır, ama ağaçları kesip açacağınız bütün topraklar sizin olur. Kenanlılar güçlüdür, demirden savaş arabalarına sahiptirler ama, yine de onları sürersiniz.”