< Yoswa 14 >

1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
And these are the countries which the children of Israel inherited in the land of Canaan, which Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun, and the heads of the fathers of the tribes of the children of Israel, distributed for inheritance to them.
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
By lot was their inheritance, as the LORD commanded by the hand of Moses, for the nine tribes, and for the half tribe.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
For Moses had given the inheritance of two tribes and an half tribe on the other side of Jordan: but to the Levites he gave no inheritance among them.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
For the children of Joseph were two tribes, Manasseh and Ephraim: therefore they gave no part to the Levites in the land, except cities to dwell in, with their common lands for their cattle and for their substance.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
As the LORD commanded Moses, so the children of Israel did, and they divided the land.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
Then the children of Judah came to Joshua in Gilgal: and Caleb the son of Jephunneh the Kenezite said to him, Thou knowest the thing that the LORD said to Moses the man of God concerning me and thee in Kadeshbarnea.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
Forty years old was I when Moses the servant of the LORD sent me from Kadeshbarnea to spy the land; and I brought him word again as it was in my heart.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
Nevertheless my brethren that went up with me made the heart of the people melt: but I wholly followed the LORD my God.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
And Moses swore on that day, saying, Surely the land on which thy feet have trodden shall be thy inheritance, and thy children’s for ever, because thou hast wholly followed the LORD my God.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
And now, behold, the LORD hath kept me alive, as he said, these forty and five years, even since the LORD spoke this word to Moses, while the children of Israel wandered in the wilderness: and now, lo, I am this day eighty and five years old.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
As yet I am as strong this day as I was in the day that Moses sent me: as my strength was then, even so is my strength now, for war, both to go out, and to come in.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Now therefore give me this mountain, of which the LORD spoke in that day; for thou heardest in that day how the Anakims were there, and that the cities were great and fortified: if the LORD will be with me, then I shall be able to drive them out, as the LORD said.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
And Joshua blessed him, and gave to Caleb the son of Jephunneh Hebron for an inheritance.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Hebron therefore became the inheritance of Caleb the son of Jephunneh the Kenezite to this day, because that he wholly followed the LORD God of Israel.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
And the name of Hebron before was Kirjatharba; which Arba was a great man among the Anakims. And the land had rest from war.

< Yoswa 14 >