< Yoswa 14 >
1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
Toto pak jest, což dědičně obdrželi synové Izraelští v zemi Kanán, což uvedli jim právem dědičným k vládařství Eleazar kněz, a Jozue, syn Nun, a přední z otců, v pokolení synů Izraelských,
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
Losem dělíce dědictví jejich, jakož přikázal Hospodin skrze Mojžíše, aby dal devateru pokolení a polovici pokolení.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Nebo byl dal Mojžíš dědictví půltřetímu pokolení před Jordánem, Levítům pak nedal dědictví u prostřed nich.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Nebo synů Jozefových bylo dvoje pokolení, Manassesovo a Efraimovo; a nedali dílu Levítům v zemi, kromě měst k bydlení, a podměstí jejich pro dobytek a stáda jejich.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Jakož přikázal Hospodin Mojžíšovi, tak učinili synové Izraelští, a rozdělili zemi.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
Přistoupili pak synové Juda k Jozue v Galgala, i promluvil k němu Kálef, syn Jefonův, Cenezejský: Ty víš, co jest mluvil Hospodin k Mojžíšovi, muži Božímu, z příčiny mé a tvé v Kádesbarne.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
Ve čtyřidceti letech byl jsem, když mne poslal Mojžíš, služebník Hospodinův, z Kádesbarne k spatření země, a oznámil jsem jemu tu věc, jakž bylo v srdci mém.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
Ale bratří moji, kteříž šli se mnou, zkormoutili srdce lidu, já pak cele kráčel jsem za Hospodinem Bohem svým.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
I přisáhl Mojžíš toho dne, řka: Jistě že země, po kteréž jsi chodil nohama svýma, bude v dědictví tobě i synům tvým až na věky, proto že jsi cele následoval Hospodina Boha mého.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
A nyní, aj, propůjčil mi Hospodin života, jakož zaslíbil. Již čtyřidceti a pět let jest od toho času, jakž toto mluvil Hospodin k Mojžíšovi, a jakž chodil Izrael po poušti, a aj, již dnes jsem v osmdesáti pěti letech,
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
A ještě nyní jsem při síle jako tehdáž, když poslal mne Mojžíš. Jaká byla síla má tehdáž, taková i nyní síla má jest k boji, a k vycházení i k vcházení.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Protož nyní dej mi horu tuto, o níž mluvil Hospodin onoho dne, nebo ty slyšel jsi toho dne, že Enakim jsou tam, a města veliká a pevně hrazená. Bude-li Hospodin se mnou, vyhladím je, jakož mluvil Hospodin.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
I požehnal mu Jozue, a dal Hebron Kálefovi, synu Jefone, v dědictví.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Protož dostal se Hebron Kálefovi, synu Jefona Cenezejského, v dědictví až do tohoto dne, proto že cele kráčel za Hospodinem Bohem Izraelským.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
Sloulo pak Hebron prvé město Arbe, kterýžto Arbe byl člověk veliký mezi Enakim. I odpočinula země od bojů.