< Yoswa 10 >

1 Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
Et lorsque Adoni-Tsédec, Roi de Jérusalem, apprit que Josué avait pris et dévoué Aï et traité Aï et son Roi, comme il avait traité Jéricho et son Roi, et que les habitants de Gabaon avaient fait leur paix avec Israël et restaient dans son sein,
2 Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
alors il eut une crainte extrême. Car Gabaon était une ville grande comme l'une des villes royales et plus considérable qu'Aï, et tous ses hommes étaient des guerriers.
3 Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
Alors Adoni-Tsédec, Roi de Jérusalem, députa vers Hoham, Roi de Hébron, et vers Piream, Roi de Jarmuth, et vers Japhia, Roi de Lachis, et vers Débir, Roi de Eglon, pour leur dire:
4 Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
Venez me joindre pour m'aider à réduire Gabaon, car elle a fait sa paix avec Josué et les enfants d'Israël.
5 Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
Et cinq Rois des Amoréens, le Roi de Jérusalem, le Roi de Hébron, le Roi de Jarmuth, le Roi de Lachis, le Roi de Eglon opérèrent leur jonction et s'avancèrent eux et toutes leurs armées et vinrent camper devant Gabaon, et l'assiégèrent.
6 Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
Alors les gens de Gabaon députèrent vers Josué, à son camp près de Guilgal, pour lui dire: Ne retire pas ta main à tes serviteurs, avance-toi vers nous en hâte, apporte-nous aide et secours car tous les Rois des Amoréens habitant la montagne se sont ligués contre nous.
7 Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
Là-dessus Josué se mit en marche de Guilgal, lui et avec lui tous les gens de guerre, et tous les braves guerriers.
8 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
Et l'Éternel dit à Josué: N'aie pas peur d'eux, car je les ai livrés entre tes mains, pas un de leurs hommes ne te tiendra tête.
9 Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
Et Josué fondit sur eux tout à coup. Or il employa toute la nuit à venir de Guilgal.
10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
Et l'Éternel jeta la confusion parmi eux devant Israël, et il leur fit essuyer une grande défaite près de Gabaon, et il les poursuivit sur la route de la montée de Beth-Horon, et les mena battant jusqu'à Azéca et à Makkéda.
11 Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
Et comme ils fuyaient devant Israël, ils étaient à la descente de Beth-Horon; là l'Éternel fit tomber sur eux du ciel de grosses pierres jusqu'à Azéca; et ils périrent; il y eut un plus grand nombre de ceux que tuèrent les pierres de grêle, que de ceux que les enfants d'Israël égorgèrent avec l'épée.
12 Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
C'est alors que Josué parla à l'Éternel, dans la journée où l'Éternel livra les Amoréens aux enfants d'Israël, et il dit en présence d'Israël: Soleil, attends à Gabaon, et toi, Lune, au val d'Ajalon.
13 Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
Et le soleil attendit et la lune resta, jusqu'à ce qu'Israël eût puni ses ennemis. N'est-ce pas ce qui est écrit dans le Livre du Droiturier? Et le soleil resta dans le milieu du ciel et ne se hâta pas vers son couchant, presque un jour entier.
14 Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
Et avant et après il n'y eut pas une journée telle que l'Éternel écoutât la voix d'un homme, car l'Éternel combattait pour Israël.
15 Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
Et Josué, et tout Israël avec lui, retourna au camp à Guilgal.
16 Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
Ces cinq Rois étaient donc en fuite, et ils se cachèrent dans la caverne à Makkéda.
17 Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
Alors Josué reçut cette information: Les cinq Rois se trouvent cachés dans la caverne à Makkéda.
18 Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
Et Josué dit: Roulez de grosses pierres à l'ouverture de la caverne, et postez-y des hommes pour les garder.
19 Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
Quant à vous, ne vous arrêtez pas, poursuivez vos ennemis, et attaquez-les en queue, ne les laissez pas regagner leurs villes; car l'Éternel, votre Dieu, les a livrés entre vos mains.
20 Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
Et lorsque Josué et les enfants d'Israël eurent consommé leur défaite qui fut très grande, jusqu'à extermination (des réchappés échappèrent pourtant et gagnèrent les places fortes)
21 Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
et lorsque tout le peuple fut revenu sain et sauf au camp auprès de Josué à Makkéda sans que personne remuât la langue contre les enfants d'Israël,
22 Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
alors Josué dit: Ouvrez l'entrée de la caverne et tirez de la caverne pour me les amener ces cinq Rois-là.
