< Yoswa 14 >

1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
А оце те, що посіли Ізраїлеві сини в ханаанському краї, що дали їм на спа́док священик Елеаза́р, і Ісус, син Навинів, та го́лови батьків племен Ізраїлевих синів.
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
Жеребко́м приділили їхній спа́док, як наказав був Господь через Мойсея, дев'яти племе́нам і половині пле́мени.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Бо дав Мойсей насліддя двох племе́н, та половини пле́мени по той бік Йорда́ну, а Левитам спа́дку не дав серед них.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Бо Йо́сипових синів було двоє поколінь, Манасі́я та Єфре́м, а Левитам не дали спа́дку в краю́, а тільки міста на осе́лення та їхні пасови́ська для їхньої худоби та для їхнього маєтку.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Як наказав був Господь Мойсеєві, так зробили Ізраїлеві сини, та й поділили край.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
І підійшли Юдині сини до Ісуса в Ґілґалі, та й сказав до нього Кале́в, син Єфуннеїв, кеназзе́янин: „Ти знаєш те слово, що Господь говорив до Мойсея, Божого чоловіка, про мене та про тебе в Кадеш-Барнеа.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
Я був віку сорока́ літ, коли Мойсей, раб Господній, посилав мене з Кадеш-Барнеа ви́відати той край. І я доклав йому справу, як було в серці моїм.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
А мої браття, що ходили зо мною, знеси́лили були́ серце народу, а я обстава́в за Господом, Богом моїм.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
І присягнув Мойсей того дня, говорячи: „ Поправді кажу́, — той край, що нога твоя ходила в ньому, буде на спа́док тобі та синам твоїм аж навіки, бо ти обстава́в за Господом, Богом моїм.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
А тепер оце Господь позоставив мене при житті, як говорив. Оце сорок і п'ять літ відтоді́, як Господь говорив був це слово Мойсеєві, коли Ізраїль ходив у пустині. А тепер ось я віку восьмидесяти й п'яти літ.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
Сьогодні я ще сильний, як того дня, коли Мойсей посилав мене, — яка сила моя тоді, така сила моя й тепер, щоб воювати, і вихо́дити, і прихо́дити.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
А тепер дай же мені цей гористий край, про який Господь говорив того дня, бо ти чув того дня, що там ве́летні та великі укрі́плені міста́. Може Господь буде зо мною, і я повиганяю їх, як говорив був Господь“.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
І поблагословив його Ісус, і дав Калевові, синові Єфуннеєвому, Хевро́н за спа́док.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Тому став Хевро́н Калевові, синові Єфуннеєвому, кеназзе́янинові, за спадок, і так є аж до цього дня, за те, що він обстава́в за Господом, Богом Ізраїля.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
А ім'я́ Хеврону давніше було Кір'ят-Арба, що між ве́летнів був найбільший чоловік. А Край заспоко́ївся від війни.

< Yoswa 14 >