< Yoswa 10 >

1 Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
And whanne Adonysedech, kyng of Jerusalem, hadde herde these thingis, that is, that Josue hadde take Hai, and hadde destried it; for as Josue hadde do to Jerico and to the kyng therof, so he dide to Hay, and to the kyng therof; and that Gabaonytis hadden fled to Israel, and weren boundun in pees with hem,
2 Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
Adonysedech dredde greetli; for Gabaon was a greet citee, and oon of the kyngis citees, and grettere than the citee of Hai, and alle the fiyteris therof weren most stronge.
3 Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
Therfor Adonysedech, kyng of Jerusalem, sente to Ocham, kyng of Ebron, and to Pharam, kyng of Herymoth, and to Japhie, kyng of Lachis, and to Dabir, kyng of Eglon, and seide,
4 Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
Stie ye to me, and helpe ye, that we fiyte ayens Gabaon, for it was yoldun to Josue, and to the sones of Israel.
5 Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
Therfor fyue kyngis of Ammorreis, the kyng of Jerusalem, the kyng of Ebron, the kyng of Herymoth, the kyng of Lachis, the kyng of Eglon, weren gaderid, and stieden togidere with her oostis; and settiden tentis ayens Gabaon, and fouyten ayens it.
6 Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
Sotheli the dwelleris of the citee of Gabaon, `that weren bisegid, senten to Josue, that dwellide than in tentis at Galgala, and seide to hym, Withdrawe not thin hondis fro the help of thi seruauntis; `stie thou soone, and delyuere vs, and helpe thou; for alle the kyngis of Amorreis, that dwelliden in the hilli places, camen togidere ayens vs.
7 Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
And Josue stiede fro Galgala, and al the oost of fiyters, `the strengeste men, `with hym.
8 Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
And the Lord seide to Josue, Drede thou not hem, for Y yaf hem in to thin hondis; noon of hem schal mow ayenstonde thee.
9 Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
Therfor Josue felde sodenli on hem, and stiede in al the nyyt fro Galgala;
10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
and the Lord `disturblide hem fro the face of Israel, and al to-brak with greet veniaunce in Gabaon. And Josue pursuede hem bi the weie of the stiyng of Betheron, and smoot `til to Azecha and Maceda.
11 Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
And whanne thei fledden the sones of Israel, and weren in the goyng doun of Betheron, the Lord sente grete stoonus on hem fro heuene, til to Azecha; and many mo weren deed bi the `stoonys of hail, than thei whiche the sones of Israel `smytiden bi swerd.
12 Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
Thanne Josue spak to the Lord, in the dai in which he bitook Amorrey in the siyt of the sones of Israel; and Josue seide bifore hem, Sunne, be thou not mouyd ayens Gabaon, and the moone ayens the valei of Hailon.
13 Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
And the sunne and the moone stoden, til the folc of God vengide it silf of hise enemyes. Whether this is not writun in the book of iust men? And so the sunne stood in the myddis of heuene, and hastide not to go doun in the space of o dai; so long a dai was not bifore and aftirward;
14 Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
for the Lord obeiede to the vois of man, and fauyt for Israel.
15 Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
And Josue turnede ayen, with al Israel, in to the tentis of Galgala.
16 Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
Forsothe fyue kyngis fledden, and hidden hem silf in the denne of the citee of Maceda.
17 Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
And it was teld to Josue, that fyue kyngis weren foundun hid in the denne of the citee of Maceda.
18 Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
Which Josue comaundide to felowis, and seide, Walewe ye grete stoonus to the `mouth of the denne, and putte ye witti men, that schulen kepe the closid kyngis; sotheli nyle ye stonde,
19 Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
but pursue ye the enemyes, and slee ye alle the laste of fleeris; and suffre ye not hem entre in to the strengthis of her citees, whiche enemyes youre Lord God bitook in to youre hondis.
20 Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
Therfor whanne the aduersaries weren betun with greet veniaunce, and weren almost wastid `til to deeth, thei that myyten fle Israel, entriden in to the strengthid citees.
21 Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
And al the oost turnede ayen hoole, and in hoole noumbre to Josue, in to Maceda, where the tentis weren thanne; and no man was hardi to grutche, `ether to make priuy noise, ayens the sones of Israel.
