< Yoswa 11 >
1 Yabini, mfumu ya Hazori, inamva zimene zinachitikazi. Tsono inatumiza uthenga kwa Yobabu mfumu ya Madoni, ndiponso kwa mafumu a ku Simironi ndi Akisafu.
Kwathi uJabhini inkosi yeHazori isizwa lokhu yathumela ilizwi kuJobhabhi inkosi yeMadoni lasemakhosini eShimroni le-Akhishafi,
2 Inatumizanso uthenga kwa mafumu a kumpoto, kumapiri, ndi mʼchigwa cha Yorodani kummwera kwa nyanja ya Kinereti, ndiponso kumadzulo mʼmbali mwa nyanja pafupi ndi Dori.
lasemakhosini enyakatho ayesezintabeni ze-Arabha eningizimu yeKhinerethi emawatheni amaqaqa entshonalanga kanye laseNafothi Dori entshonalanga;
3 Inatumizanso uthenga kwa Akanaani amene ankakhala kummawa ndi kumadzulo kwa Yorodani. Uthenga unapitanso kwa Aamori, Ahiti, Aperezi ndi Ayebusi amene amakhala mʼdziko la ku mapiri ndiponso kwa Ahivi amene ankakhala mʼmunsi mwa phiri la Herimoni ku chigwa cha Mizipa.
lakumaKhenani empumalanga lentshonalanga; lakuma-Amori, amaHithi, amaPherizi lamaJebusi elizweni elilamaqaqa; kanye lakumaHivi ngaphansi kweHemoni esabelweni seMizipha.
4 Mafumuwo anabwera pamodzi ndi ankhondo awo onse. Gulu la ankhondo linali lalikulu ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Analinso ndi akavalo ndi magaleta ambiri.
Baphuma lamabutho abo wonke lenani elikhulu lamabhiza lezinqola, ibutho elikhulu, ubunengi lingangetshebetshebe okhunjini lolwandle.
5 Mafumu onsewa anasonkhana pamodzi ndipo anamanga misasa yawo ku mtsinje wa Meromu, kuti amenyane ndi Israeli.
Wonke amakhosi la abambana asesakha izihonqo ndawonye eManzini aseMeromi, ukulwa labako-Israyeli.
6 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope chifukwa mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzawapereka kuti muwaphe. Akavalo awo muwadule matsinde ndipo magaleta awo muwatenthe ndi moto.”
UThixo wathi kuJoshuwa, “Ungabesabi, ngoba ngalesisikhathi kusasa ngizabanikela bonke kwabako-Israyeli sebefile. Uzaquma imisipha yamabhiza abo njalo utshise izihonqo zabo.”
7 Kotero Yoswa pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo anafika kwa adani awo aja ku mtsinje wa Meromu modzidzimutsa ndi kuwathira nkhondo.
Ngakho uJoshuwa lebutho lakhe lonke bahlangana labo mathupha eManzini eMeromi wasebahlasela,
8 Yehova anawapereka mʼmanja mwa Israeli mwakuti anawagonjetseratu ndi kuwapirikitsa njira yonse mpaka ku Sidoni Wamkulu ndi ku Misirefoti Maimu, ndiponso kummawa ku chigwa cha Mizipa. Onse anaphedwa popanda wopulumuka.
uThixo wabanikela esandleni sika-Israyeli. Babanqoba, baxotshana labo baze babafikisa eSidoni Enkulu kusiya eMisirefothi-Mayimi, leSigodini seMizipha empumalanga kwaze kwasala kungelamuntu ophilayo.
9 Yoswa anawachita zimene Yehova analamula. Iye anadula matsinde a akavalo awo ndi kutentha magaleta awo.
UJoshuwa wenza kibo lokho ayekulaywe nguThixo: Waquma imisipha yamabhiza abo njalo watshisa izinqola zabo.
10 Pambuyo pake Yoswa anabwera nalanda mzinda wa Hazori ndi kupha mfumu yake. (Nthawi imeneyo mzinda wa Hazori unali wopambana mizinda ina yonse).
Ngalesosikhathi uJoshuwa waphenduka wabuyela emuva wathumba iHazori wasehlasela inkosi yakuleyo ndawo ngenkemba. (IHazori yayiyisigodlo sayo yonke imibuso leyo.)
11 Anapha aliyense wa mu mzindamo popanda wotsala wamoyo, ndipo mzinda wa Hazori anawutentha ndi moto.
Wonke umuntu owayephakathi kwayo wabhujiswa ngenkemba. Bababhubhisa baphela, abaze batshiya lutho oluphefumulayo, watshisa iHazori ngokwayo.
12 Yoswa analanda mizinda yonse ndi mafumu ake. Anthu onse anaphedwa ndi lupanga monga momwe analamulira Mose, mtumiki wa Yehova.
UJoshuwa wathumba wonke amadolobho esikhosini lamakhosi awo wawahlasela ngenkemba. Wawabhubhisa wonke, njengokulaya kukaMosi inceku kaThixo.
