< Yoswa 10 >

1 Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
Dès qu'Adoni-Tsédek, roi de Jérusalem, apprit que Josué s'était emparé d'Aï, et qu'il l'avait vouée à l'interdit, qu'il avait traité Aï et son roi, comme il avait traité Jérico et son roi, et que les habitants de Gabaon avaient fait la paix avec les Israélites, et qu'ils étaient parmi eux,
2 Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
Il craignit fort, parce que Gabaon était une grande ville, comme l'une des villes royales; car elle était plus grande qu'Aï, et tous ses hommes étaient vaillants.
3 Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
Adoni-Tsédek, roi de Jérusalem, envoya donc vers Hoham roi de Hébron, vers Piram roi de Jarmuth, vers Japhia roi de Lakis, et vers Débir roi d'Églon, pour leur dire:
4 Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
Montez vers moi, et portez-moi secours, et frappons Gabaon; car elle a fait la paix avec Josué et avec les enfants d'Israël.
5 Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
Les cinq rois des Amoréens, le roi de Jérusalem, le roi de Hébron, le roi de Jarmuth, le roi de Lakis et le roi d'Églon, s'assemblèrent donc et montèrent, eux et toutes leurs armées, et campèrent contre Gabaon, et lui firent la guerre.
6 Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
Et les gens de Gabaon envoyèrent dire à Josué, au camp de Guilgal: N'abandonne point tes serviteurs; monte vers nous promptement; délivre-nous, et donne-nous du secours; car tous les rois des Amoréens, qui habitent la montagne, se sont assemblés contre nous.
7 Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
Josué monta donc de Guilgal, et avec lui tout le peuple propre à la guerre, et tous les hommes forts et vaillants.
8 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
Et l'Éternel dit à Josué: Ne les crains point, car je les ai livrés entre tes mains, et aucun d'eux ne subsistera devant toi.
9 Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
Josué vint donc subitement à eux, et il monta toute la nuit de Guilgal.
10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
Et l'Éternel les mit en déroute devant Israël, qui leur fit éprouver une grande défaite près de Gabaon, et les poursuivit par le chemin de la montée de Beth-Horon, et les battit jusqu'à Azéka, et à Makkéda.
11 Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
Et comme ils fuyaient devant Israël, et qu'ils étaient à la descente de Beth-Horon, l'Éternel jeta du ciel sur eux de grosses pierres, jusqu'à Azéka, et ils périrent. Ceux qui moururent par les pierres de grêle furent plus nombreux que ceux que les enfants d'Israël tuèrent avec l'épée.
12 Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
Alors Josué parla à l'Éternel, le jour où l'Éternel livra l'Amoréen aux enfants d'Israël, et il dit, en présence d'Israël: Soleil, arrête-toi sur Gabaon, et toi lune, sur la vallée d'Ajalon!
13 Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
Et le soleil s'arrêta, et la lune aussi, jusqu'à ce que la nation se fût vengée de ses ennemis. Cela n'est-il pas écrit dans le livre du Juste? Le soleil s'arrêta au milieu des cieux, et ne se hâta point de se coucher, environ un jour entier.
14 Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
Il n'y a point eu de jour comme celui-là, ni avant ni après, où l'Éternel ait exaucé la voix d'un homme; car l'Éternel combattait pour Israël.
15 Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
Et Josué, et tout Israël avec lui, retourna au camp, à Guilgal.
16 Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
Or les cinq rois s'enfuirent, et se cachèrent dans une caverne, à Makkéda.
17 Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
Et on le rapporta à Josué en disant: On a trouvé les cinq rois, cachés dans une caverne, à Makkéda.
18 Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
Alors Josué dit: Roulez de grandes pierres à l'entrée de la caverne, et mettez près d'elle des hommes pour les garder.
19 Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
Mais vous, ne vous arrêtez pas, poursuivez vos ennemis, et attaquez-les par derrière; ne les laissez point entrer dans leurs villes; car l'Éternel votre Dieu les a livrés entre vos mains.
20 Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
Et lorsque Josué et les enfants d'Israël eurent achevé d'en faire une très grande défaite, jusqu'à les détruire entièrement, et que ceux d'entre eux qui échappèrent, se furent retirés dans les villes fortifiées,
21 Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
Tout le peuple retourna en paix au camp, vers Josué, à Makkéda; et personne ne remua la langue contre les enfants d'Israël.