22 Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
And Josue comaundide, and seide, Opene ye the `mouth of the denne, and brynge forth to me the fyue kyngis that ben hid therynne.
23 Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
And the mynystris diden, as it was comaundid to hem; and thei brouyten forth to Josue fyue kyngis fro the denne; the kyng of Jerusalem, the kyng of Ebron, the kyng of Herymoth, the kyng of Lachis, the kyng of Eglon.
24 Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
And whanne thei weren led out to Josue, he clepide alle the men of Israel, and seide to the princes of the oost, that weren with hym, Go ye, and sette youre feet on the neckis of these kyngis. And whanne thei hadden go, and trediden the neckis of `the kyngis suget `to her feet,
25 Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
eft Josue seide to hem, Nyle ye drede, nethir `drede ye with ynne, be ye coumfortid, and be ye stronge; for the Lord schal do so to alle youre enemyes, ayens whiche ye schulen fiyte.
26 Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
And Josue smoot, and killide hem, and hangide on fyue trees; and thei weren hangid `til to euentid.
27 Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
And whanne the sunne yede doun, he comaundide to felowis, that thei schulden put hem doun fro the iebatis; and whanne thei weren put doun, thei `castiden forth hem in to the denne, in which thei weren hid; and thei puttiden grete stoonus on the mouth therof, whiche stoonus dwellen `til to present tyme.
28 Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
In the same dai Josue took also Maceda, and smoot bi the scharpnesse of swerd, and killide the kyng therof, and alle the dwelleris therof; he lefte not therynne, nameli, litle relikis; and he dide to the kyng of Maceda as he hadde do to the kyng of Jerico.
29 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
Forsothe Josue passide with al Israel fro Maceda in to Lempna, and fauyt ayens it,
30 Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
which the Lord bitook, with the kyng therof, in the hond of Israel; and thei smytiden the citee bi the scharpnesse of swerd, and alle the dwelleris therof, and leften not ony relikis therynne; and thei diden to the kyng of Lempna as thei hadden do to the kyng of Jerico.
31 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
Fro Lempna he passide with al Israel in to Lachis; and whanne the oost was disposid bi cumpas, he fauyt ayens it.
32 Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
And the Lord bitook Lachis in the hond of the sones of Israel; and he took it in the tothir dai, and smoot bi the scharpnesse of swerd, and ech man, that was therynne, as he hadde do to Lempna.
33 Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
In that time Yram, kyng of Gazar, stiede to helpe Lachis; whom Josue smoot, with al his puple, til to deeth.
34 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
And he passide fro Lachis in to Eglon,
35 Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
and cumpasside, and ouercam it in the same dai; and he smoot bi the scharpnesse of swerd alle men that weren therynne, bi alle thingis whiche he hadde do to Lachis.
36 Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
Also he stiede with al Israel fro Eglon in to Ebron, and fauyt ayens it,
37 Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
and took, and smoot bi the scharpnesse of swerd; and the kyng therof, and alle citees of that cuntrey, and alle men that dwelliden therynne; he lefte not ony relikis therynne; as he hadde do to Eglon so he dide also to Ebron, and wastide bi swerd alle thingis that weren therynne.
38 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
Fro thennus he turnyde in to Dabir, and took it, and wastide;
39 Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
and he smoot bi the scharpnesse of swerd the kyng therof, and alle tounnes `bi cumpas; he lefte not ony relikis therynne; as he hadde do to Ebron, and to Lempna, and to `the kyngis of tho, so he dide to Dabir, and to the kyng therof.
40 Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
And so Josue smoot al the `lond of the hillis, and of the south, and `of the feeld, and Asedoch with her kyngis; he lefte not therynne ony relikis, but he killide al thing that myyte brethe, as the Lord God of Israel comaundide to hym;
41 Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
fro Cades Barne `til to Gazan, and al the lond of Jesson, `til to Gabaon Josue took,
42 Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
and wastide with o fersnesse alle the kyngis, and `cuntreis of hem; for the Lord God of Israel fauyt for hym.
43 Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.
And he turnede ayen with al Israel to the place of tentis in Galgala.

< Yoswa 10 >