23 Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
Et on le fit, et on lui amena ces cinq Rois-là qui furent tirés de la caverne, le Roi de Jérusalem, le Roi de Hébron, le Roi de Jarmuth, le Roi de Lachis, le Roi de Eglon.
24 Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
Et ces Rois amenés devant Josué, Josué convoqua tous les hommes d'Israël, et dit aux chefs des gens de guerre qui avaient marché avec lui: Approchez! posez vos pieds sur les cous de ces Rois. Et ils s'approchèrent et posèrent leurs pieds sur leurs cous.
25 Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
Alors Josué leur dit: Soyez sans crainte et sans peur, ayez courage et résolution, car ainsi l'Éternel traitera tous vos ennemis que vous avez à combattre.
26 Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
Après quoi Josué les fit égorger et tuer, puis pendre à cinq arbres; et ils restèrent pendus aux arbres jusqu'au soir.
27 Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
Et au moment du coucher du soleil, sur l'ordre de Josué, on les détacha des arbres, et on les jeta dans la caverne où ils s'étaient cachés, et l'on plaça de grosses pierres à l'ouverture de la caverne, et elles y sont aujourd'hui même.
28 Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Et dans ce même jour Josué ayant pris Makkéda la mit à sac avec le tranchant de l'épée, et il dévoua son Roi, ainsi que toutes les personnes qui s'y trouvaient, et ne laissa survivre aucun réchappé; et il traita le Roi de Makkéda comme il avait traité le Roi de Jéricho.
29 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
Alors Josué et tout Israël avec lui, de Makkéda se porta sur Libna, et il attaqua Libna.
30 Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Et l'Éternel la livra aussi entre les mains d'Israël, ainsi que son Roi, et la frappa avec le tranchant de l'épée, ainsi que toutes les personnes qui s'y trouvaient, et il n'y laissa survivre aucun réchappé, et il traita son Roi comme il avait traité le Roi de Jéricho.
31 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Puis Josué, et tout Israël avec lui, de Libna marcha sur Lachis devant laquelle il campa; et il l'attaqua.
32 Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
Et l'Éternel livra Lachis entre les mains d'Israël qui la prit dès le second jour et la mit à sac avec le tranchant de l'épée ainsi que toutes les personnes qui y étaient, tout comme il avait traité Libna.
33 Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
Alors Horam, Roi de Gézer, s'avança pour secourir Lachis, et Josué le défit lui et son peuple, à ne pas lui laisser un réchappé.
34 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Ensuite Josué, et tout Israël avec lui, de Lachis se porta sur Eglon devant laquelle ils campèrent et qu'ils attaquèrent.
35 Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
Et ils la prirent le jour même, et ils sévirent sur elle avec le tranchant de l'épée, ainsi que sur toutes les personnes qui s'y trouvaient, et le jour même il la dévoua tout comme il avait traité Lachis.
36 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
Ensuite Josué, et tout Israël avec lui, de Eglon se porta sur Hébron qu'ils attaquèrent.
37 Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
Et l'ayant prise ils sévirent avec le tranchant de l'épée sur elle, et sur son Roi, et sur toutes ses villes et sur toutes les personnes qui y étaient; il ne laissa survivre aucun réchappé ainsi qu'il avait fait à Eglon, et il la dévoua avec toutes les personnes qui y étaient.
38 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
Alors Josué, et tout Israël avec lui, se tourna contre Debir, et il l'attaqua.
39 Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
Et il la prit ainsi que son Roi et toutes ses villes, et ils sévirent sur elles avec le tranchant de l'épée, et ils dévouèrent toutes les personnes qui y étaient sans laisser survivre un réchappé; comme il avait traité Hébron, ainsi traita-t-il Debir, et son Roi, de la même manière qu'il avait traité Libna et son Roi.
40 Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
Ainsi Josué réduisit tout le pays, la Montagne, le Midi, le Pays-bas et les versants, et tous leurs Rois; il ne laissa survivre aucun réchappé, et il dévoua tout ce qui respirait, selon l'ordre de l'Éternel, Dieu d'Israël.
41 Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
Et Josué les réduisit de Cadès-Barnéa à Gaza, et tout le district de Gosen jusques à Gabaon.
42 Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
Et dans une seule campagne Josué prit tous ces rois et leur pays, car l'Éternel, Dieu d'Israël, combattait pour Israël.
43 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.
Alors Josué et tout Israël avec lui, revint au camp à Guilgal.

< Yoswa 10 >