22 Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
Alors Josué dit: Ouvrez l'entrée de la caverne, faites-en sortir ces cinq rois, et amenez-les-moi.
23 Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
Et ils firent ainsi. Ils firent sortir de la caverne ces cinq rois, le roi de Jérusalem, le roi d'Hébron, le roi de Jarmuth, le roi de Lakis et le roi d'Églon, et les lui amenèrent.
24 Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
Et lorsqu'ils eurent amené ces rois à Josué, Josué appela tous les hommes d'Israël, et dit aux chefs des gens de guerre qui étaient allés avec lui: Approchez-vous, mettez vos pieds sur le cou de ces rois. Et ils s'approchèrent, et mirent les pieds sur leurs cous.
25 Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
Puis Josué leur dit: Ne craignez point et ne soyez point effrayés; fortifiez-vous et prenez courage; car c'est ainsi que l'Éternel fera à tous vos ennemis, contre lesquels vous combattrez.
26 Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
Après cela Josué les frappa et les fit mourir, et les fit pendre à cinq arbres, et ils demeurèrent pendus aux arbres jusqu'au soir.
27 Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
Et comme le soleil allait se coucher, Josué commanda qu'on les descendît des arbres; on les jeta dans la caverne où ils s'étaient cachés, et on mit à l'entrée de la caverne de grandes pierres, qui y sont demeurées jusqu'à ce jour même.
28 Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Josué prit aussi Makkéda, en ce même jour, et la fit passer au fil de l'épée; il voua à l'interdit son roi, ses habitants, et toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune; et il fit au roi de Makkéda comme il avait fait au roi de Jérico.
29 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
Puis Josué, et tout Israël avec lui, passa de Makkéda à Libna, et assiégea Libna;
30 Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
Et l'Éternel la livra aussi entre les mains d'Israël, avec son roi; et il la fit passer au fil de l'épée, ainsi que toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune; et il fit à son roi comme il avait fait au roi de Jérico.
31 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Ensuite Josué, et tout Israël avec lui, passa de Libna à Lakis, et campa contre elle et lui fit la guerre;
32 Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
Et l'Éternel livra Lakis entre les mains d'Israël, qui la prit le deuxième jour et la fit passer au fil de l'épée, avec toutes les personnes qui y étaient, tout comme il avait fait à Libna.
33 Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
Alors Horam, roi de Guézer, monta pour secourir Lakis, et Josué le frappa, lui et son peuple, de manière à ne pas laisser échapper un homme.
34 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Puis Josué, et tout Israël avec lui, passa de Lakis à Églon; ils campèrent contre elle et lui firent la guerre;
35 Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
Et ils la prirent le même jour, et la firent passer au fil de l'épée; et Josué voua à l'interdit en ce jour-là toutes les personnes qui y étaient, tout comme il avait fait à Lakis.
36 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
Ensuite Josué, et tout Israël avec lui, monta d'Églon à Hébron, et ils lui firent la guerre;
37 Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
Ils la prirent et la firent passer au fil de l'épée, avec son roi et toutes ses villes, et toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune, tout comme il avait fait à Églon; il la voua à l'interdit, avec toutes les personnes qui y étaient.
38 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
Puis Josué, et tout Israël avec lui, rebroussa chemin vers Débir, et lui fit la guerre;
39 Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
Il la prit avec son roi et toutes ses villes; et ils les firent passer au fil de l'épée, et vouèrent à l'interdit toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune. Il fit à Débir et à son roi comme il avait fait à Hébron, et comme il avait fait à Libna et à son roi.
40 Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
Josué battit donc tout le pays, la montagne, le Midi, la plaine et les coteaux, et tous leurs rois; il ne laissa échapper personne; et il voua à l'interdit tout ce qui respirait, comme l'Éternel, le Dieu d'Israël, l'avait commandé.
41 Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
Josué les battit ainsi depuis Kadès-Barnéa jusqu'à Gaza, et tout le pays de Gossen, jusqu'à Gabaon.
42 Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
Et Josué prit, en une seule fois, tous ces rois et leur pays, parce que l'Éternel, le Dieu d'Israël, combattait pour Israël.
43 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.
Puis Josué, et tout Israël avec lui, retourna au camp, à Guilgal.

< Yoswa 10 >