< Yoswa 17 >
1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
I dopade dio plemenu Manasijinu, a on bješe prvenac Josifov; Mahiru prvencu Manasijinu ocu Galadovu, jer bješe èovjek junak, zato mu dopade Galad i Vasan;
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
Dobiše dio i ostali sinovi Manasijini po porodicama svojim, sinovi Avijezerovi, i sinovi Helekovi, i sinovi Azrilovi, i sinovi Sihemovi, i sinovi Eferovi, i sinovi Semidini. To su sinovi Manasije sina Josifova; ljudi po porodicama svojim.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
A Salpad sin Efera sina Galada sina Mahira sina Manasijina nije imao sinova nego kæeri; i ovo su imena kæerima njegovijem: Mala i Nuja, Egla, Melha i Tersa.
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
I one doðoše pred Eleazara sveštenika i pred Isusa sina Navina i pred knezove, i rekoše: Gospod je zapovjedio Mojsiju da nam se dade našljedstvo meðu braæom našom. I dade im Isus po zapovijesti Gospodnjoj našljedstvo meðu braæom oca njihova.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
I dopade Manasiji deset dijelova, osim zemlje Galadske i Vasanske, koje su s onu stranu Jordana.
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
Jer kæeri Manasijine dobiše našljedstvo meðu sinovima njegovijem, a zemlja Galadska dopade drugim sinovima Manasijinim.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
A meða Manasijina bješe od Asira k Mihmeti, koja je prema Sihemu, potom ide ta meða nadesno k stanovnicima En-Tafujskim.
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
A Manasijina je zemlja Tafujska, ali Tafuja na meði Manasijinoj pripada sinovima Jefremovijem.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
Odatle slazi meða na potok Kanu, s južne strane toga potoka; i gradovi su Jefremovi meðu gradovima Manasijinim; a meða je Manasijina sa sjeverne strane potoka i izlazi na more.
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
S juga je Jefremovo, a sa sjevera Manasijino, a more im je meða; i s Asirom granièe na sjeveru a s Isaharom na istoku.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
Jer je Manasijino u plemenu Isaharovu i Asirovu: Vet-San sa selima svojim, i Ivleam sa selima svojim, i Dorani sa selima svojim, i En-Dorani sa selima svojim, i Tanašani sa selima svojim, i Megiðani sa selima svojim; ta tri kraja.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
Ali sinovi Manasijini ne mogoše izagnati Hananeja iz tijeh gradova, nego Hananeji stadoše živjeti u toj zemlji.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
Ali kad ojaèaše sinovi Izrailjevi, udariše danak na Hananeje, ali ih ne izagnaše.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
A sinovi Josifovi rekoše Isusu govoreæi: zašto si nam dao u našljedstvo jedan dio i jedno uže, kad je nas množina i Gospod nas je blagoslovio dovde?
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
A Isus im reèe: kad vas je množina, idite u šumu, i ondje okrèite sebi u zemlji Ferezejskoj i Rafajskoj, ako vam je tijesna gora Jefremova.
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
A sinovi Josifovi rekoše: neæe nam biti dosta ova gora; a svi Hananeji koji žive u dolini imaju gvozdena kola; i oni koji su u Vet-Sanu i u selima njegovijem i oni koji su u dolini Jezraelskoj.
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
A Isus reèe domu Josifovu, Jefremu i Manasiji, govoreæi: velik si narod i silan si, neæeš imati jednoga dijela.
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
Nego gora neka bude tvoja; ako je šuma, isijeci je, pak æeš imati meðe njezine; jer æeš izagnati Hananeje, ako i imaju gvozdena kola, ako i jesu jaki.