13 Israeli sanatenthe mizinda yomangidwa pa zitunda, kupatula mzinda wa Hazori, umene Yoswa anawutentha.
Kukanti-ke u-Israyeli kazange atshise loba yiwaphi amadolobho ayakhelwe emadundulwini ngaphandle kweHazori, eyatshiswa nguJoshuwa.
14 Aisraeli anatenga zinthu zonse za mʼmizindayi pamodzi ndi ziweto kuti zikhale zawo, koma anapha anthu onse ndi lupanga osasiyako ndi mmodzi yemwe wamoyo.
Abako-Israyeli bathatha zaba ngezabo zonke impahla ababezithumbile okwakugoqela izifuyo zamadolobho la bahamba lakho kodwa bonke abantu bababhubhisa ngenkemba baphela du, bengatshiyi lutho oluphefumulayo.
15 Monga momwe Yehova analamulira mtumiki wake Mose, nayenso Mose analamulira Yoswa ndipo Yoswa anachita chilichonse chimene Yehova analamulira Mose.
Njengoba uThixo walaya inceku yakhe uMosi, uMosi laye walaya uJoshuwa, uJoshuwa wakwenza lokho: katshiyanga lutho lungenziwanga ezintweni zonke uThixo owazilaya uMosi.
16 Kotero Yoswa analanda dziko lonse: dziko la ku mapiri, dera lonse la Negevi, chigawo chonse cha Goseni, ndi chigwa chake chonse, chigwa cha Yorodani, dziko lonse la lamapiri la Israeli pamodzi ndi chigwa chake chomwe.
Ngakho uJoshuwa wathatha ilizwe lonke: ilizwe lamaqaqa, yonke iNegebi, isabelo sonke seGosheni, amawatha asentshonalanga, i-Arabha, lezintaba zako-Israyeli lamawatha azo,
17 Dziko lolandidwalo linayambira ku phiri la Halaki limene linali ku Seiri mpaka ku Baala-Gadi mʼchigwa cha Lebanoni, kumunsi kwa phiri la Herimoni. Yoswa anagwira ndi kupha mafumu a dziko lonselo
kusukela entabeni yeHalakhi, ephakama ngokuya eSeyiri, kusiya eBhali-Gadi esiGodini seLebhanoni ngaphansi kwentaba iHemoni. Wathumba wonke amakhosi awo, wawehlula, wawabulala.
18 atachita nawo nkhondo kwa nthawi yayitali.
UJoshuwa walwa impi lawo wonke amakhosi okwesikhathi eside.
19 Palibe ngakhale ndi mfumu imodzi yomwe imene inachita mgwirizano wa mtendere ndi Aisraeli kupatula Ahivi okhala ku Gibiyoni. Koma mizinda ina yonse anachita kuyigonjetsa pa nkhondo.
Ngaphandle kwamaHivi ayehlala eGibhiyoni, kalikho idolobho loba elilodwa elenza isivumelwano sokuthula labako-Israyeli, kwabawathumba empini.
20 Yehova anali atawumitsa mitima yawo kuti alimbane ndi Aisraeli kuti aphedwe popanda kuchitiridwa chifundo. Izi ndi zimene Yehova analamula Mose kuti zichitidwe.
Ngoba kwakunguThixo owenza inhliziyo zawo zaba lukhuni zafuna ukulwa impi lo-Israyeli, ukwenzela ukuthi enelise ukubachitha baphele, ebabhubhisa okungelazwelo, njengokulaywa kukaMosi nguThixo.
21 Pa nthawi imeneyi Yoswa anapita kukawononga Aanaki okhala mʼdziko lija la ku mapiri ku Hebroni, Debri, Anabu komanso madera onse a ku mapiri a Yuda ndi Israeli. Yoswa anawawononga onse pamodzi ndi mizinda yawo.
Ngalesosikhathi uJoshuwa waphuma wawabhubhisa ama-Anakhi elizweni lamaqaqa: kusukela eHebhroni, eDebhiri le-Anabhi, kusukela elizweni lonke lamaqaqa akoJuda. UJoshuwa wabhubhisa wababhuqa bona kanye lamadolobho abo.
22 Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsalako mʼdziko lonse la Israeli; komabe ku Gaza, ku Gati ndi Asidodi kokha ndi kumene anatsalako pangʼono.
Akula ma-Anakhi asala esabelweni sabako-Israyeli; ngaphandle kweGaza iGathi le-Ashidodi lapho okwasila abanye bakhona.
23 Choncho Yoswa anagonjetsa dziko lonse monga momwe Yehova analamulira Mose. Tsono Yoswa analipereka kwa Aisraeli kuti likhale lawo, fuko lililonse gawo lake. Anthu onse anapumula, osamenyanso nkhondo.
Ngakho uJoshuwa wathumba ilizwe lonke njengoba uThixo walaya uMosi, waselinika abako-Israyeli njengelifa kusiya ngokwahlukaniswa kwezizwana zabo. Ngakho-ke ilizwe laphumula ekulweni izimpi.