< Yoswa 14 >

1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
Lala ngamazwe abantwana bakoIsrayeli abawadla abe yilifa elizweni leKhanani, uEleyazare umpristi loJoshuwa indodana kaNuni lenhloko zaboyise bezizwe zabantwana bakoIsrayeli ababanika wona aba yilifa,
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
ngenkatho yelifa labo, njengokulaya kweNkosi ngesandla sikaMozisi, ngezizwe eziyisificamunwemunye lengxenye yesizwe.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Ngoba uMozisi wayesenike ilifa izizwe ezimbili lengxenye yesizwe ngaphetsheya kweJordani; kodwa kumaLevi kanikanga ilifa phakathi kwazo.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Ngoba abantwana bakoJosefa babeyizizwe ezimbili, uManase loEfrayimi. Njalo kabawanikanga amaLevi isabelo elizweni, ngaphandle kwemizi yokuhlala, lamadlelo ayo ezifuyo zabo lempahla zabo.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Njengokulaya kweNkosi kuMozisi, abantwana bakoIsrayeli benza njalo, balaba ilizwe.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
Khona abantwana bakoJuda basondela kuJoshuwa eGiligali; uKalebi indodana kaJefune umKenizi wasesithi kuye: Wena uyalazi ilizwi iNkosi eyalikhuluma kuMozisi umuntu kaNkulunkulu mayelana lawe lamayelana lami eKadeshi-Bhaneya.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
Ngangileminyaka engamatshumi amane lapho uMozisi inceku yeNkosi ingithuma ngisuka eKadeshi-Bhaneya ukuhlola ilizwe. Ngasengibuyisela kuye umbiko njengokusenhliziyweni yami.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
Kodwa abazalwane bami ababenyuke lami benza inhliziyo zabantu zancibilika; kodwa mina ngayilandela ngokupheleleyo iNkosi uNkulunkulu wami.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
UMozisi wasefunga mhlalokho esithi: Isibili umhlaba olunyathele kuwo unyawo lwakho uzakuba ngowakho ube yilifa, lebantwaneni bakho kuze kube nininini, ngoba uyilandele ngokupheleleyo iNkosi uNkulunkulu wami.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
Khathesi-ke khangela, iNkosi ingilondoloze ngiphila njengokutsho kwayo okwale iminyaka engamatshumi amane lanhlanu, kusukela esikhathini iNkosi eyakhuluma ngaso lelilizwi kuMozisi, uIsrayeli esahamba enkangala. Khathesi-ke khangela, lamuhla ngileminyaka engamatshumi ayisificaminwembili lanhlanu.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
Ngisaqinile lalamuhla njengasosukwini uMozisi angithuma ngalo. Njengamandla ami ngalesosikhathi, asenjalo amandla ami khathesi, awempi lawokuphuma lawokungena.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Ngakho-ke nginika lintaba iNkosi eyakhuluma ngayo ngalolosuku, ngoba wena wezwa mhlalokho ukuthi amaAnaki ayekhona lapho lemizi emikhulu ebiyelwe ngemithangala. Aluba iNkosi ilami, ngizawaxotsha elifeni, njengokutsho kweNkosi.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
UJoshuwa wasembusisa wanika uKalebi indodana kaJefune iHebroni ibe yilifa.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Ngalokho-ke iHebroni yaba ngekaKalebi indodana kaJefune umKenizi yaba yilifa kuze kube lamuhla, ngoba wayilandela ngokupheleleyo iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
Lebizo leHebroni kuqala laliyiKiriyathi-Arba, owayengumuntu omkhulu phakathi kwamaAnaki. Ilizwe laseliphumula empini.

< Yoswa 14 >