< Yoswa 14 >
1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
Voici ce qu’ont possédé les enfants d’Israël dans la terre de Chanaan que leur donnèrent Eléazar, le prêtre, et Josué, fils de Nun et les princes des familles de chaque tribu d’Israël,
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
Distribuant tout par le sort, comme avait ordonné le Seigneur par l’entremise de Moïse, aux neuf tribus et à la demi-tribu de Manassé.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Car aux deux autres tribus et à Y autre demi-tribu, Moïse avait donné au-delà du Jourdain une possession; à l’exception des Lévites qui ne reçurent aucune terre comme leurs frères;
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Mais en leur place succédèrent les fils de Joseph, divisés en deux tribus, Manassé et Ephraïm; et les Lévites ne reçurent point d’autre part dans la terre de Chanaan que des villes pour les habiter, et leurs faubourgs pour leurs bêtes de somme et leurs troupeaux.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Comme le Seigneur avait ordonné à Moïse, ainsi firent les enfants d’Israël, et ils partagèrent la terre.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
C’est pourquoi les enfants de Juda vinrent trouver Josué à Galgala; et Caleb, fils de Jéphoné, le Cénézéen, lui dit: Tu sais ce que le Seigneur a dit de moi et de toi à Moïse, homme de Dieu, à Cadesbarné.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
J’avais quarante ans, lorsque Moïse, serviteur du Seigneur, m’envoya de Cadesbarné, pour considérer la terre, et que je lui rapportai ce qui me paraissait vrai.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
Mais mes frères qui étaient montés avec moi, ont dissous le cœur du peuple; et néanmoins moi, je suivis le Seigneur mon Dieu.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
Et Moïse jura en ce jour-là, disant: La terre que ton pied a foulée sera ta possession et la possession de tes enfants pour toujours, parce que tu as suivi le Seigneur mon Dieu.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
Le Seigneur m’a donc accordé la vie, comme il a promis jusqu’au présent jour. Il y a quarante-cinq ans que le Seigneur dit cette parole à Moïse, quand Israël allait à travers le désert: aujourd’hui j’ai quatre vingt-cinq ans.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
Aussi fort que je l’étais au temps que je fus envoyé pour explorer le pays: la vigueur de ce temps-là a persévéré jusqu’aujourd’hui, tant pour combattre que pour marcher.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Donne-moi donc cette montagne, que ma promise le Seigneur, toi-même l’entendant, sur laquelle sont des Enacim, des villes grandes et fortifiées; pour voir si le Seigneur sera avec moi, et si je pourrai les exterminer comme il m’a promis.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
Et Josué le bénit, et il lui livra Hébron en possession.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Et depuis, Hébron a été à Caleb, fils de Jéphoné, le Cénézéen, jusqu’au présent jour, parce qu’il suivit le Seigneur Dieu d’Israël.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
Hébron était appelée auparavant du nom de Cariatharbé: Adam, le plus grand entre les Enacim, y est enterré: et le pays se reposa des combats.