< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
А Ісус поста́рівся й увійшов у дні. І сказав Господь до нього: „Ти поста́рівся та ввійшов у дні, а кра́ю позостається ще дуже багато, щоб посісти його.
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
Оце позосталий край: усі округи филисти́мські, і ввесь Ґешурей,
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
від Шіхору, що навпроти Єгипту, і аж до границі Екрону на пі́вніч, що до ханаанеянина залічений, п'ять филистимських князів: аззатський, ашдодський, ашкелонський, ґаттійський і екронський, та аввеї.
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
Від пі́вдня вся ханаанська земля та Меара, що сидонська, аж до Афеки, аж до аморейської границі,
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
і ґівлейська земля, і ввесь Ливан на схід сонця від Баал-Ґаду під горою Гермон аж до входу до Хамату.
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
Усіх ме́шканців гір від Ливану аж до Місрефот-Маїму, усіх сидо́нян, — Я повиганяю їх перед Ізраїлевими синами. Тільки поділи́ її жеребком на спа́док Ізра́їлеві, як Я наказав був тобі.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
А тепер поділи цей край на спа́док дев'яти́ племе́нам та половині пле́мени Манасі́їному“.
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
Ра́зом із ним Руви́мові та Ґа́дові взяли свій спа́док що дав їм Мойсей по той бік Йорда́ну на схід, як дав їм Мойсей, раб Господній,
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
від Ароеру, що на березі арнонського потоку, і місто, що серед тієї долини, і вся медевська рівнина аж до Дівону,
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
і всі міста Сигона, царя аморейського, що царював у Хешбоні, аж до границі Аммонових синів,
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
і Ґілеад, і границя ґешурейська та маахейська, і вся гора Гермон, і ввесь Башан аж до Салхи,
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
усе царство Оґа в Башані, що царював в Аштароті та в Едреї, — він позостався з останку рефаїв, а Мойсей повбивав їх та повиганяв їх.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
І не вигнали Ізраїлеві сини ґешуре́янина, і маахате́янина, — і сидів Ґешур та Маахат серед Ізраїля, і так є аж до цього дня.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Тільки Левієвому племені не дав він спа́дку, — огняні́ жертви Господа, Бога Ізраїля, то спа́док його, „як Я говорив був йому.“
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
І дав Мойсей племені Рувимових синів спа́док за їхніми ро́дами.
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
І була їм границя від Ароеру, що на березі арнонського потоку, і місто, що серед тієї долини, і вся рівни́на при Медеві,
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
Хешбон і всі міста його, що на рівнині, Дівон, і Бамот-Баал, і Бет-Баал-Меон,
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
і Ягца, і Кедемот, і Мефаат,
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
і Кір'ятаїм, і Сівма, і Церет-Гашшахар на горі Емеку,
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
і Бет-Пеор, і узбіччя Пісґі, і Бет-Гаєшімот,
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
і всі міста рівни́ни, і все царство Сигона, царя аморейського, що царював у Хешбоні, що Мойсей убив його та мідіянських начальників: Евія, і Рекема, і Цура, і Хура, і Реву, сигонових князів, мешканців того кра́ю.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
А Валаама, Беорового сина, чарівника́, Ізраїлеві сини забили мечем серед інших, яких вони побили.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
І була́ границя Рувимових синів: Йорда́н і границя. Це спа́док Рувимових синів за їхніми родами, їхні міста та їхні оселі.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
І дав Мойсей Ґадовому племені, синам Ґада за їхніми родами,
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
і була їм границя: Язер, і всі ґілеадські міста, і половина краю аммонових синів аж до Ароеру, що навпроти Рабби,
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
А з Хешбону аж до Рамат Гамміцпі й Бетоніму, а від Маханаїму аж до границі Девіру,
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
і в долині Бет-Гараму, і Бет-Німра, і Суккот, і Цафон, останок царства Сигона, царя хешбонського, Йорда́н і границя аж до кінця озера Кіннерет по тім боці Йорда́ну на схід.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
Це спа́док Ґадових синів за їхніми ро́дами, міста та їхні оселі.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
І дав Мойсей половині племени Манасіїного, і воно було половині племени Манасіїних синів за їхніми ро́дами.
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
І була їхня границя від Манахаїму, увесь Башан, усе царство Оґа, царя башанського, і всі села Яіру, що в Башані, шістдеся́т міст.
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
А половина Ґілеаду, і Аштарот, і Едрея, міста Оґового царства в Башані, — синам Махіра, Манасіїного сина, половині синів Махіра за їхніми ро́дами.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
Оце те, що Мойсей дав на спа́док в моавських степа́х по тім боці Йорда́ну на схід.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.
А Левієвому племені Мойсей не дав спа́дку, — Господь, Бог Ізраїлів, Він їхній спа́док, як говорив їм.

< Yoswa 13 >