< Yoswa 17 >

1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
Inilah tanah yang diberikan kepada suku Manasye, anak sulung Yusuf. Daerah Gilead dan Basan di sebelah timur sungai Yordan diberikan kepada Makir, anak sulung Manasye, ayah Gilead. Daerah itu diberikan kepada Makir karena dia seorang pahlawan perang.
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
Tanah di sebelah barat sungai Yordan diberikan kepada marga-marga lainnya dari suku Manasye, yaitu Abiezer, Helek, Asriel, Sikem, Hefer, dan Semida. Marga-marga ini adalah keturunan laki-laki dari Manasye, anak Yusuf.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
Akan tetapi, Zelafehad anak Hefer tidak mempunyai anak laki-laki, hanya anak-anak perempuan yang bernama Mahla, Noa, Hogla, Milka, dan Tirza. (Hefer adalah anak Gilead, cucu Makir, dan cicit Manasye.)
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
Perempuan-perempuan itu menemui imam Eleazar, Yosua, serta para pemimpin bangsa Israel dan berkata, “TUHAN menyuruh Musa untuk memberikan tanah warisan kepada kami di antara saudara-saudara kami.” Maka Yosua memberi mereka tanah warisan di antara saudara-saudara laki-laki ayah mereka, sesuai perintah TUHAN.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
Demikianlah suku Manasye mendapat sepuluh bidang tanah di sebelah barat sungai Yordan, karena keturunan perempuan Manasye itu juga menerima tanah warisan sama seperti keturunan laki-laki. Suku Manasye juga mendapat daerah Gilead dan Basan di sebelah timur sungai Yordan. Daerah Gilead sudah diberikan kepada keturunan Manasye lainnya.
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
Wilayah suku Manasye terbentang dari perbatasan wilayah suku Asyer sampai ke kota Mikmetat, yang terletak di sebelah timur kota Sikem, kemudian terus ke arah selatan sampai ke daerah penduduk En Tapuah.
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
Daerah Tapuah adalah milik suku Manasye, tetapi kota Tapuah di perbatasan wilayah Manasye adalah milik suku Efraim.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
Kemudian garis batas selatan itu turun ke sungai Kana dan menelusurinya ke arah barat sampai ke Laut Tengah. Wilayah suku Manasye sebagian besar terletak di sebelah utara sungai Kana. Di sebelah selatan sungai Kana, ada beberapa kota yang dimiliki suku Efraim meskipun masih terletak di dalam wilayah Manasye. Demikianlah wilayah suku Manasye berbatasan dengan wilayah suku Efraim di sebelah selatan, Laut Tengah di sebelah barat, wilayah suku Asyer di sebelah barat laut, dan wilayah suku Isakar di sebelah timur laut.
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
Di dalam wilayah suku Asyer dan suku Isakar, ada beberapa kota beserta desa-desa di sekitarnya yang diberikan kepada suku Manasye. Kota-kota itu adalah Bet Sean, Yibleam, Dor (di pinggir laut), En Dor, Taanak, dan Megido.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
Namun, suku Manasye tidak dapat mengusir orang Kanaan yang tinggal di kota-kota itu karena mereka bersikeras tinggal di daerah sana.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
Ketika orang Israel semakin kuat, mereka menjadikan orang-orang Kanaan itu pekerja paksa, tetapi tidak mengusir mereka sepenuhnya.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
Berkatalah keturunan Yusuf kepada Yosua, “TUHAN sudah memberkati kami sehingga jumlah kami sangat banyak. Kenapa engkau memberikan kepada kami hanya sebidang tanah saja sebagai warisan?”
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
Jawab Yosua kepada mereka, “Kalau jumlah kalian sangat banyak dan daerah pegunungan Efraim terlalu sempit bagi kalian, mendakilah ke hutan dan bukalah tanah di daerah orang Feris dan Refaim.”
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
Kata mereka lagi, “Pegunungan itu terlalu sempit bagi kami. Lagipula semua orang Kanaan yang tinggal di dataran rendah mempunyai kereta-kereta perang dari besi, baik yang tinggal di daerah Bet Sean dan desa-desa sekitarnya, maupun yang tinggal di lembah Yisreel.”
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
Lalu kata Yosua kepada keturunan Yusuf, yaitu suku Efraim dan Manasye, “Memang, kalian sangat banyak dan sangat kuat. Kalian akan mendapat lebih dari satu bagian.
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
Daerah pegunungan juga akan menjadi milik kalian. Karena daerah itu adalah hutan, bukalah hutan itu dan milikilah seluruhnya. Kalian juga akan mengusir orang Kanaan meskipun mereka kuat dan mempunyai kereta-kereta perang dari besi.”

< Yoswa 17 >